< Ezekieli 1 >

1 Tsiku lachisanu la mwezi wachinayi, chaka cha makumi atatu, ine ndinali pakati pa amʼndende mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara. Tsono kumwamba kunatsekuka ndipo ndinaona maonekedwe a Mulungu mʼmasomphenya.
Godine tridesete, mjeseca èetvrtoga, petoga dana, kad bijah meðu robljem na rijeci Hevaru, otvoriše se nebesa, i vidjeh utvare Božje.
2 Pa tsiku lachisanu la mwezi, chaka chachisanu Yehoyakini ali mʼndende,
Petoga dana toga mjeseca, pete godine otkako se zarobi car Joahin,
3 Yehova anayankhula ndi wansembe Ezekieli, mwana wa Buzi, mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara mʼdziko la Ababuloni. Dzanja la Yehova linali pa iye kumeneko.
Doðe rijeè Gospodnja Jezekilju sinu Vuzijevu, svešteniku, u zemlji Haldejskoj na rijeci Hevaru, i ondje doðe ruka Gospodnja nada nj.
4 Ndinayangʼana ndipo ndinangoona mphepo yamkuntho ikubwera kuchokera kumpoto. Panali mtambo waukulu wozunguliridwa ndi kuwala ndipo moto unali lawilawi kuchokera mu mtambowo. Pakati pa motowo pankaoneka ngati mkuwa wonyezimira.
I vidjeh, i gle, silan vjetar dolažaše od sjevera, i velik oblak i oganj koji se razgorijevaše, i oko njega svjetlost, a isred ognja kao jaka svjetlost;
5 Mʼkatikati mwa motowo munali zinthu zinayi zamaonekedwe a nyama. Thupi lawo limaoneka ngati la munthu
Isred njega još kao èetiri životinje, koje na oèi bijahu nalik na èovjeka;
6 koma chilichonse chinali ndi nkhope zinayi ndiponso mapiko anayi.
I u svake bijahu èetiri lica, i èetiri krila u svake;
7 Miyendo yake inali yowongoka; mapazi ake anali a ziboda ngati phazi la mwana wangʼombe. Ndipo zibodazo zinkawala ngati mkuwa wonyezimira.
I noge im bijahu prave, a u stopalu bijahu im noge kao u teleta; i sijevahu kao uglaðena mjed.
8 Mʼmunsi mwa mapiko awo kumbali zonse zinayi, nyamazo zinali ndi manja a munthu. Zonse zinayi zinali ndi nkhope ndi mapiko,
I ruke im bijahu èovjeèije pod krilima nad èetiri strane, i lica im i krila bijahu na èetiri strane.
9 ndipo mapiko awowo anakhudzana. Chilichonse chimapita molunjika kutsogolo; sizimatembenuka pamene zimayenda.
Sastavljena im bijahu krila jedno s drugim; i ne okretahu se iduæi, nego svaka iðaše naprema se.
10 Nkhope zawo zimaoneka motere: Chilichonse chinali ndi nkhope ya munthu, ndipo mbali ya kumanja chilichonse chinali ndi nkhope zinayi zosiyana motere: nkhope ya munthu, nkhope ya mkango ku dzanja lamanja, nkhope ya ngʼombe ku dzanja lamanzere, ndipo kumbuyo kwake nkhope ya chiwombankhanga.
I lice bijaše u sve èetiri lice èovjeèije i lice lavovo s desne strane, a s lijeve strane lice volujsko i lice orlovo u sve èetiri.
11 Ndi mʼmene zinalili nkhope zawo. Mapiko awo anali otambasukira mmwamba. Chamoyo chilichonse chinali ndi mapiko awiri okhudzana ndi mapiko a chinzake. Chinalinso ndi mapiko ena awiri ophimbira thupi lake.
I lica im i krila bijahu razdijeljena ozgo; u svake se dva krila sastavljahu jedno s drugim, a dva pokrivahu im tijelo.
12 Zamoyozo zinkayenda molunjika kutsogolo. Kulikonse kumene mzimu umazitsogolera kupita, nazonso zimapita kumeneko, osatembenuka pamene zikupita.
I svaka iðaše pravo naprema se; iðahu kuda duh iðaše, i ne okretahu se iduæi.
13 Pakati pa zamayozo panali chinthu chooneka ngati makala oyaka kapena miyuni yoyaka. Moto umayendayenda pakati pa zamayozo; wowala kwambiri, ndipo mphenzi zimatuluka pakati pawo.
I na oèi bijahu te životinje kao živo ugljevlje, gorahu na oèi kao svijeæe; taj oganj prolažaše izmeðu životinja i svijetljaše se, i iz ognja izlažaše munja.
14 Zamoyozo zinkathamanga uku ndi uko ngati kungʼanima kwa mphenzi.
I životinje trèahu i vraæahu se kao munja.
15 Pamene ndinali kuyangʼana zamoyozo, ndinangoona mikombero ndipo pansi pambali pa chamoyo chilichonse panali mkombero umodzi.
I kad gledah životinje, gle, toèak jedan bijaše na zemlji uza svaku životinju prema èetiri lica njihova.
16 Maonekedwe a mikomberoyo anali ngati mwala wonyezimira. Mikombero yonse inali yofanana ndipo mapangidwe awo anali ngati wongolowanalowana.
Oblièjem i napravom bijahu toèkovi kao boje hrisolitove, i sva èetiri bijahu jednaka, i oblièjem i napravom bijahu kao da je jedan toèak u drugom.
17 Mikombero ija poyenda inkatha kupita mbali iliyonse yomwe zamoyozo zinayangʼana popanda kutembenuka.
Kad iðahu, iðahu sva èetiri svaki na svoju stranu, i iduæi ne skretahu.
18 Marimu a mikomberoyo anali aatali ndi ochititsa mantha ndipo marimu onse anayi anali ndi maso ponseponse.
I naplaci im bijahu visoki strahota; i bijahu naplaci puni oèiju unaokolo u sva èetiri.
19 Zamoyozo zinkati zikamayenda, mikomberoyo imayendanso mʼmbali mwake; ndipo zamoyozo zinkati zikamakwera mmwamba, mikomberoyo imakweranso.
I kad iðahu životinje, iðahu i toèkovi uz njih; i kad se životinje podizahu od zemlje, podizahu se i toèkovi.
20 Kulikonse kumene mzimu wake unkazitsogolera, zamoyozo zinkapita komweko. Ndipo mikombero ija inkapita nawo pamodzi popeza kuti mzimu wa zamoyozo ndiwo umayendetsa mikombero ija.
Kuda duh iðaše, onamo iðahu, i podizahu se toèkovi prema njima, jer duh životinjski bješe u toèkovima.
21 Zamoyo zija zinkati zikamayenda mikombero imayendanso. Zamoyozo zimati zikayima, nayonso mikombero inkayima. Zamoyozo zinkati zikawuluka, mikomberonso imawuluka nazo pamodzi chifukwa mzimu wa zamoyo zija ndiwo umayendetsa mikombero ija.
Kad one iðahu, iðahu i oni; i kad one stajahu, stajahu i oni; i kad se one podizahu od zemlje, podizahu se i toèkovi prema njima, jer duh životinjski bješe u toèkovima.
22 Pamwamba pa mitu ya zamoyozo panali chinthu chonga thambo, lowala ndipo kunyezimira kwake ngati galasi loyangʼanitsa ku dzuwa, loyalidwa pamwamba pa mitu yake.
A nad glavama životinjama bijaše kao nebo, po viðenju kao kristal, strašno, razastrto ozgo nad glavama njihovijem.
23 Zamoyozo zinatambalitsa mapiko ake mʼmunsi mwa thambo lija, mapiko ake ena kumakhudzana, mapiko awiri kumaphimba thupi lake.
A pod tijem nebom bijahu im krila pružena, jedno prema drugom, a dva krila svakoj pokrivahu tijelo.
24 Pamene zamoyo zimayenda ndimamva phokoso la mapiko ake, ngati mkokomo wa madzi ambiri, ngati liwu la Wamphamvuzonse, ngati phokoso la gulu lankhondo. Zimati zikayima zinkagwetsa mapiko ake.
I èujah huku krila njihovijeh kad iðahu kao da bješe huka velike vode, kao glas svemoguæega i kao graja u okolu; i kad stajahu, spuštahu krila.
25 Ndipo panamveka mawu kuchokera pamwamba pa thambo la pa mitu ya zamoyo zija. Nthawi iyi nʼkuti zamoyozo zitayima ndi kugwetsa pansi mapiko ake.
I kad stavši spuštahu krila, èujaše se glas ozgo iz neba, koje bijaše nad glavama njihovijem.
26 Pamwamba pa thambo la pa mitu yake panali chinthu chimene chimaoneka ngati mpando waufumu wopangidwa ndi mwala wa safiro, ndipo pamwamba pa mpando waufumuwo panali chinthu chooneka ngati munthu.
I ozgo na onom nebu što im bijaše nad glavama, bijaše kao prijesto, po viðenju kao kamen safir, i na prijestolu bijaše po oblièju kao èovjek.
27 Ndinaona kuti mmwamba mwa chiwuno chake munali ngati chitsulo chowala konsekonse ngati moto. Mʼmunsi mwa chiwuno chake munalinso ngati moto wokhawokha. Kuwala kwa mphamvu kunamuzungulira munthuyo.
I vidjeh kao jaku svjetlost, i u njoj unutra kao oganj naokolo, od bedara gore, a od bedara dolje vidjeh kao oganj i svjetlost oko njega.
28 Kuwalako kunali ndi maonekedwe a utawaleza mʼmitambo tsiku limene kwagwa mvula. Umu ndi mmene ulemerero wa Yehova umaonekera. Pamene ndinawuona ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akundiyankhula.
Kao duga u oblaku kad je kiša, taka na oèi bijaše svjetlost unaokolo. To bijaše viðenje slave Božje na oèima; i kad vidjeh, padoh na lice svoje, i èuh glas nekoga koji govoraše.

< Ezekieli 1 >