< Ezekieli 7 >

1 Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
Potom doðe mi rijeè Gospodnja govoreæi:
2 “Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti: “Chimaliziro! Chimaliziro chafika ku ngodya zinayi za dziko.
Sine èovjeèji, ovako kaže Gospod Gospod za zemlju Izrailjevu: kraj, doðe kraj na èetiri strane zemlji.
3 Chimaliziro chili pa iwe tsopano. Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe. Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
Doðe ti kraj, i pustiæu gnjev svoj na te, i sudiæu ti po putovima tvojim i obratiæu na te sve gadove tvoje.
4 Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako. Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
I oko moje neæe te požaliti, niti æu se smilovati, nego æu putove tvoje obratiti na te, i gadovi æe tvoji biti usred tebe, i poznaæete da sam ja Gospod.
5 “Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: “Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo! Taona chikubwera!
Ovako veli Gospod Gospod: zlo, jedno zlo, evo ide.
6 Chimaliziro chafika! Chimaliziro chafika! Chiwonongeko chakugwera. Taona chafika!
Kraj doðe, kraj doðe, usta na te, evo doðe.
7 Inu anthu okhala mʼdziko, chiwonongeko chakugwerani. Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
Doðe jutro tebi, stanovnièe zemaljski, doðe vrijeme, približi se dan, kad æe biti polom a ne jeka gorska.
8 Ine ndili pafupi kukukwiyirani, ndipo ukali wanga udzathera pa iwe; Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
Sada æu odmah izliti jarost svoju na te, i navršiæu gnjev svoj na tebi, i sudiæu ti po tvojim putovima, i obratiæu na te sve gadove tvoje.
9 Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.
Neæe žaliti oko moje, niti æu se smilovati, daæu ti po putovima tvojim, i gadovi æe tvoji biti usred tebe, i poznaæete da sam ja Gospod, koji bije.
10 “Taona, tsikulo! Taona, lafika! Chiwonongeko chako chabwera. Ndodo yaphuka mphundu za maluwa. Kudzitama kwaphuka.
Evo dana, evo doðe, jutro nasta, procvate prut, ponositost napupi.
11 Chiwawa chasanduka ndodo yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo. Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo. Palibiretu ndipo sipadzapezeka munthu wowalira maliro.
Nasilje naraste prut bezakonja, niko neæe ostati od njih ni od mnoštva njihova ni od buke njihove, niti æe biti naricanja za njima.
12 Nthawi yafika! Tsiku layandikira! Munthu wogula asakondwere ndipo wogulitsa asamve chisoni, popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
Doðe vrijeme, prispje dan; ko kupuje neka se ne raduje, i ko prodaje neka ne žali, jer æe doæi gnjev na sve ljudstvo njihovo.
13 Wogulitsa sadzazipezanso zinthu zimene anagulitsa kwa wina chinkana onse awiri akanali ndi moyo, pakuti chilango chidzagwera onsewo ndipo sichingasinthike. Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense amene adzapulumutsa moyo wake.
Jer ko prodaje, neæe opet doæi do onoga što proda, ako i ostane živ; jer utvara za sve mnoštvo njihovo neæe se vratiti natrag, i niko se neæe okrijepiti bezakonjem svojim da saèuva život svoj.
14 “Lipenga lalira, ndipo zonse zakonzeka. Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo, pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
Zatrubiše u trube, i spremiše sve; ali nema nikoga da izaðe u boj, jer se gnjev moj raspalio na sve ljudstvo njihovo.
15 Ku bwalo kuli kumenyana ndipo mʼkati muli mliri ndi njala. Anthu okhala ku midzi adzafa ndi nkhondo. Iwo okhala ku mizinda adzafa ndi mliri ndi njala.
Napolju maè, a unutra pomor i glad; ko bude u polju, poginuæe od maèa; a ko bude u gradu, njega æe glad i pomor proždrijeti.
16 Onse amene adzapulumuka ndi kumakakhala ku mapiri, azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa. Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
A koji ih uteku, izbaviæe se i biæe po gorama kao golubovi iz dolina, svi æe uzdisati, svaki za svoje bezakonje.
17 Dzanja lililonse lidzalefuka, ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
Sve æe ruke klonuti i sva æe koljena postati kao voda.
18 Iwo adzavala ziguduli ndipo adzagwidwa ndi mantha. Adzakhala ndi nkhope zamanyazi ndipo mitu yawo adzameta mpala.
I pripasaæe oko sebe kostrijet, i drhat æe ih popasti, i na svakom æe licu biti stid, i sve æe im glave biti æelave.
19 “Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa. Siliva ndi golide wawo sizidzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala, kapena kukhala okhuta, pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
Srebro æe svoje pobacati po ulicama, i zlato æe njihovo biti kao neèistota; srebro njihovo i zlato njihovo neæe ih moæi izbaviti u dan gnjeva Gospodnjega; neæe nasititi duše svoje niti æe napuniti trbuha svojega, jer im je bezakonje njihovo spoticanje.
20 Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina. Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa kukhala zowanyansa.
Jer slavni nakit svoj obratiše na oholost, i naèiniše od njega likove gadova svojih, gnusobe svoje; zato uèinih da im je neèistota.
21 Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe. Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda ndi kudziyipitsa.
I daæu ga u ruke inostrancima da ga razgrabe, i bezbožnicima na zemlji da je plijen, i oskvrniæe ga.
22 Ine ndidzawalekerera anthuwo ndipo adzayipitsa malo anga apamtima. Adzalowamo ngati mbala ndi kuyipitsamo.
I odvratiæu lice svoje od njih, i oskvrniæe svetinju moju, i uæi æe u nju lupeži i oskvrniæe je.
23 “Konzani maunyolo, chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
Naèini verige, jer je zemlja puna krvnoga suda, i grad je pun nasilja.
24 Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa kuti idzalande nyumba zawo. Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
Zato æu dovesti najgore izmeðu naroda da naslijede kuæe njihove, i ukinuæu oholost silnijeh, i sveta mjesta njihova oskvrniæe se.
25 Nkhawa ikadzawafikira adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
Ide pogibao; oni æe tražiti mira, ali ga neæe biti.
26 Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake, ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake. Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri. Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo, ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
Nevolja za nevoljom dolaziæe, i glas za glasom stizaæe; i oni æe tražiti utvaru od proroka; zakona æe nestati u sveštenika i svjeta u staraca.
27 Mfumu idzalira, kalonga adzagwidwa ndi mantha. Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha. Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo, ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.
Car æe tužiti, i knezovi æe se obuæi u žalost, i ruke narodu zemaljskom drktaæe; uèiniæu im po putovima njihovijem i sudiæu im prema sudovima njihovijem; i poznaæe da sam ja Gospod.

< Ezekieli 7 >