< Ezekieli 5 >

1 Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
Potom, sine èovjeèji, uzmi nož oštar, britvu brijaèku uzmi, i pusti je po glavi svojoj i po bradi svojoj, pa uzmi mjerila i razdijeli.
2 Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
Treæinu sažezi ognjem usred grada, kad se navrše dani opsade, a drugu treæinu uzmi i isijeci maèem oko njega, a ostalu treæinu razmetni u vjetar, i ja æu izvuæi maè za njima.
3 Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
Ali uzmi malo, i zaveži u skut svoj.
4 Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
I od toga još uzmi i baci u oganj i sažezi ognjem; odatle æe izaæi oganj na sav dom Izrailjev.
5 Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
Ovako veli Gospod Gospod: ovo je Jerusalim koji postavih usred naroda i optoèih ga zemljama.
6 Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
Ali promijeni zakone moje na bezakonje veæma nego narodi, i uredbe moje veæma nego zemlje što su oko njega, jer odbaciše moje zakone, i ne hodiše po mojim uredbama.
7 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
Zato ovako veli Gospod Gospod: što postaste gori od naroda koji su oko vas, ne hodiste po mojim uredbama i ne izvršivaste mojih zakona, pa ni po uredbama naroda koji su oko vas ne èiniste,
8 “Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
Zato ovako veli Gospod Gospod: evo i mene na te, i izvršiæu usred tebe sudove na vidiku narodima;
9 Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
I uèiniæu ti što još nijesam uèinio niti æu više uèiniti za sve gadove tvoje.
10 Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
Zato oci æe jesti sinove usred tebe, i sinovi æe jesti oce svoje, i izvršiæu na tebi sudove i rasijaæu sav ostatak tvoj u sve vjetrove.
11 Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
Zato, tako ja živ bio, veli Gospod Gospod, što si oskvrnio moju svetinju svakojakim neèistotama svojim i svakojakim gadovima svojim, zato æu i ja tebe potrti, i neæe oko moje žaliti, niti æu se smilovati.
12 Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
Treæina æe tvoja pomrijeti od pomora, i od gladi æe izginuti usred tebe, a druga æe treæina pasti od maèa oko tebe, a treæinu æu rasijati u sve vjetrove, i izvuæi æu maè za njima.
13 “Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
I tako æe se izvršiti gnjev moj i namiriæu jarost svoju na njima i zadovoljiæu se, i oni æe poznati da sam ja Gospod govorio u revnosti svojoj kad izvršim gnjev svoj na njima.
14 “Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
I uèiniæu od tebe pustoš i rug meðu narodima koji su oko tebe pred svakim koji prolazi.
15 Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
I biæeš rug i sramota i nauk i èudo narodima što su oko tebe kad izvršim sudove na tebi gnjevom, jarošæu i ljutijem karanjem; ja Gospod rekoh;
16 Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
Kad pustim na vas ljute strijele gladi, koje æe biti smrtne, koje æu pustiti da vas zatrem, i kad glad navalim na vas i slomim vam potporu u hljebu,
17 Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”
Kad pustim na vas glad i ljute zvijeri, koje æe ti djecu izjesti; i kad pomor i krv proðu kroza te, i kad pustim maè na te. Ja Gospod rekoh.

< Ezekieli 5 >