< Ezekieli 40 >

1 Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu.
Sürgünlüğümüzün yirmi beşinci yılı, yılın başında, ayın onuncu günü, Yeruşalim Kenti'nin düşüşünün on dördüncü yılı, tam o gün RAB'bin eli beni yakalayıp oraya götürdü.
2 Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda.
Görümde Tanrı beni İsrail ülkesine götürüp çok yüksek bir dağın üzerine koydu. Dağın güneyinde kente benzer yapılar vardı.
3 Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera.
Tanrı beni oraya götürdü, tunca benzer bir adam gördüm. Elinde keten ip ve bir ölçü değneği tutarak kapının girişinde duruyordu.
4 Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”
Bana, “İnsanoğlu, gözlerinle gör, kulaklarınla işit, sana göstereceğim her şeye dikkat et” dedi, “Sen bunun için buraya getirildin. Göreceğin her şeyi İsrail halkına anlat.”
5 Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.
Tapınağı çepeçevre kuşatan bir duvar gördüm. Adamın elindeki ölçü değneğinin uzunluğu altı arşındı. Her arşına bir elin eni kadar uzunluk eklenmişti. Adam duvarı ölçtü; kalınlığı ve yüksekliği bir ölçü değneği kadardı.
6 Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu.
Sonra doğuya bakan kapıya gitti, basamakları çıkıp kapı eşiğini ölçtü. Eni bir ölçü değneği kadardı.
7 Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.
Bekçi odalarının her birinin uzunluğu ve genişliği bir ölçü değneği kadardı. Odaların arasındaki duvarın kalınlığı beş arşındı. Tapınağa bakan eyvanın kapı eşiği bir ölçü değneği uzunluktaydı.
8 Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu.
Eyvanı ölçtü;
9 Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.
genişliği sekiz arşın, kapı sövelerinin kalınlığı ikişer arşındı. Eyvan tapınağa bakıyordu.
10 Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana.
Doğu Kapısı'nın her yanında üçer bekçi odası vardı. Hepsi aynı ölçüdeydi. Odalar arasındaki duvarların ölçüsü de aynıydı.
11 Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka.
Adam kapının genişliğini ölçtü. Genişliği on, iç girişin genişliği on üç arşındı.
12 Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu.
Her bekçi odasının önünde bir arşın yüksekliğinde bir duvar vardı. Odalar kare şeklindeydi, kenarları altışar arşındı.
13 Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka.
Sonra girişleri karşı karşıya olan odaların arka duvarlarının arasını ölçtü; yirmi beş arşındı.
14 Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo.
Sütunları ölçtü, altmış arşındı. Kapının çevresindeki avlu sütunlara kadar uzanıyordu.
15 Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27.
Kapı girişinden eyvanın sonuna kadarki uzaklık elli arşındı.
16 Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.
Her iki yandaki bekçi odalarında, odalar arasındaki duvarlarda ve eyvanın çepeçevre duvarlarında içe bakan kafesli pencereler vardı. Bölme duvarları hurma ağacı motifleriyle kaplıydı.
17 Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo.
Adam bundan sonra beni dış avluya götürdü. Orada odalar ve dış avluyu çevreleyen taş yol vardı. Taş yol boyunca otuz oda vardı.
18 Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi.
Girişin iki yanındaki taş yolun genişliği kapıların uzunluğu kadardı. Bu aşağı taş yoldu.
19 Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Avlunun genişliğini aşağı girişten iç avlunun girişine dek ölçtü. Doğu ve kuzeydeki uzaklık yüz arşındı.
20 Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja.
Adam dış avlunun kuzeye bakan kapısının uzunluğunu ve genişliğini ölçtü.
21 Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
İki yandaki üçer bekçi odasının, aralarındaki duvarların ve eyvanın ölçüsü, birinci kapının ölçüsünün aynısıydı. Uzunluğu elli arşın, genişliği yirmi beş arşındı.
22 Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde.
Pencerelerin, eyvanın, hurma ağacı motiflerinin ölçüsü, doğuya bakan kapının ölçüsünün aynısıydı. Oraya yedi basamakla çıkılıyordu, eyvan bunların karşısındaydı.
23 Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Doğu Kapısı'na olduğu gibi, Kuzey Kapısı'na da bakan bir iç avlu kapısı vardı. Adam bu iki kapı arasındaki uzaklığı ölçtü, yüz arşındı.
24 Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija.
Adam beni güneye doğru götürdü. Orada güneye bakan bir kapı gördüm. Adam kapının sövelerini ve eyvanı ölçtü. Ölçüleri öbürlerinin aynısıydı.
25 Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13.
Öbürlerinde olduğu gibi, bu kapının ve eyvanın her yanında da pencereler vardı. Uzunluğu elli arşın, genişliği yirmi beş arşındı.
26 Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma.
Oraya yedi basamakla çıkılıyordu, eyvan bunların karşısındaydı. İki kapı sövesi de hurma ağacı motifleriyle kaplıydı.
27 Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
İç avlunun güneye bakan bir kapısı vardı. Adam bu kapıdan güneydeki dış kapıya kadar olan uzaklığı ölçtü, yüz arşındı.
28 Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija.
Adam beni Güney Kapısı'ndan iç avluya götürdü. Güney Kapısı'nı ölçtü. Ölçüleri öbürlerinin aynısıydı.
29 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13.
Bekçi odalarının, odalar arasındaki duvarların, eyvanın ölçüleri öbürlerinin aynısıydı. Dış duvarlarda ve eyvanın her yanında pencereler vardı. Girişin uzunluğu elli arşın, genişliği yirmi beş arşındı.
30 (Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake).
Eyvan dış avluya bakıyordu. Kapı söveleri hurma ağacı motifleriyle kaplıydı. Oraya sekiz basamakla çıkılıyordu.
31 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
32 Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija.
Adam beni doğudaki iç avluya götürdü. Oradaki kapıyı ölçtü. Ölçüleri öbürlerinin aynısıydı.
33 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Bekçi odalarının, odalar arasındaki duvarların, eyvanın ölçüleri öbürlerinin aynısıydı. Dış duvarlarda ve eyvanın her yanında pencereler vardı. Girişin uzunluğu elli arşın, genişliği yirmi beş arşındı.
34 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Eyvan dış avluya bakıyordu. Kapı söveleri hurma ağacı motifleriyle kaplıydı. Oraya sekiz basamakla çıkılıyordu.
35 Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija.
Sonra adam beni Kuzey Kapısı'na götürdü. Kapıyı ölçtü. Ölçüleri öbürlerinin aynısıydı.
36 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Bunun da bekçi odaları, aralarındaki duvarlar, eyvanı aynıydı. Kapının her yanında pencereler vardı. Girişin uzunluğu elli arşın, genişliği yirmi beş arşındı.
37 Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Eyvan dış avluya bakıyordu. Kapı söveleri her yanda hurma ağacı motifleriyle kaplıydı. Oraya sekiz basamakla çıkılıyordu.
38 Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza.
İç avlu girişlerindeki eyvanların yanında kapısı eyvana açılan bir oda vardı. Yakmalık sunular burada yıkanıyordu.
39 Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula.
Eyvanın her iki yanında ikişer masa vardı. Yakmalık sunu, günah sunusu ve suç sunusu için hayvanlar bu masaların üzerinde kesiliyordu.
40 Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero.
Eyvanın dış duvarının yanında, Kuzey Kapısı'nın basamaklarının her iki yanında ikişer olmak üzere dört masa daha vardı.
41 Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza.
Böylece kurbanlık hayvanların kesimi için kapının her iki yanında dörder olmak üzere sekiz masa vardı.
42 Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina.
Yakmalık sunular için yontma taştan dört masa vardı. Her masanın uzunluğu ve genişliği birer buçuk arşın, yüksekliği bir arşındı. Yakmalık sunularla öbür kurbanların kesiminde kullanılan aletleri bunların üzerine koyuyorlardı.
43 Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.
Odanın duvarlarına çifte çengeller asılmıştı; her biri bir el genişliğindeydi. Masalar sunulacak kurban eti için kullanılıyordu.
44 Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto.
İç kapının dış bölümünde, iç avluda iki oda vardı. Bunlardan biri Kuzey Kapısı'nın yanındaydı ve güneye bakıyordu, öbürü Güney Kapısı'nın yanındaydı ve kuzeye bakıyordu.
45 Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu,
Adam bana, “Güneye bakan oda tapınakta hizmet görecek kâhinler için” dedi,
46 ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”
“Kuzeye bakan oda da sunakta hizmet görecek kâhinler için. Bunlar Levi soyundan, RAB'be hizmet etmek için O'na yaklaşan Sadokoğulları'dır.”
47 Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
Adam avluyu ölçtü. Kareydi, uzunluğu yüz arşın, genişliği yüz arşındı. Sunak tapınağın önündeydi.
48 Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse.
Adam sonra beni tapınağın eyvanına götürüp eyvanın kapı sövelerini ölçtü. Her iki yandaki sövelerin genişliği beşer arşındı. Girişin genişliği on dört arşın, iki yandaki duvarların genişliği de üçer arşındı.
49 Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.
Eyvanın uzunluğu yirmi arşın, genişliği on iki arşındı. Oraya basamaklarla çıkılıyordu. Kapı sövelerinin her bir yanında sütunlar vardı.

< Ezekieli 40 >