< Ezekieli 40 >

1 Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu.
La vingt-cinquième année de notre captivité, au commencement de l'année, le dixième jour du mois, la quatorzième année après que la ville eut été ruinée, ce jour-là même, la main de Yahweh fut sur moi, et il m'emmena en ce lieu-là.
2 Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda.
Dans des visions divines il m'emmena au pays d'Israël, et il me plaça sur une montagne très élevée; et sur cette montagne, il y avait comme une construction de ville au midi.
3 Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera.
Quand il m'eut amené là, je vis un homme dont l'aspect était comme l'aspect de l'airain; dans sa main était un cordeau de lin et une canne à mesurer, et il se tenait dans le portique.
4 Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”
Cet homme me dit: " Fils de l'homme, regarde de tes yeux et écoute de tes oreilles, et applique ton cœur à tout ce que je vais te faire voir, car c'est pour qu'on te le fasse voir que tu as été amené ici. Fais connaître à la maison d'Israël tout ce que tu vas voir. "
5 Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.
Et voici qu'un mur extérieur entourait la maison de tous côtés, et l'homme avait à la main un roseau à mesurer de six coudées, chaque coudée étant d'une coudée et un palme. Il mesura la largeur de cette construction: elle était d'un roseau; et la hauteur: elle était d'un roseau.
6 Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu.
Puis il alla au portique dont la façade était dans la direction de l'orient, et il en monta les degrés; et il mesura le seuil du portique, qui était d'un roseau en largeur; savoir, le premier seuil, d'un roseau en largeur.
7 Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.
Chaque loge avait un roseau en longueur et un roseau en largeur; entre les loges, il y avait cinq coudées. Le seuil du portique, du côté du vestibule du portique, du côté de la maison, était d'un roseau.
8 Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu.
Il mesura le vestibule du portique, du côté de la maison; il était d'un roseau.
9 Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.
Il mesura encore le vestibule du portique: il avait huit coudées, et ses piliers deux coudées. Le vestibule du portique était du côté de la maison.
10 Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana.
Les loges du portique oriental étaient au nombre de trois d'un côté, et de trois de l'autre côté; toutes les trois avaient la même mesure, et les piliers de chaque côté avaient aussi la même mesure.
11 Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka.
Il mesura la largeur de l'ouverture du portique: elle était de dix coudées; et la longueur du portique de treize coudées.
12 Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu.
Il y avait devant les loges une clôture d'une coudée de chaque côté; et chaque loge avait six coudées d'un côté et six de l'autre.
13 Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka.
Et il mesura le portique du toit d'une loge jusqu'au toit de l'autre: vingt-cinq coudées en largeur, d'une porte jusqu'à l'autre porte.
14 Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo.
Il compta soixante coudées pour les piliers, et à ces piliers touchait le parvis qui entourait le portique.
15 Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27.
L'espace entre le devant de la porte d'entrée et le devant du vestibule intérieur de la porte était de cinquante coudées.
16 Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.
Il y avait aux loges, à leurs piliers, des fenêtres grillées du côté intérieur du portique, tout autour; il en était de même aux vestibules; et ainsi il y avait des fenêtres tout autour, donnant à l'intérieur; et aux pilastres il y avait des palmiers.
17 Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo.
Puis il me conduisit au parvis extérieur: et voici qu'il y avait des chambres et un pavé disposés tout autour du parvis; il y avait trente chambres le long du pavé.
18 Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi.
Le pavé longeait les portiques, correspondant à la longueur des portiques; c'était le pavé inférieur.
19 Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Il mesura la largeur du devant du portique inférieur jusqu'au devant du parvis intérieur: cent coudées, à l'orient et au septentrion.
20 Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja.
Quant au portique du parvis extérieur dont la façade est dans la direction du nord, il en mesura la longueur et la largeur,
21 Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
— ses loges, trois d'un côté et trois de l'autre; ses piliers et son vestibule ayant la même mesure que ceux du premier portique, — cinquante coudées en longueur et vingt-cinq coudées en largeur.
22 Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde.
Ses fenêtres, son vestibule et ses palmiers avaient la même mesure que ceux du portique dont la façade est dans la direction de l'orient; on y montait par sept degrés, et son vestibule était en face des degrés.
23 Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Il y avait un portique au parvis intérieur, en face du portique du septentrion comme en face de celui de l'orient; il mesura d'un portique à l'autre: cent coudées.
24 Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija.
Il me conduisit ensuite dans la direction du midi, et voici un portique dans la direction du midi; il en mesura les pilastres et le vestibule, qui avaient les mêmes dimensions
25 Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13.
— il avait tout autour, ainsi que son vestibule, des fenêtres pareilles aux autres fenêtres —: cinquante coudées en longueur et vingt-cinq coudées en largeur.
26 Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma.
On y montait par sept degrés, et son vestibule était en face des degrés; il y avait des palmiers à ses pilastres, l'un d'un côté, l'autre de l'autre.
27 Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Le parvis intérieur avait aussi un portique dans la direction du midi; il mesura d'un portique à l'autre dans la direction du midi: cent coudées.
28 Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija.
Il me conduisit dans le parvis intérieur par le portique du midi, et il mesura le portique qui était au midi, qui avait les mêmes dimensions
29 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13.
— ses loges, ses pilastres et son vestibule avaient les mêmes dimensions; et il avait, ainsi que son vestibule, des fenêtres tout autour —: cinquante coudées de longueur et vingt-cinq coudées de largeur.
30 (Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake).
Il y avait des vestibules tout autour, de vingt-cinq coudées en longueur et de cinq coudées en largeur.
31 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Son vestibule était du côté du parvis extérieur; il avait des palmiers à ses pilastres et huit degrés pour y monter.
32 Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija.
Puis il me conduisit, dans le parvis intérieur, vers la direction de l'orient, et il mesura le portique qui avait les mêmes dimensions
33 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
— ses loges, ses pilastres et son vestibule avaient les mêmes dimensions; et il avait, ainsi que son vestibule, des fenêtres tout autour — cinquante coudées en longueur et vingt-cinq coudées en largeur.
34 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Son vestibule touchait au parvis extérieur; il avait des palmiers à ses pilastres, d'un côté et de l'autre, et huit degrés pour y monter.
35 Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija.
Puis il me conduisit vers le portique du septentrion, et il y mesura les mêmes dimensions
36 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
— Il y avait à ses loges, à ses pilastres et à son vestibule des fenêtres tout autour —: cinquante coudées de longueur et vingt-cinq coudées de largeur.
37 Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Ses piliers touchaient au parvis extérieur; il y avait des palmiers sur ses pilastres et huit degrés pour y monter.
38 Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza.
Il y avait une chambre, avec sa porte, près des pilastres des portiques; c'est là qu'on lavait les holocaustes.
39 Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula.
Dans le vestibule du portique, il y avait deux tables d'un côté et deux tables de l'autre, sur lesquelles on devait immoler les victimes destinées à l'holocauste, au sacrifice pour le péché et au sacrifice pour le délit.
40 Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero.
Au côté extérieur, au septentrion pour celui qui montait à l'entrée du portique, il y avait deux tables, et de l'autre côté, vers le vestibule du portique, deux tables.
41 Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza.
Il se trouvait ainsi, sur les côtés de la porte, quatre tables d'une part et quatre tables de l'autre; en tout huit tables, sur lesquelles on devait immoler.
42 Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina.
Il y avait encore quatre tables servant aux holocaustes, en pierre de taille, longues d'une coudée et demie, larges d'une coudée et demie et hautes d'une coudée, sur lesquelles on posait les instruments avec lesquels on immolait les victimes destinées à l'holocauste et aux autres sacrifices.
43 Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.
Des crochets d'un palme étaient fixés tout autour de l'édifice; et la chair des sacrifices devait être placée sur les tables.
44 Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto.
En dehors du portique intérieur, il y avait les chambres des chantres, dans le parvis intérieur; celle qui était à côté du portique septentrional, avait sa façade dans la direction du midi; l'autre à côté du portique oriental, avait sa façade dans la direction du nord.
45 Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu,
Il me dit: " Cette chambre dont la façade est dans la direction du midi est pour les prêtres qui sont chargés du service de la maison.
46 ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”
Et la chambre dont la façade est dans la direction du nord est pour les prêtres chargés du service de l'autel. " Ce sont les fils de Sadoc qui, parmi les enfants de Lévi, s'approchent de Yahweh pour le servir.
47 Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
Puis il mesura le parvis, qui était carré, ayant cent coudées de longueur et cent coudées de largeur. L'autel était devant la maison.
48 Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse.
Il me conduisit ensuite vers le vestibule de la maison, et il mesura le pilier du vestibule: cinq coudées d'un côté et cinq coudées de l'autre; et la largeur du portique: trois coudées d'un côté et trois coudées de l'autre.
49 Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.
La longueur du vestibule était de vingt coudées, et la largeur de onze coudées, aux degrés par lesquels on y montait; et il y avait des colonnes près des piliers, l'une d'un côté, l'autre de l'autre.

< Ezekieli 40 >