< Ezekieli 39 >

1 “Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
Ti dakle, sine èovjeèji, prorokuj protiv Goga, i reci: ovako veli Gospod Gospod: evo me na te, Gože, kneže i glavo Mesehu i Tuvalu.
2 Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
I vratiæu te natrag i vodiæu te, i izvešæu te iz sjevernijeh krajeva i dovešæu te na gore Izrailjeve.
3 Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
I izbiæu ti luk tvoj iz lijeve ruke, i prosuæu ti iz desne ruke strijele.
4 Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
Na gorama æeš Izrailjevijem pasti ti i sve èete tvoje i narodi koji budu s tobom; pticama, svakojakim pticama krilatijem i zvijerima poljskim daæu te da te izjedu.
5 Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Na polju æeš pasti, jer ja rekoh, govori Gospod Gospod.
6 Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
I pustiæu oganj na Magoga i na one koji žive na ostrvima bez straha; i poznaæe da sam ja Gospod.
7 “Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
I sveto ime svoje obznaniæu usred naroda svojega Izrailja, i neæu više dati da se skvrni sveto ime moje, nego æe poznati narodi da sam ja Gospod, svetac u Izrailju.
8 Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
Evo, doæi æe, i zbiæe se, govori Gospod Gospod; to je dan za koji govorih.
9 “Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
Tada æe izaæi stanovnici gradova Izrailjevijeh, i naložiæe na oganj i spaliæe oružje i štitove i štitiæe, lukove i strijele, sulice i koplja, i ložiæe ih na oganj sedam godina.
10 Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
I neæe nositi drva iz polja, niti æe sjeæi u šumi, nego æe oružje ložiti na oganj, i oplijeniæe one koji ih plijeniše, i pootimaæe od onijeh koji od njih otimaše, govori Gospod Gospod.
11 “Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
I u to æu vrijeme dati Gogu mjesto za grob ondje u Izrailju, dolinu kojom se ide na istok k moru, i ona æe stisnuti usta putnicima; ondje æe biti pogreben Gog i sve mnoštvo njegovo i prozvaæe se dolina mnoštva Gogova.
12 “Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
I ukopavaæe ih dom Izrailjev sedam mjeseca, da bi oèistili zemlju.
13 Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
I ukopavaæe ih sav narod, i biæe im na slavu u onaj dan kad se proslavim, govori Gospod Gospod.
14 “Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
I odvojiæe ljude koji æe jednako iæi po zemlji i s onima koji prolaze ukopavati one koji bi ostali po zemlji da je oèiste; poslije sedam mjeseca tražiæe.
15 Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
I prohodiæe zemlju i iæi po njoj, i ko vidi kosti ljudske, naèiniæe kod njih znak, dokle ih ne ukopaju grobari u dolini mnoštva Gogova.
16 (Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
A i gradu æe biti ime Amona; i tako æe oèistiti zemlju.
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
Ti, dakle, sine èovjeèji, ovako govori Gospod Gospod, reci pticama, svakojakim pticama i svijem zvijerima poljskim: skupite se i hodite, saberite se sa svijeh strana na žrtvu moju, koju koljem za vas, na veliku žrtvu na gorama Izrailjevijem, i ješæete mesa i piæete krvi;
18 Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
Ješæete mesa junaèkoga i piæete krvi knezova zemaljskih, ovnova, jaganjaca i jaraca i telaca, sve ugojene stoke Vasanske.
19 Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
I ješæete pretiline da æete se nasititi, i piæete krvi da æete se opiti od žrtava mojih što æu vam naklati.
20 Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
I nasitiæete se za mojim stolom konja i konjika, junaka i svakojakih vojnika, govori Gospod Gospod.
21 “Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
I pustiæu slavu svoju meðu narode, i svi æe narodi vidjeti sud moj koji æu uèiniti i moju ruku koju æu dignuti na njih.
22 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
I poznaæe dom Izrailjev da sam ja Gospod Bog njihov, od onoga dana i poslije.
23 Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
I narodi æe poznati da se za svoje bezakonje zarobi dom Izrailjev, što meni zgriješiše, te sakrih lice svoje od njih, i dadoh ih u ruke neprijateljima njihovijem, i svi padoše od maèa.
24 Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
Po neèistoti njihovoj i po prijestupu njihovu uèinih im i sakrih lice svoje od njih.
25 “Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
Toga radi ovako govori Gospod Gospod: povratiæu roblje Jakovljevo i smilovaæu se svemu domu Izrailjevu i revnovaæu za sveto ime svoje,
26 Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
Pošto podnesu sramotu svoju i sve prijestupe svoje, kojima mi prestupiše dok sjeðahu u svojoj zemlji bez straha i nikoga ne bješe da ih plaši,
27 Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
Kad ih dovedem natrag iz naroda i saberem ih iz zemalja neprijatelja njihovijeh, i posvetim se u njima pred mnogim narodima.
28 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
I poznaæe da sam ja Gospod Bog njihov kad odvedavši ih u ropstvo meðu narode opet ih saberem u zemlju njihovu ne ostavivši ih nijednoga ondje.
29 Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
I neæu više kriti lica svojega od njih kad izlijem duh svoj na dom Izrailjev, govori Gospod Gospod.

< Ezekieli 39 >