< Ezekieli 35 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
And the word of the Lord was maad to me,
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
and he seide, Thou, sone of man, sette thi face ayens the hil of Seir; and thou schalt profesie to it, and thou schalt seie to it,
3 awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
The Lord God seith these thingis, Thou hil of Seir, lo! Y to thee; Y schal stretche forth myn hond on thee, and Y schal yyue thee desolat and forsakun.
4 Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Y schal distrie thi citees, and thou schalt be forsakun; and thou schalt wite, that Y am the Lord.
5 “Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
For thou were an enemye euerlastynge, and closidist togidere the sonis of Israel in to the hondis of swerd, in the tyme of her turment, in the tyme of the laste wickidnesse;
6 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
therfor Y lyue, seith the Lord God, for Y schal yyue thee to blood, and blood schal pursue thee; and sithen thou hatidist blood, blood schal pursue thee.
7 Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
And Y schal yyue the hil of Seir desolat and forsakun, and Y schal take awei fro it a goere and a comere ayen;
8 Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
and Y schal fille the hillis therof with the careyns of her slayn men. Men slayn by swerd schulen falle doun in thi litle hillis, and in thi valeys, and in thi strondis.
9 Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Y schal yyue thee in to euerlastynge wildirnessis, and thi citees schulen not be enhabitid; and ye schulen wite, that Y am the Lord God.
10 “Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
For thou seidist, Twei folkis and twei londis schulen be myne, and Y schal welde tho bi eritage, whanne the Lord was there;
11 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
therfor Y lyue, seith the Lord God, for Y schal do bi thi wraththe, and bi thin enuye, which thou didist, hatinge hem, and Y schal be made knowun bi hem, whanne Y schal deme thee;
12 Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
and thou schalt wite, that Y am the Lord. Y herde alle thi schenschipis, whiche thou spakist of the hillis of Israel, and seidist, The hillis of Israel ben forsakun, and ben youun to vs, for to deuoure.
13 Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
And ye han rise on me with youre mouth, and ye han deprauyd ayens me; Y herde youre wordis.
14 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
The Lord God seith these thingis, While al the lond is glad, Y schal turne thee in to wildernesse.
15 Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
As thou haddist ioie on the eritage of the hous of Israel, for it was distried, so Y schal do to thee; the hil of Seir schal be distried, and al Ydumee; and thei schulen wite, that Y am the Lord.

< Ezekieli 35 >