< Ezekieli 32 >

1 Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti:
W dwunastym roku, w dwunastym miesiącu, pierwszego [dnia] tego miesiąca, doszło do mnie słowo PANA mówiące:
2 “Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti, “Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu. Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja. Umakhuvula mʼmitsinje yako, kuvundula madzi ndi mapazi ako ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.
Synu człowieczy, podnieś lament nad faraonem, królem Egiptu, i powiedz mu: Jesteś podobny do młodego lwa pośród narodów, jesteś jak wieloryb w morzu, gdyż bujając po swoich rzekach, mącisz wody swoimi nogami i mieszasz jego rzeki.
3 “Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri, ndidzakuponyera khoka langa ndi kukugwira mu ukonde wanga.
Tak mówi Pan BÓG: Rozciągnę nad tobą swoją sieć w zgromadzeniu wielu narodów, a wyciągną cię w swoim niewodzie.
4 Ndidzakuponya ku mtunda ndi kukutayira pansi. Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe, ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.
I zostawię cię na ziemi, porzucę cię na otwartym polu i sprawię, że obsiądzie cię wszelkie ptactwo niebieskie, i nasycę tobą zwierzęta całej ziemi.
5 Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.
Rozrzucę twoje ciało po górach i napełnię doliny twoją wysokością.
6 Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako, mpaka kumapiri komwe, ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.
Twoją ziemię, w której pływasz, napoję twoją krwią aż do gór, i rzeki będą napełnione tobą.
7 Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba ndikudetsa nyenyezi zake. Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo, ndipo mwezi sudzawala.
A gdy cię zgaszę, zakryję niebo i zaciemnię jego gwiazdy, słońce zakryję chmurą, a księżyc nie da swego światła.
8 Zowala zonse zamumlengalenga ndidzazizimitsa; ndidzachititsa mdima pa dziko lako, akutero Ambuye Yehova.
Wszystkie świecące światła na niebie zaciemnię z twojego powodu i sprowadzę ciemność na twoją ziemię, mówi Pan BÓG.
9 Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, ku mayiko amene iwe sunawadziwe.
Nadto zasmucę serce wielu narodów, gdy za moją sprawą nadejdzie [wieść] o twoim zniszczeniu do narodów, do ziem, których nie znałeś.
10 Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe, ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo. Pa nthawi ya kugwa kwako, aliyense wa iwo adzanjenjemera moyo wake wonse.
Tak, sprawię, że zdumieje się nad tobą wiele narodów, a ich królowie bardzo się zatrwożą z twojego powodu, gdy zacznę wywijać swoim mieczem przed nimi; i będą drżeć nieustannie – każdy o swoją duszę – w dniu twego upadku.
11 “‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti, “‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni lidzabwera kudzalimbana nawe.
Tak bowiem mówi Pan BÓG: Miecz króla Babilonu spadnie na ciebie.
12 Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe ndi lupanga la anthu amphamvu, anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu. Adzathetsa kunyada kwa Igupto, ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.
Mieczami mocarzy powalę twoją rzeszę. Najokrutniejsi ze wszystkich narodów zniszczą pychę Egiptu i będzie zgładzone całe jego mnóstwo.
13 Ndidzawononga ziweto zake zonse zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri. Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.
Wytępię całe jego bydło znad wielkich wód, tak że nie zamąci ich stopa ludzka ani nie zamąci ich kopyto bydlęcia.
14 Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta, akutero Ambuye Yehova.
Wtedy sprawię, że ich wody uspokoją się, a ich rzeki popłyną jak oliwa – mówi Pan BÓG.
15 Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja; ndikadzawononga dziko lonse ndi kukantha onse okhala kumeneko, adzadziwa kuti ndine Yehova.’
Gdy zamienię ziemię Egiptu w spustoszenie, a ziemia zostanie pozbawiona tego, co ją napełnia, gdy pobiję wszystkich jej mieszkańców, wtedy poznają, że ja jestem PANEM.
16 “Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”
To jest lament, który podniosą nad nią. Córki narodów będą ją opłakiwać. Nad Egiptem i nad całą jego rzeszą będą lamentować, mówi Pan BÓG.
17 Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti:
Potem, w dwunastym roku, piętnastego [dnia] miesiąca, doszło do mnie słowo PANA mówiące;
18 “Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa.
Synu człowieczy, zawódź nad rzeszą Egiptu, zepchnij ją i córki tych sławnych narodów aż do najniższych stron ziemi, do tych, którzy zstępują do dołu.
19 Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’
I [mów]: Kogo przewyższasz pięknem? Zstąp i połóż się z nieobrzezanymi.
20 Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo.
Padną pośród pobitych mieczem; został wydany pod miecz, wywleczcie go z całą jego rzeszą.
21 Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’ (Sheol h7585)
Najmocniejsi z mocarzy będą do niego mówić spośród piekła wraz z jego pomocnikami. Zstąpili [tam], leżą z nieobrzezanymi pobitymi mieczem. (Sheol h7585)
22 “Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo.
Tam [jest] Assur i cała jego rzesza, wokół niego [są] jego groby; wszyscy ci pobici upadli od miecza.
23 Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.
Ich groby są położone po stronach dołu, jego rzesza jest dokoła jego grobu. Ci wszyscy pobici polegli od miecza, ci, którzy szerzyli postrach w ziemi żyjących.
24 “Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda.
Tam [jest] Elam i cała jego rzesza dokoła jego grobu, ci wszyscy pobici upadli od miecza i zstąpili nieobrzezani do najgłębszych stron ziemi; szerzyli swój postrach w ziemi żyjących. Już znoszą swoją hańbę z tymi, którzy zstępują do dołu.
25 Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.
Postawili mu łoże pośród pobitych z całą jego rzeszą, wokół niego są jego groby. Wszyscy ci nieobrzezani są pobici mieczem. Ich postrach szerzył się w ziemi żyjących, ale już ponoszą swoją hańbę z tymi, którzy zstąpili do dołu, a wśród pobitych zostali położeni.
26 “Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo.
Tam [jest] Meszek, Tubal i cała jego rzesza, i wokoło niego jego groby. Ci wszyscy nieobrzezani [zostali] pobici mieczem, choć szerzyli swój postrach w ziemi żyjących.
27 Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo. (Sheol h7585)
Oni jednak nie będą leżeć z mocarzami, którzy spośród nieobrzezanych upadli i zstąpili do grobu ze swym orężem wojennym i położono im miecze pod głowy. Ich nieprawości zaś zostaną na ich kościach, chociaż byli postrachem dla mocarzy w ziemi żyjących. (Sheol h7585)
28 “Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.
I ty będziesz skruszony wśród nieobrzezanych, i będziesz leżał pośród pobitych mieczem.
29 “Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.
Tam [jest] Edom, jego królowie i wszyscy jego książęta, którzy zostali położeni ze swoją mocą i wraz z pobitymi mieczem. Ci będą leżeć z nieobrzezanymi i z tymi, którzy zstępują do dołu.
30 “Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.
Tam [są] wszyscy książęta północy i wszyscy Sydończycy, którzy zstępują do pobitych; wstydzą się swego postrachu, jaki szerzyli swoją mocą, i leżą nieobrzezani z pobitymi mieczem. Znoszą swoją hańbę z tymi, którzy zstępują do dołu.
31 “Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Zobaczy ich faraon i ucieszy się z całej swojej rzeszy, którą pobito mieczem, faraon i całe jego wojsko – mówi Pan BÓG.
32 Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
Szerzyłem bowiem swój postrach w ziemi żyjących i zostanie położony wśród nieobrzezanych z pobitymi mieczem – faraon i cała jego rzesza – mówi Pan BÓG.

< Ezekieli 32 >