< Ezekieli 3 >

1 Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.”
And He said unto me: 'Son of man, eat that which thou findest; eat this roll, and go, speak unto the house of Israel.'
2 Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.
So I opened my mouth, and He caused me to eat that roll.
3 Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.
And He said unto me: 'Son of man, cause thy belly to eat, and fill thy bowels with this roll that I give thee.' Then did I eat it; and it was in my mouth as honey for sweetness.
4 Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga.
And He said unto me: 'Son of man, go, get thee unto the house of Israel, and speak with My words unto them.
5 Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli.
For thou art not sent to a people of an unintelligible speech and of a slow tongue, but to the house of Israel;
6 Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera.
not to many peoples of an unintelligible speech and of a slow tongue, whose words thou canst not understand. Surely, if I sent thee to them, they would hearken unto thee.
7 Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma.
But the house of Israel will not consent to hearken unto thee; for they consent not to hearken unto Me; for all the house of Israel are of a hard forehead and of a stiff heart.
8 Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo.
Behold, I have made thy face hard against their faces, and thy forehead hard against their foreheads.
9 Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”
As an adamant harder than flint have I made thy forehead; fear them not, neither be dismayed at their looks, for they are a rebellious house.'
10 Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako.
Moreover He said unto me: 'Son of man, all My words that I shall speak unto thee receive in thy heart, and hear with thine ears.
11 Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”
And go, get thee to them of the captivity, unto the children of thy people, and speak unto them, and tell them: Thus saith the Lord GOD; whether they will hear, or whether they will forbear.'
12 Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!”
Then a spirit lifted me up, and I heard behind me the voice of a great rushing: 'Blessed be the glory of the LORD from His place';
13 Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu.
also the noise of the wings of the living creatures as they touched one another, and the noise of the wheels beside them, even the noise of a great rushing.
14 Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu.
So a spirit lifted me up, and took me away; and I went in bitterness, in the heat of my spirit, and the hand of the LORD was strong upon me.
15 Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.
Then I came to them of the captivity at Tel-abib, that dwelt by the river Chebar, and I sat where they sat; and I remained there appalled among them seven days.
16 Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti,
And it came to pass at the end of seven days, that the word of the LORD came unto me, saying:
17 “Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza.
'Son of man, I have appointed thee a watchman unto the house of Israel; and when thou shalt hear a word at My mouth, thou shalt give them warning from Me.
18 Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
When I say unto the wicked: Thou shalt surely die; and thou givest him not warning, nor speakest to warn the wicked from his wicked way, to save his life; the same wicked man shall die in his iniquity, but his blood will I require at thy hand.
19 Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
Yet if thou warn the wicked, and he turn not from his wickedness, nor from his wicked way, he shall die in his iniquity; but thou hast delivered thy soul.
20 “Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
Again, when a righteous man doth turn from his righteousness, and commit iniquity, I will lay a stumblingblock before him, he shall die; because thou hast not given him warning, he shall die in his sin, and his righteous deeds which he hath done shall not be remembered; but his blood will I require at thy hand.
21 Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”
Nevertheless if thou warn the righteous man, that the righteous sin not, and he doth not sin, he shall surely live, because he took warning; and thou hast delivered thy soul.'
22 Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.”
And the hand of the LORD came there upon me; and He said unto me: 'Arise, go forth into the plain, and I will there speak with thee.'
23 Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.
Then I arose, and went forth into the plain; and, behold, the glory of the LORD stood there, as the glory which I saw by the river Chebar; and I fell on my face.
24 Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako.
Then spirit entered into me, and set me upon my feet; and He spoke with me, and said unto me: 'Go, shut thyself within thy house.
25 Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu.
But thou, son of man, behold, bands shall be put upon thee, and thou shalt be bound with them, and thou shalt not go out among them;
26 Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu.
and I will make thy tongue cleave to the roof of thy mouth, that thou shalt be dumb, and shalt not be to them a reprover; for they are a rebellious house.
27 Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”
But when I speak with thee, I will open thy mouth, and thou shalt say unto them: Thus saith the Lord GOD; he that heareth, let him hear, and he that forbeareth, let him forbear; for they are a rebellious house.

< Ezekieli 3 >