< Ezekieli 25 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
Opet mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira anthu a ku Amoni ndipo unenere mowadzudzula.
Sine èovjeèji, okreni lice svoje prema sinovima Amonovijem i prorokuj na njih.
3 Awawuze kuti, ‘Inu anthu a ku Amoni, imvani zimene Ambuye Yehova akunena. Iye akuti: Inu munanena mawu onyoza pamene Nyumba yanga yopatulika inkayipitsidwa. Munanyozanso dziko la Israeli pamene linaguga ndiponso anthu a ku Yuda pamene anatengedwa ukapolo.
I reci sinovima Amonovijem: èujte rijeè Gospoda Gospoda; ovako veli Gospod Gospod: što si govorio: aha! za svetinju moju, što se oskvrni, i za zemlju Izrailjevu, što opustje, i za dom Judin, što otide u ropstvo;
4 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu akummawa ngati cholowa chawo. Iwo adzamanga misasa yawo ndi kukhoma matenti awo pakati panu. Adzadya zipatso zanu ndi kumwa mkaka wanu.
Zato, evo, ja æu te dati u našljedstvo istoènijem narodima, i pogradiæe u tebi dvorove sebi, i naèiniæe sebi kolibe u tebi; oni æe jesti plodove tvoje i piti mlijeko tvoje.
5 Ndidzasandutsa Raba kuti akhale busa la ngamira ndi mizinda ya Aamoni kuti ikhale makola a nkhosa. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
I od Rave æu naèiniti obor kamilama i od zemlje sinova Amonovijeh tor ovèji, i poznaæete da sam ja Gospod.
6 Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu munawomba mʼmanja ndi kumalumphalumpha. Munkakondwa mu mtima mwanu pamene munkanyoza dziko la Israeli.
Jer ovako veli Gospod Gospod: što si pljeskao rukama i lupao nogom i veselio se iz srca što si opustošio svu zemlju Izrailjevu,
7 Nʼchifukwa chake ndidzatambasula dzanja langa kuti ndikulangeni, ndipo ndidzakuperekani kuti mukhale chofunkha cha anthu a mitundu ina. Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukufafanizani mʼmayiko onse. Ndidzakuwonongani, ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova!’”
Zato, evo, ja æu dignuti ruku svoju na te, i daæu te narodima da te plijene, i istrijebiæu te izmeðu naroda i zatræu te izmeðu zemalja, i iskorijeniæu te, i poznaæeš da sam ja Gospod.
8 “Ambuye Yehova akuti, ‘Anthu a ku Mowabu ndi a ku Seiri ananena kuti anthu a ku Yuda ali ngati mayiko ena onse.’
Ovako veli Gospod Gospod: što govori Moav i Sir: eto, dom je Judin kao svi narodi;
9 Nʼchifukwa chake ndidzagumula mbali ina ya Mowabu, kuyambira ku mizinda yake ya kumalire; mizinda yokongola ya Beti-Yesimoti, Baala-Meoni ndi Kiriataimu.
Zato, evo, ja æu otvoriti stranu Moavovu od gradova, od gradova na meði, krasnu zemlju Vet-jesimotsku, Valmeonsku i Kirijatajimsku,
10 Ndidzapereka Amowabu pamodzi ndi Aamoni mʼmanja mwa anthu akummawa kotero kuti Aamoni adzayiwalikiratu pakati pa anthu a mitundu ina.
Narodima istoènijem iza zemlje sinova Amonovijeh, i daæu im je u našljedstvo da nema spomena sinovima Amonovijem meðu narodima.
11 Ndidzawalangadi Amowabuwo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
I na Moavcima æu izvršiti svoje sudove, i poznaæe da sam ja Gospod.
12 “Ambuye Yehova akuti, ‘Pakuti Edomu analipsira Ayuda, ndiye kuti analakwa kwambiri pochita zimenezi.
Ovako veli Gospod Gospod: što se Edom osveti domu Judinu i teško skrivi osvetivši im se,
13 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kulanga Edomu ndi kupha anthu ake ndiponso nyama zawo. Ndidzawonongeratu Edomu ndipo adzaphedwa ndi lupanga kuchokera ku Temani mpaka ku Dedani.
Zato ovako veli Gospod Gospod: dignuæu ruku svoju na Edomsku i istrijebiæu iz nje i ljude i stoku, i obratiæu je u pustoš, od Temana do Dedana pašæe od maèa.
14 Ndidzalanga Edomu ndi dzanja la anthu anga Aisraeli. Adzalanga anthu a ku Edomu molingana ndi mkwiyo ndi ukali wanga. Choncho adzaona kulipsira kwanga akutero Ambuye Yehova.’”
I osvetiæu se Edomcima rukom naroda svojega Izrailja, i uèiniæe s Edomcima po gnjevu mojemu i po jarosti mojoj, i poznaæe moju osvetu, govori Gospod Gospod.
15 “Ambuye Yehova akuti, ‘Afilisti analanga anthu anga mwankhanza ndi kuwalipsira.
Ovako veli Gospod Gospod: što Filisteji radiše iz osvete, i osvetiše se radujuæi se iz srca i potiruæi iz stare mržnje,
16 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kukantha Afilistiwo. Ndidzafafaniza Akereti ndi kuwononga iwo amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.
Zato ovako veli Gospod Gospod: evo ja æu dignuti ruku svoju na Filisteje, i istrijebiæu Hereteje, i potræu ostatak od primorja.
17 Ndidzawabwezera chilango choopsa ndipo ndidzawalanga mu mkwiyo wanga. Ndikadzawalipsira ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
I uèiniæu na njima veliku osvetu karanjem gnjevnijem, i poznaæe da sam ja Gospod kad izvršim osvetu svoju na njima.

< Ezekieli 25 >