< Ezekieli 18 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
Opet mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
2 “Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
Šta hoæete vi koji govorite prièu o zemlji Izrailjevoj govoreæi: oci jedoše kiselo grožðe, a sinovima trnu zubi?
3 “Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
Tako ja bio živ, govori Gospod Gospod, neæete više govoriti te prièe u Izrailju.
4 Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
Gle, sve su duše moje, kako duša oèina tako i duša sinovlja moja je, koja duša zgriješi ona æe poginuti.
5 “Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
Jer ako je ko pravedan i èini sud i pravdu,
6 Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
Na gorama ne jede i oèiju svojih ne podiže ka gadnijem bogovima doma Izrailjeva, i ne skvrni žene bližnjega svojega i ne ide k ženi odvojenoj radi neèistote,
7 Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
I nikome ne èini nasilja, zalog dužniku svojemu vraæa, ništa ne otima, hljeb svoj daje gladnome i gologa odijeva,
8 Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
Ne daje na dobit i ne uzima pridavka, od nepravde usteže ruku svoju, i pravo sudi izmeðu jednoga èovjeka i drugoga,
9 Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
Po uredbama mojim hodi, i drži zakone moje tvoreæi istinu; taj je pravedan, doista æe živjeti, govori Gospod Gospod.
10 “Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
Ako rodi sina lupeža, koji bi krv proljevao ili bi èinio tako što,
11 Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
A ne bi èinio svega onoga, nego bi jeo na gorama, i ženu bližnjega svojega skvrnio,
12 Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
Siromahu i ubogome nasilje èinio, otimao što, zaloga ne bi vraæao, i ka gadnijem bogovima podizao bi oèi svoje èineæi gad,
13 Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
Davao bi na dobit, i uzimao pridavak; hoæe li taj živjeti? Neæe živjeti; uèinio je sve te gadove, doista æe poginuti, krv æe njegova na njemu biti.
14 “Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
Ali gle, ako rodi sina koji bi vidio sve grijehe oca svojega što èini, i uzeo bi na um, te ne bi èinio onako,
15 “Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
Ne bi jeo na gorama, niti bi oèiju svojih podizao ka gadnijem bogovima doma Izrailjeva, žene bližnjega svojega ne bi skvrnio,
16 Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
I nikome ne bi èinio nasilja, zaloga ne bi uzimao i ne bi ništa otimao, davao bi hljeb svoj gladnome i gologa bi odijevao,
17 Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
Od siromaha bi ustezao ruku svoju, ne bi uzimao dobiti ni pridavka, zakone bi moje izvršivao i po uredbama mojim hodio; taj neæe poginuti za bezakonje oca svojega, doista æe živjeti.
18 Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
A otac njegov, što je èinio nasilje, otimao od brata svojega i èinio što nije dobro u narodu svom, gle, on æe poginuti za svoje bezakonje.
19 “Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
Ali govorite: zašto da ne nosi sin bezakonja oèina? Jer sin èini sud i pravdu, sve uredbe moje drži i izvršuje; doista æe živjeti.
20 Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
Koja duša zgriješi ona æe umrijeti, sin neæe nositi bezakonja oèina niti æe otac nositi bezakonja sinovljega; na pravedniku æe biti pravda njegova, a na bezbožniku æe biti bezbožnost njegova.
21 “‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
Ako li bi se bezbožnik obratio od svijeh grijeha svojih koje uèini, i držao bi sve uredbe moje i tvorio sud i pravdu, doista æe živjeti, neæe poginuti.
22 Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
Bezakonja njegova što ih je god uèinio neæe mu se više spominjati, u pravdi svojoj koju èini živjeæe.
23 Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
Eda li je meni milo da pogine bezbožnik? govori Gospod, a ne da se odvrati od putova svojih i bude živ?
24 “‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
Ali kad bi se pravednik odvratio od pravde svoje i èinio nepravdu, i radio po svijem gadovima koje èini bezbožnik, hoæe li on živjeti? pravedna djela njegova, što je god èinio, neæe se spomenuti; za bezakonje svoje koje uèini i za grijeh svoj kojim zgriješi poginuæe.
25 “Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
Još govorite: nije prav put Gospodnji. Èujte, dome Izrailjev, moj li put nije prav? nijesu li vaši putovi nepravi?
26 Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
Kad se pravednik odvrati od pravde svoje i èini zlo i umre zato, umrijeæe za zlo svoje koje uèini.
27 Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
A kad se bezbožnik odvrati od bezbožnosti svoje koju je èinio, i èini sud i pravdu, on æe saèuvati u životu dušu svoju.
28 Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
Jer uzevši na um vrati se od svijeh bezakonja svojih koja uèini; doista æe živjeti, i neæe poginuti.
29 Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
Ali dom Izrailjev veli: put Gospodnji nije prav. Moji li putovi nijesu pravi? dome Izrailjev, nijesu li vaši putovi nepravi?
30 “Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
Zato, dome Izrailjev, sudiæu vam svakome po putovima njegovijem, govori Gospod; obratite se i proðite se svijeh grijeha svojih, i neæe vam bezakonje biti na spoticanje.
31 Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
Odbacite od sebe sva bezakonja koja èiniste, i naèinite sebi novo srce i nov duh; i zašto da mrete? dome Izrailjev.
32 Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”
Jer mi nije mila smrt onoga koji mre, govori Gospod Gospod; obratite se dakle i budite živi.

< Ezekieli 18 >