< Ezekieli 17 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
I doszło do mnie słowo PANA mówiące:
2 “Iwe mwana wa munthu, aphere mwambi anthu a Israeli ndi kuwawuza fanizo.
Synu człowieczy, zadaj zagadkę i opowiedz domowi Izraela przypowieść;
3 Uwawuze kuti Ambuye Yehova akuti, chiwombankhanga chachikulu, cha mapiko amphamvu, nthenga zitalizitali zamathothomathotho chinabwera ku Lebanoni. Chinagwira nthambi ya pamwamba pa mtengo wa mkungudza.
I powiedz: Tak mówi Pan BÓG: Wielki orzeł o wielkich i długich skrzydłach, pełen pstrego pierza, przyleciał nad Liban i wziął wierzchołek cedru.
4 Chinabudula msonga yeniyeni ya nthambiyo nʼkupita nayo ku dziko lamalonda ndipo anakayika mu mzinda wa anthu amalonda.
Ułamał koniec jego pędów, zaniósł go do ziemi kupieckiej i złożył go w mieście kupieckim.
5 “‘Kenaka chinatenga mbewu ina ya mʼdziko ndi kukayidzala ku malo a chonde kumene kunali madzi ambiri. Anayidzala ngati mmene amadzalira mtengo wa msondozi.
Wziął też nasienie tej ziemi i zasadził na urodzajnym polu; umieścił je nad wielkimi wodami jak wierzbę.
6 Ndipo inaphuka nisanduka mtengo wa mpesa wotambalala chamʼmunsi. Nthambi zake zinaloza mmwamba kumene kunali chiwombankhangacho, koma mizu yake inalowa pansi. Kotero unakhala mtengo wamphesa ndipo unasanduka wa nthambi ndiponso wa masamba ambiri.
I urosło, i stało się bujną winoroślą, [choć] niskiego wzrostu; jej latorośle zwracały się ku niemu, a korzenie były mu poddane. I stało się winoroślą, która wydała latorośle i wypuściła pędy.
7 “‘Koma panali chiwombankhanga chinanso chachikulu, cha mapiko amphamvu ndi cha nthenga zambiri. Tsopano mtengo wamphesa uja unakhotetsera mizu yake kwa chiwombankhangacho kuchokera pa malo amene unadzalidwa ndipo unatambalitsa nthambi zake kwa chiwombankhangacho kufuna kuthiridwa madzi.
Ale był inny wielki orzeł o wielkich skrzydłach i gęstym pierzu, a oto ta winorośl zwróciła swoje korzenie ku niemu i rozciągnęła swe latorośle do niego, aby on ją nawadniał z bruzd swego sadu.
8 Koma mtengowo unadzalidwa kale pa nthaka yabwino mʼmbali mwa madzi kuti ukhale ndi nthambi zambiri, ubereke zipatso ndi kukhala wokongola.’
A [była] przecież zasadzona na dobrym polu, nad wielkimi wodami, aby wypuściła latorośle, wydała owoc i stała się wspaniałą winoroślą.
9 “Ukawawuze Aisraeli kuti, ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Kodi udzakula bwino? Kodi chiwombankhanga chija sichidzawuzula mizu ndi kubudula nthambi zake kuti ufote? Masamba ake onse anthete adzafota. Sipadzafunika dzanja lamphamvu kapena anthu ambiri kuti awuzule.
Wtedy powiedz: Tak mówi Pan BÓG: Czy się jej poszczęści? Czy [orzeł] nie wyrwie jej korzeni i nie oberwie jej owocu [tak], by uschła? Uschną wszystkie listki, które wypuści, i nie będzie trzeba wielkiej mocy ani licznego ludu, aby ją wyrwać z korzeniami.
10 Ngakhale utawokedwa pena, kodi udzaphuka? Kodi sudzafoteratu mphepo ya kummawa ikadzawomba, kufotera pa malo pamene anawuwokerapo?’”
Oto jakkolwiek będzie zasadzona, czy się [jej] poszczęści? Czy doszczętnie nie uschnie, gdy dotknie ją wiatr wschodni? Uschnie w bruzdach, w których wyrosła.
11 Kenaka Yehova anandiyankhula nati:
Potem doszło do mnie słowo PANA:
12 “Tawafunsa anthu owukirawa kuti, ‘kodi mukudziwa tanthauzo la zinthu zimenezi?’ Uwafotokozere kuti, ‘Mfumu ya Babuloni inapita ku Yerusalemu ndikukatengako mfumu ndi anthu ake otchuka ndi kubwera nawo ku Babuloni.
Mów teraz do domu buntowniczego: Czyż nie wiecie, co znaczą te [rzeczy]? Powiedz: Oto król Babilonu przybył do Jerozolimy, zabrał jej króla i książąt i uprowadził ich ze sobą do Babilonu.
13 Ndipo anatenga mmodzi wa banja laufumu ndi kuchita naye mgwirizano, ndipo anamulumbiritsa kuti akhale womvera. Inatenganso akulu onse a mʼdzikomo
Wziął też jednego z potomków króla, zawarł z nim przymierze i związał go przysięgą. Zabrał też możnych tej ziemi;
14 kuti ufumu wa dzikolo utsitsidwe, usadzaphukenso, koma kuti ukhalepobe posunga pangano limene unachita.
Aby królestwo było poniżone, tak by się nie podnosiło, [ale] by tak trwało, zachowując jego przymierze.
15 Koma mfumu inawukira mfumu ya ku Babuloni potumiza nthumwi ku dziko la Igupto kukatenga akavalo ndi gulu lalikulu la nkhondo. Kodi mfumu yotereyi ingapambane? Kodi wochita zinthu zoterezi angapulumuke? Kodi angaphwanye mgwirizano ndi kupulumuka?
Lecz on zbuntował się przeciwko niemu, wysyłając swych posłów do Egiptu, aby dano mu koni i liczny lud. Czy mu się poszczęści? Czy ujdzie zemsty ten, który tak czynił? Czy ocali się ten, który złamał przymierze?
16 “‘Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, mfumuyo idzafera ku Babuloni, mʼdziko la mfumu imene inayika pa mpando waufumu. Inapeputsa lumbiro lake nʼkuphwanya pangano limene inachita ndi mfumu inayo.
Jak żyję, mówi Pan BÓG, w miejscu tego króla, który go uczynił królem, a którego przysięgą wzgardził i którego przymierze złamał, u niego w Babilonie umrze.
17 Farao ndi gulu lake lankhondo lamphamvu sadzatha kumuthandiza pa nkhondo, pamene mfumu ya Babuloni idzapanga mitumbira ya nkhondo ndi nsanja za nkhondo kuti iwononge miyoyo yambiri.
I ani faraon z wielkim wojskiem i z licznym zastępem nie pomoże mu na wojnie, gdy usypie wały i pobuduje wieże, aby zniszczyć mnóstwo ludzi;
18 Mfumu ya ku Yuda inanyoza lumbiro lake pophwanya pangano. Inalonjeza komabe sinatsatire malonjezo ake. Choncho sidzapulumuka.
Ponieważ wzgardził przysięgą, łamiąc przymierze. Oto bowiem dał na to swą rękę, a to wszystko uczynił. Nie ujdzie zemsty.
19 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndithu pali Ine wamoyo, Ine ndidzalanga mfumu imeneyi chifukwa inanyoza lumbiro langa, ndi kuphwanya pangano langa.
Dlatego tak mówi Pan BÓG: Jak żyję, moją przysięgę, którą wzgardził, i moje przymierze, które złamał, złożę mu na głowę.
20 Ndidzayitchera ukonde ndipo idzakodwa mu msampha wanga. Ndidzapita nayo ku Babuloni ndi kuyilanga kumeneko chifukwa inali yosakhulupirika kwa Ine.
Rozciągnę na nim swoją sieć i zostanie schwytany w moje sidła, i zaprowadzę go do Babilonu, a tam się z nim rozprawię za jego występek, którym zgrzeszył przeciwko mnie.
21 Asilikali ake onse amene akuthawa adzaphedwa ndi lupanga, ndipo opulumuka adzabalalitsidwa ku mbali zonse. Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova ndayankhula.
A wszyscy, którzy uciekli od niego wraz ze wszystkimi jego hufcami, od miecza polegną, a pozostali zostaną rozproszeni na wszystkie wiatry. I poznacie, że ja, PAN, [to] powiedziałem.
22 “‘Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndidzatenga nthambi pamwamba penipeni pa mkungudza ndi kuyidzala; ndidzathyola nthambi yanthete kuchokera pa nthambi zapamwamba penipeni ndi kuyidzala pamwamba pa phiri lalitali.
Tak mówi Pan BÓG: Wezmę wierzchołek tego wysokiego cedru i zasadzę; z najwyższych jego gałązek odłamię młodą gałązkę i zasadzę [ją] na wysokiej i wyniosłej górze;
23 Ndidzayidzaladi pa phiri lalitali la Israeli. Idzaphuka nthambi ndi kubereka zipatso. Choncho idzasanduka mkungudza wamphamvu. Mbalame za mtundu uliwonse zidzamanga zisa zawo mʼmenemo; zidzapeza malo okhala mu mthunzi wa nthambi zake.
Na wysokiej górze Izraela ją zasadzę. Wypuści gałązki, wyda owoc i stanie się cedrem wspaniałym. I będzie mieszkać pod nim wszelkie ptactwo skrzydlate; pod cieniem jego gałęzi będą mieszkać.
24 Mitengo yonse yakuthengo idzadziwa kuti Ine ndine Yehova amene ndimafupikitsa mitengo yayitali ndi kutalikitsa mitengo yayifupi. Ndimawumitsa mitengo yabiriwiri ndi kubiriwitsa mitengo yowuma. “‘Ine Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichita.’”
A tak wszystkie drzewa polne poznają, że ja, PAN, poniżyłem drzewo wysokie, a wywyższyłem drzewo niskie, ususzyłem drzewo zielone, a sprawiłem, że zakwitło drzewo suche. Ja, PAN, to powiedziałem i uczynię.

< Ezekieli 17 >