< Ezekieli 16 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
Opet mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
2 “Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa.
Sine èovjeèji, pokaži Jerusalimu gadove njegove,
3 Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti.
I reci: ovako veli Gospod Gospod Jerusalimu: postanjem i rodom ti si iz zemlje Hananske; otac ti bješe Amorejac a mati Hetejka.
4 Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu.
A o roðenju tvom, kad si se rodila, nije ti pupak odrezan i nijesi okupana vodom da bi bila èista, niti si solju natrvena ni pelenama povita.
5 Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.
Oko te ne požali da ti uèini što od toga i da ti se smiluje; nego ti bi baèena u polje, jer bijaše mrska duša tvoja onoga dana kad si se rodila.
6 “‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’
I iduæi mimo tebe i vidjevši te gdje se valjaš u svojoj krvi, rekoh ti: da si živa u svojoj krvi! i opet ti rekoh: da si živa u svojoj krvi!
7 ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.
I uèinih da rasteš na tisuæe kao trava u polju; i ti naraste i posta velika i doðe do najveæe ljepote; dojke ti napupiše, i dlake te probiše; ali ti bijaše gola naga.
8 “‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.
I iduæi mimo tebe pogledah te, i gle, godine ti bijahu godine za ljubljenje; i raširih skut svoj na te, i pokrih golotinju tvoju, i zakleh ti se i uèinih vjeru s tobom, govori Gospod Gospod, i ti posta moja.
9 “‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta.
I okupah te vodom, i sprah s tebe krv tvoju, i pomazah te uljem.
10 Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta.
I obukoh ti vezenu haljinu, i obuh ti crevlje od jazavca, i opasah te tankim platnom i zastrijeh te svilom.
11 Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako,
I nakitih te nakitom, i metnuh ti narukvice na ruke i grivnu oko vrata.
12 ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako.
I grivnu oko èela metnuh ti, i oboce u uši, slavan vijenac na glavu.
13 Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi.
I ti bijaše okiæena zlatom i srebrom, i odijelo ti bijaše od tankoga platna i od svile i vezeno, jeðaše bijelo brašno i med i ulje, i bijaše vrlo lijepa, i prispje do carstva.
14 Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.
I razide se glas o tebi po narodima radi ljepote tvoje, jer bješe savršena krasotom mojom, koju metnuh na te, govori Gospod Gospod.
15 “‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake.
Ali se ti osloni na ljepotu svoju, i prokurva se s glasa svojega, te si prosipala kurvarstvo svoje svakome koji prolažaše, i bivala si njegova.
16 Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso.
I uzevši od haljina svojih naèinila si šarene visine, i kurvala si se na njima, kako nigda nije bilo niti æe biti.
17 Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama.
I uzevši krasni nakit svoj od moga zlata i od moga srebra što ti dadoh, naèinila si sebi muške likove, i kurvala si se s njima.
18 Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo.
I uzevši vezene haljine svoje zaodjela si ih, i ulje moje i kad moj stavila si pred njih.
19 Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
I hljeb moj, koji ti dadoh, bijelo brašno i ulje i med, èim te hranjah, postavila si pred njih za miris ugodni. Tako je bilo, govori Gospod Gospod.
20 “‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire
I uzimala si sinove svoje i kæeri svoje koje si rodila, i njih si im prinosila da se spale. Malo li bješe kurvarstva tvojega,
21 kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo?
Te si i sinove moje klala i davala si ih da im se provedu kroz oganj?
22 Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.
I uza sve gadove svoje i kurvarstva svoja nijesi se opominjala dana mladosti svoje kad si bila gola i naga i valjala se u krvi svojoj.
23 “‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse,
I poslije sve zloæe svoje, teško, teško tebi! govori Gospod Gospod, )
24 wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse.
Sagradila si sebi kuæu kurvarsku, i naèinila si sebi visine na svakoj ulici,
25 Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo.
Na svakoj rasputici naèinila si sebi visinu, i nagrdila si svoju ljepotu, i razmetala si noge svoje svakome koji prolažaše, i umnožila si kurvarstvo svoje.
26 Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako.
Kurvala si se sa sinovima Misirskim, susjedima svojim velika tijela, i umnožila si kurvarstvo svoje da bi me razgnjevila.
27 Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa.
Zato, gle, digoh ruku svoju na te i umalih obrok tvoj, i dadoh te na volju nenavidnicima tvojima, kæerima Filistejskim, koje bješe stid od sramotnoga puta tvojega.
28 Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe.
Kurvala si se sa sinovima Asirskim, jer se ne mogaše nasititi; kurvala si se s njima, i opet se nijesi nasitila.
29 Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.
I umnožila si kurvarstvo svoje u zemlji Hananskoj dori do Haldejske, i ni tako se nijesi nasitila.
30 “‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi.
Kako je iznemoglo srce tvoje, govori Gospod Gospod, kad èiniš sve što èini najgora kurva,
31 Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.
Kad si gradila kurvarsku kuæu na svakoj rasputici i èinila visinu na svakoj ulici! A ni kao kurva nijesi, jer nijesi marila za platu;
32 “‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako!
Nego kao žena preljuboèinica, koja mjesto muža svoga prima druge.
33 Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe.
Svijem kurvama daje se plata, a ti si davala platu svijem milosnicima svojim i darivala si ih da dolaze k tebi sa svijeh strana da se kurvaju s tobom.
34 Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.
I tako je u tebe naopako prema ženama u tvom kurvarstvu: jer niko ne ide za tobom da se kurva, i ti daješ platu, a ne daje se tebi plata; to je naopako.
35 “‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova!
Zato, kurvo, èuj rijeè Gospodnju.
36 Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano,
Ovako veli Gospod Gospod: što se otrov tvoj prosu, i što se u kurvanju tvom otkrivala golotinja tvoja tvojim milosnicima i svijem gadnijem idolima tvojim, i za krv sinova tvojih, koje si im dala,
37 nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse.
Zato, evo, ja æu skupiti sve milosnike tvoje, s kojima si se milovala, i sve koje si ljubila, i sve na koje si mrzila, skupiæu ih sve oko tebe, i otkriæu im golotinju tvoju da vide svu golotinju tvoju.
38 Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri.
I sudiæu ti kako se sudi onima koje èine preljubu i onima koje krv proljevaju, i daæu te na smrt gnjevu i revnosti.
39 Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa.
I predaæu te u njihove ruke, te æe razoriti tvoju kuæu kurvarsku i raskopati visine tvoje, i svuæi æe haljine s tebe, i uzeæe ti krasni nakit i ostaviæe te golu nagu.
40 Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo.
I dovešæe na te ljudstvo, te æe te zasuti kamenjem, i izbošæe te maèevima svojim.
41 Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako.
I popaliæe kuæe tvoje ognjem, i izvršiæe na tebi sud pred mnogim ženama, i uèiniæu te æeš se okaniti kurvanja i neæeš više davati plate.
42 Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.
I namiriæu gnjev svoj nad tobom, i revnost æe se moja ukloniti od tebe, i umiriæu se, i neæu se više gnjeviti.
43 “‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.
Zato što se nijesi opominjala dana mladosti svoje, nego si me dražila svijem tijem, zato, evo, i ja æu obratiti put tvoj na tvoju glavu, govori Gospod Gospod, te neæeš èiniti grdila niti kakvih gadova svojih.
44 “‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’
Gle, ko god govori prièe, govoriæe o tebi prièu, i reæi æe: kaka mati, taka joj kæi.
45 Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori.
Ti si kæi matere svoje, koja se odmetnula muža svojega i djece svoje, i sestra si sestara svojih, koje se odmetnuše muževa svojih i djece svoje, mati vam je Hetejka a otac Amorejac.
46 Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi.
A starija ti je sestra Samarija s kæerima svojim, koja ti sjedi s lijeve strane, a mlaða ti je sestra koja ti sjedi s desne strane Sodom sa kæerima svojim.
47 Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo.
A ti ni njihovijem putem nijesi hodila, niti si èinila po njihovijem gadovima, kao da ti to bješe malo, nego si bila gora od njih na svijem putovima svojim.
48 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.
Tako ja živ bio, govori Gospod Gospod, sestra tvoja Sodom i kæeri njezine nijesu èinile kako si èinila ti i tvoje kæeri.
49 “‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi.
Evo, ovo bješe bezakonje sestre tvoje Sodoma: u ponosu, u izobilju hljeba i bezbrižnom miru bješe ona i kæeri njezine, a ne pomagahu siromahu i ubogome;
50 Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu.
Nego se ponašahu i èinjahu gadove preda mnom, zato ih zatrh kad vidjeh.
51 Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye.
Samarija nije zgriješila ni pola koliko ti, jer si poèinila gadova svojih više nego one, te si opravdala sestre svoje svijem gadovima svojim koje si uèinila.
52 Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.
I ti dakle, koja si sudila sestrama svojim, nosi sramotu svoju za grijehe svoje, kojima si postala grða od njih; one su pravednije od tebe; i ti se dakle stidi i nosi sramotu, kad si opravdala sestre svoje.
53 “‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu.
Ako dovedeš natrag njihovo roblje, roblje Sodomsko i kæeri njezinijeh, i roblje Samarijsko i kæeri njezinijeh, dovešæu i tvoje roblje iz ropstva meðu njima,
54 Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa.
Da nosiš sramotu svoju i da se stidiš za sve što si èinila, i da im budeš utjeha.
55 Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja.
Ako se sestre tvoje, Sodom i kæeri njezine povrate kao što su bile, i ako se Samarija i kæeri njezine povrate kao što su bile, povratiæeš se i ti i kæeri tvoje kao što ste bile.
56 Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu
Jer usta tvoja ne pominjaše Sodoma sestre tvoje u vrijeme oholosti tvoje,
57 kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza.
Prije nego se otkri zloæa tvoja kao u vrijeme sramote od kæeri Sirskih i od svijeh što su oko njih, kæeri Filistejskih, koje te sramoæahu sa svijeh strana.
58 Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.
Nosi nevaljalstvo svoje i gadove svoje, govori Gospod.
59 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa.
Jer ovako veli Gospod Gospod: uèiniæu ti kako si ti uèinila prezrevši zakletvu i prestupivši zavjet.
60 Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe.
Ali æu se ja opomenuti zavjeta svojega koji sam uèinio s tobom u vrijeme mladosti tvoje, i utvrdiæu ti vjeèan zavjet.
61 Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe.
Tada æeš se opomenuti putova svojih i postidjeæeš se kad primiš sestre svoje starije od sebe i mlaðe, koje æu ti dati za kæeri, ali ne po tvom zavjetu.
62 Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
I ja æu utvrditi svoj zavjet s tobom, i poznaæeš da sam ja Gospod.
63 Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’”
Da se opomeneš i postidiš i da ne otvoriš više usta od sramote, kad ti oprostim sve što si uèinila, govori Gospod Gospod.

< Ezekieli 16 >