< Ezekieli 12 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
Opet mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
2 “Iwe mwana wa munthu, ukukhala pakati pa anthu owukira, iwowo maso openyera ali nawo, koma sakuona ndipo makutu omvera ali nawo, koma sakumva chifukwa choti ndi anthu owukira.
Sine èovjeèji, usred doma odmetnièkoga sjediš, koji ima oèi da vidi i ne vidi, ima uši da èuje i ne èuje; jer su dom odmetnièki.
3 “Choncho, iwe mwana wa munthu, longedza katundu wako wopita naye ku ukapolo. Unyamuke nthawi yamasana iwo akuona. Uchite ngati wanyamuka kuchoka kumene ukukhala kupita ku dziko lachilendo iwowo akuona. Mwina adzamvetsetsa, paja ndi anthu aupandu.
Zato ti, sine èovjeèji, spremi što treba za seobu, i seli se obdan na njihove oèi; i iseli se iz svojega mjesta na drugo mjesto na njihove oèi, ne bi li vidjeli, jer su dom odmetnièki.
4 Utulutse katundu wako wopita naye ku ukapolo nthawi ya masana iwo akuona. Ndipo nthawi ya madzulo, iwo akuona, uchoke monga ngati ukupita ku ukapolo.
I iznesi stvari svoje kao kad se ko seli obdan na njihove oèi, a sam izidi uveèe na njihove oèi kao oni koji se sele.
5 Iwo akuona, ubowole pa khoma ndipo utulutsirepo katundu wako.
Na njihove oèi prokopaj zid, i iznesi svoje stvari.
6 Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”
Na njihove oèi digni na ramena i iznesi po mraku, lice svoje pokrij da ne vidiš zemlje, jer te dadoh da budeš znak u domu Izrailjevu.
7 Choncho ine ndinachita monga momwe anandilamulira. Nthawi yamasana ndinatulutsa zinthu zanga nditazimanga ngati ndikupita ku ukapolo. Ndipo nthawi yamadzulo ndinabowola khoma ndi manja anga. Pamene chisisira chinkayamba, ndinasenza katundu wanga pa phewa kutuluka naye iwo akuona.
I uèinih tako kako mi se zapovjedi; stvari svoje iznesoh obdan kao kad se seli; a uveèe prokopah zid rukom; i po mraku iznesoh na ramenima noseæi na njihove oèi.
8 Mmawa mwake Yehova anandiyankhula nati:
A ujutru doðe mi rijeè Gospodnja govoreæi:
9 “Iwe mwana wa munthu, kodi anthu aupandu a Israeli sanakufunse kuti ukuchita chiyani?
Sine èovjeèji, reèe li ti dom Izrailjev, dom odmetnièki: što radiš?
10 “Uwawuze kuti, ‘zimene ndikunena Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndi izi: Uthengawu ndi wonena za kalonga wa ku Yerusalemu pamodzi ndi banja lonse la Israeli amene akukhala kumeneko.’
Reci im: ovako veli Gospod Gospod: ovo je breme za kneza koji je u Jerusalimu i za sav dom Izrailjev što je ondje.
11 Uwawuze kuti, ‘Ndiwe chizindikiro chowachenjeza.’ “Zidzakuchitikirani monga momwe zakuchitikira iwemu. Iwo adzatengedwa kupita ku ukapolo.”
Reci: ja sam vam znak, kako ja uèinih tako æe im biti; preseliæe se i otiæi u ropstvo.
12 “Kalonga wawo adzatenga katundu wake nʼchisisira nʼkunyamuka. Adzatulukira pa bowo limene anthu anabowola pa khoma. Adzaphimba nkhope yake kuti asaone kumene akupita.
I knez koji je meðu njima noseæi na ramenima po mraku æe izaæi; oni æe prokopati zid da iznesu; on æe pokriti lice svoje da ne vidi zemlje oèima.
13 Ndidzayala ukonde wanga pa iye ndi kumukola mu msampha wanga. Ndidzabwera naye ku Babuloni, dziko la Akaldeya, koma sadzaliona dzikolo, ndipo adzafera kumeneko.
Ali æu mu razapeti mrežu svoju i uhvatiæe se u zamku moju, i odvešæu ga u Vavilon, u zemlju Haldejsku, ali je neæe vidjeti, a ondje æe umrijeti.
14 Ine ndidzabalalitsa kumbali zonse zinayi onse okhala naye pafupi, ndiwo omuthandiza ake pamodzi ndi ankhondo ake. Ndidzawalondola ndi lupanga losolola.
I sve koji su oko njega, pomoænike njegove, i svu vojsku njegovu rasijaæu u sve vjetrove, i izvuæi æu maè za njima.
15 “Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsira ku mayiko ena.
I poznaæe da sam ja Gospod kad ih rasijem po narodima i razaspem po zemljama.
16 Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”
A ostaviæu ih nekoliko ljudi koji æe ostati od maèa i od gladi i od pomora da pripovijedaju sve gadove svoje meðu narodima u koje otidu; i poznaæe da sam ja Gospod.
17 Pambuyo pake Yehova anandiyankhulanso nati,
Opet mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
18 “Iwe mwana wa munthu, uzinjenjemera ukamadya chakudya chako, ndipo uzinthunthumira ndi mantha ukamamwa madzi ako.
Sine èovjeèji, hljeb svoj jedi prezajuæi i vodu svoju pij drkæuæi i brinuæi se.
19 Uwawuze anthu a mʼdzikomo kuti izi ndi zimene Ambuye Wamphamvuzonse akunena za anthu okhala mu Yerusalemu ndi dziko la Israeli: Iwo adzadya chakudya chawo ndi mantha ndi kumwa madzi awo ndi nkhawa. Zonse za mʼdziko lawo zidzalandidwa chifukwa cha ziwawa za anthu onse okhala mʼmenemo.
I reci narodu zemaljskom: ovako veli Gospod Gospod za stanovnike Jerusalimske, za zemlju Izrailjevu: hljeb æe svoj jesti u brizi i vodu æe svoju piti prepadajuæi se, jer æe zemlja opustjeti i ostati bez svega što je u njoj za bezakonje svijeh koji žive u njoj.
20 Mizinda imene ili ndi anthu idzasakazika ndipo dziko lidzasanduka chipululu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
I gradovi u kojima žive opustjeæe, i zemlja æe biti pusta, i poznaæete da sam ja Gospod.
21 Yehova anayankhulanso nane kuti,
Opet mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
22 “Iwe mwana wa munthu, kodi mwambi umene ukunenedwa mu Israeli ndi wotani: ‘Masiku akupita koma masomphenya onse sakukwaniritsidwa?’
Sine èovjeèji, kaka je to prièa u vas o zemlji Izrailjevoj što govorite: protežu se dani, i od utvare neæe biti ništa?
23 Choncho uwawuze anthuwo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndidzawuthetsa mwambi umenewu ndipo sadzawunenanso mu Israeli.’ Uwawuze kuti, ‘masiku ayandikira oti zonse zimene ndinanena mʼmasomphenya zichitikedi.
Zato im reci: ovako veli Gospod Gospod: ukinuæu tu prièu i neæu je više govoriti u Izrailju; nego im reci: blizu su dani i rijeè svake utvare.
24 Pakuti masiku amenewo sikudzakhalanso masomphenya abodza kapena kuwombeza kwa chinyengo pakati pa anthu a Israeli.
Jer neæe više biti u domu Izrailjevu zaludne utvare ni gatanja kojim se laska.
25 Koma Ine Ambuye ndidzayankhula chimene ndikufuna, ndipo chidzachitikadi, osachedwa ayi. Pakuti mʼmasiku anu omwe ano, inu anthu opanduka, ndidzakwaniritsa chilichonse chimene ndidzanena. Ndikutero Ine Yehova.’”
Jer æu ja Gospod govoriti, i što reèem zbiæe se; neæe se više odgaðati, nego za vašega vremena, dome odmetnièki, reæi æu rijeè i izvršiæu je, govori Gospod Gospod.
26 Yehova anandiyankhula nati:
Opet mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
27 “Iwe mwana wa munthu, Aisraeli akunena kuti, ‘masomphenya amene ukuona sadzachitika kwa zaka zambiri. Iwo akuti ukulosa za zinthu zimene zidzachitika ku tsogolo kwambiri.’
Sine èovjeèji, gle, dom Izrailjev govori: utvara koju taj vidi, do nje ima mnogo vremena, i za daleko vrijeme taj prorokuje.
28 “Choncho uwawuze kuti, ‘zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso; chilichonse chimene ndikunena chidzachitikadi. Ndikutero Ine Yehova.’”
Zato im reci: ovako veli Gospod Gospod: neæe se više odgaðati nijedna moja rijeè; rijeè koju reèem zbiæe se, govori Gospod Gospod.

< Ezekieli 12 >