< Eksodo 38 >

1 Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229.
I naèini od drveta sitima oltar za žrtve paljenice u dužinu od pet lakata, i u širinu od pet lakata, èetvorouglast visok tri lakta.
2 Anapanga nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo, kotero kuti nyangazo ndi guwalo zinali chinthu chimodzi, ndipo anakuta guwalo ndi mkuwa.
I naèini mu na èetiri ugla njegova rogove; iz njega izlažahu rogovi, i okova ga u mjed.
3 Anapanganso ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
I naèini sve posuðe za oltar, lonce i lopatice i kotliæe i viljuške i kliješta; sve mu posuðe naèini od mjedi.
4 Anapanga sefa yachitsulo chamkuwa ya guwa lansembelo kuti ikhale mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, kuchokera pansi mpaka pakati pa khoma la guwalo.
I naèini oltaru rešetku kao mrežu od mjedi ispod oltara unaokolo oda dna do sredine.
5 Anapanga mphete zamkuwa zinayi ndipo anazilumikiza ku ngodya zinayi za sefa ija kuti zigwire nsichi zonyamulira.
I sali èetiri bioèuga za èetiri ugla rešetke mjedene, da se kroz njih provuku poluge.
6 Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndipo anazikuta ndi mkuwa.
A poluge naèini od drveta sitima, i okova ih u mjed.
7 Iwo analowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo kuti azinyamulira. Guwalo linali lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake.
I provuèe poluge kroz bioèuge s obje strane oltara, da se može nositi, od dasaka naèini ga šuplja.
8 Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
I naèini umivaonicu mjedenu i podnožje joj mjedeno od ogledala koja donošahu gomilama žene dolazeæi na vrata šatoru od sastanka.
9 Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
I naèini trijem na južnoj strani, i zavjese trijemu od tankoga platna uzvedenoga od sto lakata,
10 Anapanganso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
I dvadeset stupova za njih i dvadeset stopica pod njih od mjedi, a kuke na stupove i prijevornice od srebra.
11 Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
Tako i na sjevernoj strani zavjese od sto lakata, dvadeset stupova za njih i dvadeset stopica pod njih od mjedi; a kuke na stupove i prijevornice njihove od srebra;
12 Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
A na zapadnoj strani zavjese od pedeset lakata, deset stupova za njih i deset stopica njihovijeh od mjedi, kuke na stupove i pojasove njihove od srebra;
13 Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, inalinso yotalika mamita 23.
A na prednjoj strani prema istoku zavjese od pedeset lakata;
14 Mbali imodzi yachipata kunali nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu,
S jedne strane zavjese od petnaest lakata, tri stupa za njih i tri stopice pod njih;
15 polowera mʼbwalo panali nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
A s druge strane, do vrata od trijema i otuda i odovuda, zavjese od petnaest lakata, tri stupa za njih i tri stopice pod njih.
16 Katani yonse yotchinga kuzungulira chihema inali yofewa, yosalala ndi yolukidwa bwino.
Svi zavjesi na trijemu unaokolo bjehu od tankoga platna uzvedenoga;
17 Matsinde amizati anali amkuwa. Ngowe ndi zingwe za mizati zinali zasiliva, ndipo pamwamba pa mizatiyo anakutapo siliva. Choncho mizati yonse ya bwalolo inalumikizidwa ndi zingwe zasiliva.
A stopice pod stupovima od mjedi, kuke na stupovima i pojasovi na njima od srebra; i vrhovi im bijahu srebrni; svi stupovi u trijemu bijahu opasani srebrom.
18 Nsalu yotchinga ya pa chipata inali yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira, yofewa yosalala ndi yopangidwa ndi anthu aluso. Nsaluyo inali yotalika mamita asanu ndi anayi, molingana ndi nsalu zotchinga bwalo. Msinkhu wake unali masentimita 229,
A zavjes na vratima od trijema bijaše od porfire i od skerleta i od crvca i od tankoga platna uzvedenoga, vezen, u dužinu od dvadeset lakata a u visinu po širini pet lakata, kao i drugi zavjesi u trijemu.
19 pamodzi ndi mizati yake inayi ndi matsinde amkuwa anayi. Ngowe ndi zingwe zake zinali za siliva, ndipo pamwamba pake pa mzati anakutapo ndi siliva.
I èetiri stupa za nj, i èetiri stopice pod njih od mjedi, èepovi na njima od srebra i vrhovi im i pojasovi od srebra.
20 Zikhomo za chihema ndi zina zonse zozungulira chihemacho zinali zamkuwa.
A sve kolje šatoru i trijemu unaokolo bijaše od mjedi.
21 Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi:
Te su stvari prebrojene za šator, šator od svjedoèanstva, koje je prebrojio po zapovijesti Mojsijevoj Itamar sin Arona sveštenika za službu Levitsku.
22 Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huzi wa fuko la Yuda anapanga chilichonse Yehova analamulira Mose,
A Veseleilo sin Urije sina Orova od plemena Judina naèini sve to što zapovjedi Gospod Mojsiju,
23 pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, wa luso la zopangapanga ndi kulemba mapulani, ndi wopanga nsalu zolukidwa bwino za mtundu wa mtambo, yapepo ndi zofiira, zofewa ndi zosalala.
I s njim Elijav sin Ahisamahov od plemena Danova, drvodjelja i vješt tkati i vesti po porfiri, po skerletu, po crvcu i po tankom platnu.
24 Golide yense wochokera ku nsembe yoweyula amene anagwiritsa ntchito pa ntchito yonse yopanga malo wopatulika anali wolemera makilogalamu 1,000 potsata miyeso ya kumalo wopatulika.
A svega zlata što otide na ovo djelo, na sve djelo za svetinju, koje zlato bješe priloženo, svega ga bješe dvadeset i devet talanata, sedam stotina i trideset sikala, po svetom siklu;
25 Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika.
A srebra što doðe od zbora, sto talanata, i tisuæa sedam stotina i sedamdeset i pet sikala, po svetom siklu;
26 Munthu aliyense amapereka beka imodzi, kufanana ngati makilogalamu 6, potsata muyeso wa ku malo wopatulika. Kuchokera kwa aliyense amene anawerengedwa kuyambira zaka 20 kapena kuposerapo, amuna onse analipo 603,550.
Po sikla od glave, po siklu svetom, od svakoga koji uðe u broj, od dvadeset godina i više, od šest stotina i tri tisuæe i pet stotina i pedeset.
27 Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi.
Od sto talanata srebra sališe se stopice za svetinju i stopice za zavjes; sto stopica od sto talanata, talanat na stopicu.
28 Makilogalamu otsalawo anagwiritsa ntchito popanga ngowe zamzati kukutira pamwamba pa mizati ndiponso kupanga zingwe zake.
A od tisuæu i sedam stotina i sedamdeset i pet sikala naèini kuke na stupove, i okova im vrhove i opasa ih.
29 Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425.
A mjedi priložene bijaše sedamdeset talanata, i dvije tisuæe i èetiri stotine sikala.
30 Iwo anawugwiritsa ntchito popanga matsinde a pa chipata cha tenti ya msonkhano, guwa la mkuwa pamodzi ndi sefa yake ndiponso ziwiya zonse,
I od toga naèini stopice na vratima šatora od sastanka, i mjedeni oltar i rešetku mjedenu za nj, i sve sprave za oltar,
31 matsinde ozungulira bwalo ndiponso a pa chipata pake, ndi zikhomo zonse za tentiyo ndi matsinde a malo wozungulirapo.
I stopice u trijemu unaokolo, i stopice na vratima od trijema, i sve kolje za šator i sve kolje za trijem unaokolo.

< Eksodo 38 >