< Eksodo 35 >

1 Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
Potem Mojżesz zebrał całe zgromadzenie synów Izraela i mówił do nich: Oto są słowa, które PAN rozkazał, abyście je wypełnili.
2 Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
Przez sześć dni będzie wykonywana praca, ale siódmy dzień będzie dla was świętem, szabatem odpoczynku dla PANA. Kto w nim wykona pracę, poniesie śmierć.
3 Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
Nie rozniecicie ognia w żadnym z waszych mieszkań w dzień szabatu.
4 Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
Mojżesz powiedział też do całego zgromadzenia synów Izraela: Oto słowo, które PAN przykazał:
5 Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
Złóżcie PANU dar od siebie: każdy, kto jest ochotnego serca, niech przyniesie PANU dar: złoto, srebro i miedź;
6 nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
Błękitną [tkaninę], purpurę, karmazyn, bisior i kozią sierść;
7 zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
I skóry baranie farbowane na czerwono i skóry borsucze, i drewno akacjowe;
8 mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
Oliwę do oświetlenia, wonności na olejek do namaszczania i na wonne kadzidło;
9 miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
Kamienie onyksu i kamienie do osadzenia efodu i pektorału.
10 “Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
A wszyscy spośród was, którzy są uzdolnieni, przyjdą i będą robić wszystko, co PAN rozkazał:
11 Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
Przybytek, jego namiot i przykrycie, haczyki do niego i deski, drążki do niego, słupy i podstawki;
12 Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
Arkę i drążki do niej, przebłagalnię i zasłonę [do] osłonięcia;
13 tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
Stół i drążki do niego, wszystkie jego naczynia i chleby pokładne;
14 choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
Świecznik do oświetlenia i jego przybory, lampy do niego i oliwę do świecenia.
15 guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
Także ołtarz kadzenia z drążkami do niego, olejek do namaszczania, wonne kadzidło i zasłonę do wejścia do przybytku;
16 guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
Ołtarz całopalenia, miedzianą kratę do niego, drążki i wszystkie naczynia do niego, kadź i jej podstawę;
17 nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
Zasłony do dziedzińca, słupy i podstawki do nich, zasłonę do wejścia na dziedziniec.
18 zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
Kołki do przybytku i kołki do dziedzińca z ich sznurami.
19 zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
Szaty służebne do usługiwania w Miejscu Świętym, święte szaty kapłana Aarona i szaty dla jego synów, do sprawowania urzędu kapłańskiego.
20 Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
Wtedy całe zgromadzenie synów Izraela odeszło od Mojżesza.
21 ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
I przyszedł każdy, kogo serce pobudziło, i każdy, w którym duch był ochoczy; [i] przynieśli PANU dar do wykonania Namiotu Zgromadzenia, na wszelką służbę w nim i na święte szaty.
22 Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
Przychodzili więc mężczyźni i kobiety, każdy, kto był ochotnego serca, [i] przynosili bransoletki, kolczyki, pierścienie, naszyjniki [i] wszelkie złote przedmioty i każdy przynosił PANU ofiarę ze złota.
23 Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
Każdy też, kto miał błękitną [tkaninę], purpurę, karmazyn, bisior, kozią sierść, skóry baranie farbowane na czerwono i skóry borsucze, przynosił [je].
24 Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
Każdy, kto ofiarował dar ze srebra i miedzi, przynosił na ofiarę dla PANA; każdy też, kto miał drewno akacjowe, do wszelkiej pracy tej służby, przynosił [je].
25 Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
I wszystkie uzdolnione kobiety przędły swymi rękami i przynosiły to, co naprzędły: z błękitnej [tkaniny], purpury, karmazynu i bisioru.
26 Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
A wszystkie kobiety, których serca były obdarzone zdolnością, przędły kozią sierść.
27 Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
Przełożeni zaś przynosili kamienie onyksu i kamienie do osadzenia efodu i pektorału;
28 Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
Także wonności i oliwę do świecenia i na olejek do namaszczania, i na wonne kadzidła.
29 Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
Wszyscy synowie Izraela przynosili PANU dobrowolną ofiarę, każdy mężczyzna i każda kobieta, w których było serce ochocze do składania ofiar na każde dzieło, które PAN przez Mojżesza rozkazał wykonać.
30 Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
Potem Mojżesz powiedział do synów Izraela: Oto PAN powołał po imieniu Besalela, syna Uriego, syna Chura, z pokolenia Judy;
31 ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
I napełnił go Duchem Bożym, mądrością, rozumem i umiejętnością we wszelkim rzemiośle;
32 Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
Aby umiejętnie wymyślał wzory, aby wyrabiał ze złota, srebra i miedzi;
33 kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
Do obrabiania kamieni do oprawy, do ciosania drewna, aby wykonał wszelkie rodzaje dzieła.
34 Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
Włożył mu w serce też [zdolność], aby mógł uczyć [innych], on, i Oholiab, syn Achisamaka, z pokolenia Dana.
35 Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.
Napełnił ich mądrością serca, aby wykonywali wszelkie rzemiosło rytownicze, obmyślania projektów, hafciarskie z błękitnej [tkaniny], purpury, karmazynu i bisioru i tkackie, aby obmyślali i zręcznie wykonywali każdą pracę.

< Eksodo 35 >