< Eksodo 32 >

1 Anthu ataona kuti Mose akuchedwa kutsika mʼphiri, anasonkhana kwa Aaroni ndipo anati, “Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.”
A narod vidjevši gdje Mojsije za dugo ne slazi s gore, skupi se narod pred Arona, i rekoše mu: hajde, naèini nam bogove, koji æe iæi pred nama, jer tome Mojsiju koji nas izvede iz zemlje Misirske ne znamo šta bi.
2 Aaroni anawayankha kuti, “Vulani ndolo zagolide zimene avala akazi anu, ana anu aamuna ndi aakazi ndipo muzibweretse kwa ine.”
A Aron im reèe: poskidajte zlatne oboce što su u ušima žena vaših, sinova vaših i kæeri vaših, i donesite mi.
3 Kotero anthu onse anavula ndolo zagolide ndi kubwera nazo kwa Aaroni.
I poskida sav narod zlatne oboce što im bijahu u ušima, i donesoše Aronu.
4 Choncho Aaroni analandira golideyo ndipo anamuwumba ndi chikombole ndi kupanga fano la mwana wangʼombe. Kenaka anthu aja anati, “Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.”
A on uzev iz ruku njihovijeh, sali u kalup, i naèini tele saliveno. I rekoše: ovo su bogovi tvoji, Izrailju, koji te izvedoše iz zemlje Misirske.
5 Aaroni ataona izi, anamanga guwa lansembe patsogolo pa mwana wangʼombeyo ndipo analengeza kuti, “Mawa kudzakhala chikondwerero cha Yehova.”
A kad to vidje Aron, naèini oltar pred njim; i povika Aron, i reèe: sjutra je praznik Gospodnji.
6 Kotero tsiku linalo anthu anadzuka mmamawa ndithu ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Atatha kupereka nsembezo, anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.
I sjutradan ustavši rano prinesoše žrtve paljenice i žrtve zahvalne; i posjeda narod, te jedoše i piše, a poslije ustaše da se igraju.
7 Pamenepo Yehova anati kwa Mose, “Tsika msanga, chifukwa anthu ako amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto aja adziyipitsa kwambiri.
A Gospod reèe Mojsiju: idi, siði, jer se pokvari tvoj narod, koji si izveo iz zemlje Misirske.
8 Iwo apatuka mwamsanga kuleka kutsatira zimene ndinawalamula. Ndiye adzipangira fano la mwana wangʼombe. Aligwadira ndi kuliperekera nsembe nʼkumati, ‘Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.’”
Brzo zaðoše s puta, koji sam im zapovjedio; naèiniše sebi tele liveno, i pokloniše mu se, i prinesoše mu žrtvu, i rekoše: ovo su bogovi tvoji, Izrailju, koji te izvedoše iz zemlje Misirske.
9 Yehova anati kwa Mose, “Ine ndikuwadziwa anthu amenewa. Iwowa ndi ankhutukumve.
Još reèe Gospod Mojsiju: pogledah narod ovaj, i eto je narod tvrda vrata.
10 Chifukwa chake undileke kuti mkwiyo wanga uyake pa iwo ndi kuwawononga. Ndipo Ine ndidzakusandutsa kuti ukhale mtundu waukulu.”
I sada pusti me, da se raspali gnjev moj na njih i da ih istrijebim; ali od tebe æu uèiniti narod velik.
11 Koma Mose anapempha chifundo cha Mulungu wake ndipo anati, “Chonde Yehova, chifukwa chiyani mwakwiyira anthu awa amene munawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
A Mojsije se zamoli Gospodu Bogu svojemu, i reèe: zašto se, Gospode, raspaljuje gnjev tvoj na narod tvoj, koji si izveo iz zemlje Misirske silom velikom i rukom krjepkom?
12 Kodi mukufuna kuti Aigupto azinena kuti, ‘Munali ndi cholinga choyipa chofuna kuwaphera ku mapiri kuno ndi kuwawonongeratu pa dziko lapansi pamene munkawatulutsa ku Igupto kuja?’ Ayi, chonde mkwiyo wanu woyaka ngati motowu ubwezeni ndipo sinthani maganizo ofunira zoyipa anthu anu.
Zašto da govore Misirci i reku: na zlo ih izvede, da ih pobije po planinama i da ih istrijebi sa zemlje? Povrati se od gnjeva svojega, i požali narod svoj oda zla.
13 Kumbukirani atumiki anu, Abrahamu, Isake, Israeli ndi zija munawalonjeza polumbira pa dzina lanu kuti, ‘Ine ndidzachulukitsa zidzukulu zanu ndipo zidzakhala zambiri ngati nyenyezi zakumwamba. Zidzukulu zanuzo ndidzazipatsa dziko lonseli limene ndinalonjeza. Dziko limeneli lidzakhala lawo nthawi zonse.’”
Opomeni se Avrama, Isaka i Izrailja, sluga svojih, kojima si se sobom zakleo i obrekao im: umnožiæu sjeme vaše kao zvijezde na nebu, i zemlju ovu, za koju govorih, svu æu dati sjemenu vašemu da je njihova dovijeka.
14 Choncho Yehova analeka ndipo sanawachitire choyipa anthu ake monga anaopsezera.
I ražali se Gospodu uèiniti zlo narodu svojemu, koje reèe.
15 Mose anatembenuka ndi kutsika phiri miyala iwiri ya pangano ili mʼmanja mwake. Miyalayi inalembedwa mbali zonse, kutsogolo ndi kumbuyo komwe.
Tada se vrati Mojsije, i siðe s gore sa dvije ploèe svjedoèanstva u rukama svojim; i ploèe bjehu pisane s obje strane, otud i odovud pisane.
16 Miyalayi anayikonza ndi Mulungu. Malembawo analemba ndi Mulungu mozokota pa miyalapo.
I bjehu ploèe djelo Božije, i pismo bješe pismo Božije, urezano na ploèama.
17 Pamene Yoswa anamva phokoso la anthu anati kwa Mose, “Ku msasa kuli phokoso la nkhondo.”
A Isus èuvši viku u narodu, kad vikahu, reèe Mojsiju: vika ubojna u okolu.
18 Mose anayankha kuti, “Phokoso limeneli sindikulimva ngati phokoso la opambana nkhondo, kapena kulira kwa ongonjetsedwa pa nkhondo. Koma ndikulimva ngati phokoso la anthu amene akuyimba.”
A on reèe: nije to vika kako vièu koji su jaèi, niti je vika kako vièu koji su slabiji, nego èujem viku onijeh koji pjevaju.
19 Mose atayandikira msasa ndi kuona mwana wangʼombe ndiponso kuvina, anakwiya kwambiri ndipo anaponya pansi miyala imene inali mʼmanja mwake, ndi kuyiphwanya pa tsinde la phiri.
I kad doðe blizu okola, ugleda tele i igre, te se razgnjevi Mojsije, i baci iz ruku svojih ploèe, i razbi ih pod gorom.
20 Ndipo iye anatenga mwana wangʼombe amene anthu anapanga uja ndi kumuwotcha pa moto ndi kumuperapera ndikukhala ngati fumbi. Kenaka anawaza fumbilo mʼmadzi ndi kuwamwetsa Aisraeli madziwo.
Pa uze tele koje bijahu naèinili i spali ga ognjem, i satr ga u prah, i prosu ga po vodi, i zapoji sinove Izrailjeve.
21 Tsono Mose anafunsa Aaroni kuti, “Kodi anthu awa anakuchita chiyani kuti uwachimwitse koopsa chotere?”
I reèe Mojsije Aronu: šta ti je uèinio ovaj narod, te ga uvali u toliki grijeh?
22 Aaroni anayankha kuti, “Musakwiye mbuye wanga. Inu mukudziwa kuti anthu awa ndi ovuta.
A Aron mu reèe: nemoj se gnjeviti, gospodaru; ti znaš ovaj narod da je brz na zlo.
23 Iwo anati kwa ine, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa ife mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.’
Jer rekoše mi: naèini nam bogove, koji æe iæi pred nama, jer tome Mojsiju koji nas izvede iz zemlje Misirske ne znamo šta bi.
24 Choncho ine ndinawawuza kuti, ‘Aliyense amene ali ndi zokometsera zagolide azivule.’ Choncho iwo anandipatsa golide, ndipo ndinamuponya pa moto ndi kupanga fano la mwana wangʼombeyu.”
A ja im rekoh: ko ima zlata, neka ga skida sa sebe. I dadoše mi, a ja ga bacih u vatru, i izaðe to tele.
25 Mose anaona kuti anthuwo anali osokonezekadi chifukwa Aaroni anawalekerera mpaka kusanduka anthu osekedwa pakati pa adani awo.
A Mojsije videæi narod go, jer ga ogoli Aron na sramotu pred protivnicima njegovijem,
26 Choncho iye anayima pa chipata cholowera mu msasa ndipo anati, “Aliyense amene ali mbali ya Yehova abwere kwa ine.” Ndipo Alevi onse anapita mbali yake.
Stade Mojsije na vrata od okola, i reèe: k meni ko je Gospodnji. I skupiše se pred njega svi sinovi Levijevi.
27 Ndipo iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena, ‘Pitani ku misasa konse, mulowe ku zipata zonse ndipo aliyense akaphe mʼbale wake, kapena mnzake kapena mnansi wake.’”
I reèe im: ovako kaže Gospod Bog Izrailjev: pripašite svaki svoj maè uz bedro svoje, pa proðite tamo i amo po okolu od vrata do vrata, i pobijte svaki brata svojega i prijatelja svojega i bližnjega svojega.
28 Alevi anachita zomwe Mose analamula, ndipo tsiku limenelo panafa anthu pafupifupi 3,000.
I uèiniše sinovi Levijevi po zapovijesti Mojsijevoj, i pogibe naroda u onaj dan do tri tisuæe ljudi.
29 Kenaka Mose anati, “Lero mwadzipatula nokha kukhala ansembe otumikira Yehova. Mwachita izi popeza aliyense wa inu wapha mwana wake kapena mʼbale wake. Tsono lero Yehova wakudalitsani.”
Jer Mojsije reèe: posvetite danas ruke svoje Gospodu, svak na sinu svom i na bratu svom, da bi vam dao danas blagoslov.
30 Mmawa mwake Mose anati kwa anthu onse, “Inu mwachita tchimo lalikulu. Koma tsopano ine ndipita ku phiri kwa Yehova mwina ndikatha kukupepeserani chifukwa cha tchimo lanu.”
A sjutradan reèe Mojsije narodu: vi ljuto sagriješiste; zato sada idem gore ka Gospodu, eda bih ga umolio da vam oprosti grijeh.
31 Kotero Mose anabwereranso kwa Yehova ndipo anati, “Aa! Anthu awa achita tchimo lalikulu! Iwo adzipangira milungu yagolide.
I vrati se Mojsije ka Gospodu, i reèe: molim ti se; narod ovaj ljuto sagriješi naèinivši sebi bogove od zlata.
32 Koma tsopano, chonde akhululukireni tchimo lawo. Ngati simutero, ndiye mundifute ine mʼbuku limene mwalemba.”
Ali oprosti im grijeh: ako li neæeš, izbriši me iz knjige svoje, koju si napisao.
33 Yehova anamuyankha Mose kuti, “Ndidzafuta mʼbuku aliyense amene wandichimwira.
A Gospod reèe Mojsiju: ko mi je zgriješio, onoga æu izbrisati iz knjige svoje.
34 Tsopano pita ukawatsogolere anthu kumalo kumene ine ndinanena, ndipo mngelo wanga adzakutsogolerani. Komabe, nthawi yanga ikadzafika kuti ndiwalange, ndidzawalanga chifukwa cha tchimo lawo.”
A sada idi, vodi taj narod kuda sam ti kazao. Evo, moj æe anðeo iæi pred tobom, a kad ih pohodim, pohodiæu na njima grijeh njihov.
35 Ndipo Yehova anawakantha anthuwo ndi mliri chifukwa anawumiriza Aaroni kuti awapangire fano la mwana wangʼombe.
I Gospod bi narod zato što naèiniše tele, koje sali Aron.

< Eksodo 32 >