< Eksodo 28 >

1 “Aaroni mʼbale wako ndi ana ake aamuna, Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara uwapatule pakati pa Aisraeli. Abwere kwa iwe kuti anditumikire monga ansembe.
A ti uzmi k sebi Arona brata svojega sa sinovima njegovijem izmeðu sinova Izrailjevih da mi budu sveštenici, Aron i Nadav i Avijud i Eleazar i Itamar, sinovi Aronovi.
2 Umusokere mʼbale wako, Aaroni, zovala zopatulika kuti azioneka mwaulemerero ndi molemekezeka.
I naèini svete haljine Aronu bratu svojemu za èast i diku.
3 Uwawuze anthu onse aluso amene Ine ndawapatsa nzeru pa ntchito yosoka kuti apange zovala za Aaroni za pa mwambo womupatula, kuti iye anditumikire monga wansembe.
I kaži svijem ljudima vještijem, koje sam napunio duha mudrosti, neka naèine haljine Aronu, da se posveti da mi bude sveštenik.
4 Zovala zoti apange ndi izi: chovala chapachifuwa, efodi, mkanjo, mwinjiro wolukidwa, nduwira ndi lamba. Apangire mʼbale wako Aaroni ndi ana ake aamuna zovala zopatulikazi kuti iwo anditumikire monga ansembe.
A ovo su haljine što æe naèiniti: naprsnik i opleæak i plašt, košulja vezena, kapa i pojas. Te haljine svete neka naprave Aronu bratu tvojemu i sinovima njegovijem, da mi budu sveštenici,
5 Iwo agwiritse ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira ndi yosalala yofewa.
I neka uzmu zlata i porfire i skerleta i crvca i tankoga platna;
6 “Apange efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yolukidwa mwaluso.
I neka naèine opleæak od zlata i od porfire i od skerleta i od crvca i od tankoga platna uzvedenoga, vezen.
7 Efodiyo ikhale ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.
Dvije poramenice neka budu na njemu, koje æe se sastavljati na dva kraja, da se drži zajedno.
8 Lamba womangira efodi akhale wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Akhale wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala.
A pojas na njemu neka bude naprave iste kao i on, od zlata, od porfire, od skerleta, od crvca i od tankoga platna uzvedenoga.
9 “Utenge miyala iwiri ya onikisi ndipo uzokotepo mayina a ana a Israeli.
I uzmi dva kamena oniha, i na njima izreži imena sinova Izrailjevih,
10 Mayina asanu ndi limodzi akhale pa mwala umodzi, ndipo mayina asanu ndi limodzi pa mwala winawo motsata mabadwidwe awo.
Šest imena njihovijeh na jednom kamenu, a šest imena ostalijeh na drugom kamenu po redu kako se koji rodio.
11 Mayina a ana a Israeli uwazokote pa miyala iwiriyo, monga momwe amachitira mmisiri wozokota miyala. Ndipo uyike miyalayo mu zoyikamo zake zagolide.
Vještinom kamenarskom, kojom se režu peèati, izrezaæeš na ta dva kamena imena sinova Izrailjevijeh, i optoèi ih zlatom unaokolo.
12 Umangirire miyala iwiriyi pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli. Aaroni azinyamula mayinawo mʼmapewa ake kuti akhale chikumbutso pamaso pa Yehova.
I metni ta dva kamena na poramenice opleæku, da budu kameni za spomen sinovima Izrailjevijem, i Aron da nosi imena njihova pred Gospodom na oba ramena svoja za spomen.
13 Upange zoyikamo za maluwa agolide,
I naèini kopèe od zlata.
14 ndiponso maunyolo awiri a golide wabwino kwambiri, wopetedwa ngati zingwe ndipo uwalumikize ku zoyikamozo.
I dva lanca od èistoga zlata naèini jednaka pletena, i objesi lance pletene o kopèe.
15 “Upange chovala chapachifuwa chogwiritsa ntchito poweruza mlandu ndipo uchipange mwaluso kwambiri. Uchipange ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino.
I naprsnik sudski naèini naprave vezene onake kao opleæak, od zlata, od porfire, od skerleta, od crvca i od tankoga platna uzvedenoga naèini ga.
16 Kutalika kwake kukhale kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, ndipo chikhale chopinda pawiri.
Neka bude èetvorouglast i dvostruk, u dužinu s pedi i u širinu s pedi.
17 Uyikepo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba ukhale ndi miyala ya rubi, topazi ndi berili.
I udari po njemu drago kamenje, u èetiri reda neka bude kamenje. U prvom redu: sardonih, topaz i smaragad;
18 Mzere wachiwiri pakhale miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi;
A u drugom redu: karbunkul, safir i dijamanat;
19 mzere wachitatu pakhale miyala ya opera, agate ndi ametisiti.
A u treæem redu: ligur i ahat i ametist;
20 Mzere wachinayi pakhale miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi uyiike mu zoyikamo zagolide.
A u èetvrtom redu: hrisolit, onih i jaspid; neka budu ukovani u zlato u svom redu.
21 Miyalayo ikhalepo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse uzokotedwe ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
I tijeh kamena s imenima sinova Izrailjevijeh biæe dvanaest po imenima njihovijem, da budu rezani kao peèat, svaki sa svojim imenom, za dvanaest plemena.
22 “Upange timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe.
I na naprsnik metni lance jednake, pletene, od èistoga zlata.
23 Upangenso mphete ziwiri zagolide ndipo uzimangirire pa ngodya ziwiri za pa chovala chapachifuwa.
I dvije grivne zlatne naèini na naprsnik, i metni dvije grivne na dva kraja naprsniku.
24 Umangirire timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho.
Pa provuci dva lanca zlatna kroz dvije grivne na krajevima naprsniku.
25 Ndipo mbali ina ya timaunyoloto umangirire pa zoyikapo zake ziwiri zija ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.
A druga dva kraja od dva lanca zapni za dvije kopèe, i metni na poramenice od opleæka sprijed.
26 Upangenso mphete ziwiri zagolide, ndipo uzilumikize ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija.
I naèini druge dvije grivne zlatne, i metni ih na druga dva kraja naprsniku iznutra na strani koja je od opleæka.
27 Upangenso mphete zina ziwiri zagolide ndipo uzilumikize kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi.
I naèini još dvije zlatne grivne, i metni ih na poramenice od opleæka ozdo prema sastavcima njegovijem, više pojasa na opleæku.
28 Tsono umangirire mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi.
Tako neka vežu naprsnik grivne njegove za grivne na opleæku vrvcom od porfire, da stoji nad pojasom od opleæka, i da se ne odvaja naprsnik od opleæka.
29 “Pamene Aaroni akulowa kumalo opatulika azivala chovala chapachifuwa cha zoweruzira chija chimene chalembedwa mayina a ana a Israeli kuti Yehova awakumbukire nthawi zonse.
I neka nosi Aron imena sinova Izrailjevih na naprsniku sudskom na srcu svom kad ulazi u svetinju za spomen pred Gospodom vazda.
30 Ndiponso uyike Urimu ndi Tumimu mu chovala chapachifuwa cha zoweruziracho, kuti zikhale pamtima pa Aaroni. Choncho Aaroniyo adzakhala akutenga nthawi zonse zida zomuthandizira kuweruza ana a Israeli pamene adzafika pamaso pa Yehova.
I metni na naprsnik sudski Urim i Tumim, da bude na srcu Aronu kad ulazi pred Gospoda, i Aron æe nositi sud sinova Izrailjevih na srcu svom pred Gospodom vazda.
31 “Uyipangire efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo.
I naèini plašt pod opleæak sav od porfire.
32 Mkanjowo ukhala ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo pakhale chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike.
I ozgo neka bude prorez u srijedi, i neka bude optoèen prorez svuda unaokolo trakom tkanijem, kao prorez u oklopa, da se ne razdre.
33 Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, upange mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira zokhala ndi maberu agolide pakati pake.
A po skutu mu naèini šipke od porfire i od skerleta i od crvca svuda unaokolo, i meðu njima zlatna zvonca svuda unaokolo:
34 Choncho pazikhala mphonje imodzi kenaka belu limodzi, kuzungulira mpendero wa mkanjo wonse.
Zvonce zlatno pa šipak, zvonce zlatno pa šipak po skutu od plašta svuda unaokolo.
35 Aaroni azivala mkanjowo pamene akutumikira ngati wansembe. Kulira kwa maberu kuzimveka pamene akulowa mʼmalo opatulika pamaso pa Yehova ndiponso pamene akutuluka, kuti asafe.
I to æe biti na Aronu kad služi, da se èuje glas kad ulazi u svetinju pred Gospoda i kad izlazi, da ne pogine.
36 “Upange duwa lagolide wabwino kwambiri kukhala ngati chidindo ndipo uzokotepo mawu akuti, Cohoperekedwa kwa Yehova.
I naèini ploèu od èistoga zlata, i na njoj izreži kao na peèatu: svetinja Gospodu.
37 Ulimange ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira ya Aaroni, ndipo duwalo likhale kutsogolo kwa nduwirayo.
I veži je vrvcom od porfire za kapu, sprijed na kapi da stoji.
38 Lidzakhala pa mphumi ya Aaroni, motero iye adzasenza cholakwa chilichonse cha pa zopereka zilizonse zimene Aisraeli amazipatulira Yehova. Aaroni azivala chikwangwanichi pa mphumi pake nthawi zonse kuti Yehova alandire zopereka za anthu ake.
I biæe na èelu Aronovu, da nosi Aron grijehe svetijeh prinosa koje prinesu sinovi Izrailjevi u svijem darovima svojih svetijeh prinosa; biæe na èelu njegovu vazda, da bi bili mili Gospodu.
39 “Uluke mwinjiro wa nsalu yofewa yosalala ndiponso upange nduwira ya nsalu yofewa yosalala. Lamba wake akhale wolukidwa bwino ndi munthu waluso.
I naèini košulju od tankoga platna izmetanoga, i naèini kapu od tankoga platna, a pojas naèini vezen.
40 Upangirenso ana a Aaroni mwinjiro, malamba ndi nduwira kuti azioneka mwaulemu ndi molemekezeka.
I sinovima Aronovijem naèini košulje, i naèini im pojase, i kapice im naèini za èast i diku.
41 Zovala zimenezi umuveke Aaroni, mʼbale wako ndi ana ake. Kenaka uwadzoze, uwapatse udindo ndi kuwapatula kuti anditumikire ngati ansembe anga.
Pa to obuci Aronu bratu svojemu i sinovima njegovijem, i pomaži ih i napuni im ruke i posveti ih da mi budu sveštenici.
42 “Uwapangire akabudula a nsalu yofewa oyambira mʼchiwuno kulekeza mʼntchafu kuti asamaonetse maliseche.
I naèini im gaæe lanene, da se pokrije golo tijelo; od bedara do dno stegna da budu.
43 Aaroni ndi ana ake ayenera kuvala akabudulawo pamene akulowa mu tenti ya msonkhano kapena pamene akupita ku guwa lansembe kukatumikira malo oyera kuopa kuti angachimwe ndi kufa. “Ili likhale lamulo la nthawi zonse kwa Aaroni ndi zidzukulu zake.”
I to neka je na Aronu i na sinovima njegovijem kad ulaze u šator od sastanka ili kad pristupaju k oltaru da služe u svetinji, da ne bi noseæi grijehe poginuli. Ovo æe biti uredba vjeèna njemu i sjemenu njegovu nakon njega.

< Eksodo 28 >