< Eksodo 22 >

1 “Ngati munthu aba ngʼombe kapena nkhosa ndi kuyipha kapena kuyigulitsa, iye abweze ngʼombe zisanu pa ngʼombe imodzi ndi nkhosa zinayi pa nkhosa imodzi.
Ko ukrade vola ili ovcu ili kozu, i zakolje ili proda, da vrati pet volova za jednoga vola, a èetiri ovce ili koze za jednu ovcu ili kozu.
2 “Ngati mbala ipezeka ikuthyola nyumba ndipo imenyedwa nʼkufa, amene wapha mbalayo sanalakwe.
Ako se lupež uhvati gdje potkopava, te bude ranjen tako da umre, da ne bude kriv za krv onaj koji ga bude ubio;
3 Koma akayipha dzuwa litatuluka, woyiphayo ali ndi mlandu wakupha. “Mbala iyenera kubweza ndithu koma ngati ilibe kalikonse igulitsidwe, kulipira zomwe yabazo.
Ali ako se bude sunce rodilo, da je kriv za krv. A lupež sve da naknadi; ako li ne bi imao, onda da se on proda za svoju kraðu.
4 “Ngati chiweto chobedwacho chipezeka chamoyo mʼmanja mwake, kaya ndi ngʼombe kapena bulu kapena nkhosa, mbalayo ibwezere ziweto ziwiri pa chiweto chobedwacho.
Ako se naðe što je pokrao u njegovoj ruci živo, bio vo ili magarac ili ovca ili koza, da vrati dvostruko.
5 “Ngati munthu alekerera ziweto zake kukalowa mʼmunda wa munthu wina kukadya mbewu zake, munthuyo amubwezere mwini mundawo mbewu zina zabwino kapena mpesa wina wabwino kwambiri.
Ko potre njivu ili vinograd pustivši stoku svoju da pase po tuðoj njivi, da naknadi najboljim sa svoje njive i najboljim iz svoga vinograda.
6 “Ngati munthu ayatsa moto, motowo ndikukafika mpaka ku munda ndi kuwotcha mulu wa tirigu kapena tirigu wosadula, kapena munda wonse, ndiye kuti munthu amene anayatsa motoyo alipire.
Ako izaðe vatra i naiðe na trnje, pa izgori stog ili žito koje još stoji ili njiva, da naknadi onaj koji je zapalio.
7 “Ngati munthu asungitsidwa ndi mnzake ndalama kapena katundu, ndipo zinthu zija nʼkubedwa mʼnyumba mwake, wakubayo ngati agwidwa, ayenera kubwezera kawiri chobedwacho.
Ako ko da bližnjemu svojemu novce ili posuðe na ostavu, pa se ukrade iz kuæe njegove, ako se naðe lupež, da plati dvojinom;
8 Koma ngati mbalayo sipezeka, mwini nyumbayo ayenera kukaonekera ku bwalo lamilandu kuti akamve ngati anaba katundu wa mnzakeyo.
Ako li se ne naðe lupež, onda gospodar od one kuæe da stane pred sudije da se zakune da nije posegao rukom svojom na stvar bližnjega svojega.
9 Ngati pali kukangana kokhudza ngʼombe, bulu, nkhosa, zovala kapena kanthu kalikonse kotayika, ndipo mmodzi ndikunena kuti chinthucho nʼchake, awiriwo abwere nawo mlandu wawowo pamaso pa Mulungu ndipo amene mlandu umugomere adzayenera kumulipira mnzakeyo kawiri.
Za svaku stvar za koju bi bila raspra, ili za vola ili za magarca ili za ovcu ili za kozu, ili za haljinu, za svaku stvar izgubljenu, kad ko kaže da je njegova, pred sudije da doðe raspra obojice, pa koga osude sudije, onaj da vrati bližnjemu svojemu dvojinom.
10 “Ngati munthu wina anasungitsa mnzake bulu, ngʼombe, nkhosa, kapena chiweto chilichonse ndipo chiweto chija nʼkufa kapena kupweteka kapena kutengedwa popanda wina kuona,
Ako ko da bližnjemu svojemu da èuva magarca ili vola ili ovcu ili kozu ili kako god živinèe, pa ugine ili ohrone, ili ga ko otjera a da niko ne vidi,
11 ndiye kuti anthu awiriwo ayenera kulumbira pamaso pa Mulungu kuti asatenge chinthu cha mnzake. Zikatero mwini katundu uja avomereze zimenezi ndipo asabwezeredwe kanthu.
Zakletva Gospodnja neka bude izmeðu njih, da nije posegao rukom svojom na stvar bližnjega svojega, i gospodar od stvari neka pristane, a onaj da ne plati.
12 Koma ngati chiwetocho chinabedwa, iye ayenera kubwezera mwini wakeyo.
Ako li mu bude ukradeno, neka plati gospodaru njegovu.
13 Ngati chinagwidwa ndi zirombo, iye ayenera kubweretsa zotsalira ngati umboni ndipo sadzalipira kanthu.
Ako li ga bude rastrgla zvjerka da donese od njega svjedodžbu, i da ne plati što je rastrgnuto.
14 “Ngati munthu abwereka chiweto cha mnzake ndipo chiweto chija nʼkuvulala kapena kufa chikanali ndi iyebe, wobwerekayo ayenera kulipira.
Ako ko uzme u bližnjega svojega živinèe na poslugu, pa ohrone ili ugine, a gospodar mu ne bude kod njega, da plati.
15 Koma ngati mwini wakeyo ali ndi chiwetocho, wobwerekayo sadzalipira. Ngati anapereka ndalama pobwereka chiwetocho, ndalama anaperekazo zilowa mʼmalo mwa chiweto chakufacho.
Ako li gospodar bude kod njega, da ne plati. Ako li bude najmljeno, da plati samo najam.
16 “Ngati munthu anyenga namwali wosadziwa mwamuna amene sanapalidwe ubwenzi ndi kugona naye, munthuyo ayenera kulipira malowolo ndipo adzakhala mkazi wake.
Ko bi prevario djevojku, koja nije zaruèena, te bi spavao s njom, da joj da præiju i uzme je za ženu.
17 Ngati abambo ake akanitsitsa kwamtuwagalu kumupereka kuti amukwatire, munthuyo aperekebe malowolo woyenera namwaliyo.
A ako mu je otac njezin ne bi htio dati, da da novaca koliko ide u præiju djevojci.
18 “Musayilole mfiti yayikazi kuti ikhale ndi moyo.
Vještici ne daj da živi.
19 “Aliyense wogonana ndi chiweto ayenera kuphedwa.
Ko bi obležao živinèe, da se pogubi.
20 “Aliyense wopereka nsembe kwa mulungu wina osati Yehova awonongedwe.
Ko žrtvu prinosi bogovima drugim osim jedinoga Gospoda, da se istrijebi kao prokletnik.
21 “Musazunze mlendo kapena kumuchitira nkhanza, pakuti inu munali alendo mʼdziko la Igupto.
Došljaku nemoj èiniti krivo niti ga cvijeliti, jer ste bili došljaci u zemlji Misirskoj.
22 “Musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye.
Nemojte cvijeliti udovice i sirote.
23 Ngati muwazunza ndipo iwo nʼkulirira kwa Ine, ndidzamva kulira kwawo.
Ako li koju cvijeliš u èem god, i povièe k meni, èuæu viku njezinu,
24 Ine ndidzakukwiyirani ndipo ndidzakuphani ndi lupanga. Akazi anu adzakhala amasiye ndiponso ana anu adzakhala wopanda abambo.
I zapaliæe se gnjev moj, i pobiæu vas maèem, pa æe vaše žene biti udovice i vaša djeca sirote.
25 “Ngati mukongoza ndalama kwa mʼbale wanu amene ndi mʼmphawi pakati panu, musadzamuchite monga zimene amachita wokongoza ndalama. Musadzamuyikire chiwongoladzanja.
Kad daš u zajam novaca narodu mojemu, siromahu koji je kod tebe, nemoj mu biti kao kamatnik, ne udarajte na nj kamate.
26 Mukatenga chovala cha mnzanu kuti chikhale chikole mumubwezere dzuwa lisanalowe
Ako uzmeš u zalogu haljinu bližnjemu svojemu, vrati mu je prije nego sunce zaðe;
27 chifukwa chovala chimene amadzifundira nacho nʼchomwecho. Nanga usiku adzafunda chiyani? Tsonotu ngati adzandilirira, Ine ndidzamva pakuti ndine wachifundo.
Jer mu je to sve odijelo èim zaklanja tijelo svoje; u èem æe spavati? pa kad povièe k meni, ja æu ga èuti, jer sam milostiv.
28 “Musachite chipongwe Mulungu wanu kapena kutemberera mtsogoleri wa anthu anu.
Nemoj psovati sudija, i starješini naroda svojega ne govori ružno.
29 “Musachedwe kupereka kwa Ine zokolola zanu zochuluka ndi vinyo wanu wochuluka. “Mundipatse ana anu achisamba aamuna.
Od ljetine svoje i od žitkih stvari svojih nemoj se zatezati da prineseš prvine; prvenca izmeðu sinova svojih meni da daš.
30 Muchite chimodzimodzi ndi ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu. Mwana woyamba kubadwa azikhala ndi amayi ake masiku asanu ndi awiri. Koma pa tsiku lachisanu ndi chitatu mwanayo muzimupereka kwa Ine.
Tako èini s volom svojim i s ovcom i s kozom; sedam dana neka bude s majkom svojom, a osmoga dana da ga daš meni.
31 “Inu mukhale anthu anga opatulika. Choncho musadye nyama ya chiweto chimene chaphedwa ndi zirombo. Nyamayo muwaponyere agalu.”
Biæete mi sveti ljudi; mesa u polju rastrgnuta ne jedite, bacite ga psima.

< Eksodo 22 >