< Eksodo 18 >

1 Yetero wansembe wa ku Midiyani amenenso anali mpongozi wa Mose, anamva zonse zimene Mulungu anachitira Mose ndi anthu ake a Aisraeli ndi mmene Yehova anawatulutsira mʼdziko la Igupto.
Jethro, the priest of Midian, Moses' father-in-law, heard of all that God had done for Moses and for Israel his people. He heard that Yahweh had brought Israel out of Egypt.
2 Mose atamubweza Zipora, mkazi wake, Yetero, mpongozi wake anamulandira
Jethro, Moses' father-in-law, took Zipporah, Moses' wife, after he had sent her home,
3 mwana wake wamkaziyo pamodzi ndi ana ake aamuna awiri. Mose anamupatsa mwana wachisamba dzina loti Geresomu popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko lachilendo.”
and her two sons; the name of the one son was Gershom, for Moses had said, “I have been a foreigner in a foreign land.”
4 Ndipo mwana wake wachiwiri anamupatsa dzina loti Eliezara, pakuti anati, “Mulungu wa makolo anga anali thandizo langa. Iye anandipulumutsa ku lupanga la Farao.”
The name of the other was Eliezer, for Moses had said, “My ancestor's God was my help. He rescued me from Pharaoh's sword.”
5 Yetero, mpongozi wa Mose pamodzi ndi ana a Mose aamuna awiri ndi mkazi wake anabwera kwa Mose ku chipululu pa phiri la Mulungu kumene Mose anamanga misasa.
Jethro, Moses' father-in-law, came with Moses' sons and his wife to Moses in the wilderness where he was camped at the mountain of God.
6 Yetero anali atatumiza uthenga kwa Mose kuti, “Ine Yetero, mpongozi wako, ndikubwera ndi mkazi wako ndi ana ake awiri.”
He said to Moses, “I, your father-in-law Jethro, am coming to you with your wife and her two sons.”
7 Kotero Mose anatuluka kukakumana ndi mpongozi wake ndipo anawerama ndi kupsompsona. Atalonjerana anakalowa mu tenti
Moses went out to meet his father-in-law, bowed down, and kissed him. They asked about each other's welfare and then went into the tent.
8 Mose anafotokozera mpongozi wake zonse zimene Yehova anamuchita Farao ndi Aigupto chifukwa cha Israeli komanso zowawa zonse anakumana nazo mʼnjira. Mose anafotokozanso momwe Yehova anawapulumutsira.
Moses told his father-in-law all that Yahweh had done to Pharaoh and the Egyptians for Israel's sake, about all the hardships that had come to them along the way, and how Yahweh had rescued them.
9 Yetero anakondwa kwambiri atamva zabwino zonse zimene Yehova anachitira Aisraeli powapulumutsa mʼdzanja la Aigupto.
Jethro rejoiced over all the good that Yahweh had done for Israel, in that he had rescued them from the hand of the Egyptians.
10 Iye anati, “Alemekezeke Yehova amene wakupulumutsani mʼdzanja la Aigupto ndi Farao. Wapulumutsanso anthuwa mʼdzanja la Aigupto.
Jethro said, “May Yahweh be praised, for he has rescued you from the hand of the Egyptians and from the hand of Pharaoh, and delivered the people from the hand of the Egyptians.
11 Tsopano ndikudziwa kuti Yehova ndi wopambana milungu ina yonse, pakuti anachita izi kwa amene ananyoza Israeli.”
Now I know that Yahweh is greater than all the gods, because when the Egyptians treated the Israelites arrogantly, God rescued his people.”
12 Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Mulungu. Aaroni ndi akuluakulu onse a Israeli anabwera kudzadya chakudya pamodzi ndi mpongozi wa Mose pamaso pa Mulungu.
Jethro, Moses' father-in-law, brought a burnt offering and sacrifices for God. Aaron and all the elders of Israel came to eat a meal before God with Moses' father-in-law.
13 Mmawa mwake, Mose anakhala pa mpando kuti aweruze milandu ya anthu. Anthu anayima momuzungulira kuyambira mmawa mpaka madzulo.
On the next day Moses sat down to judge the people. The people stood around him from morning until evening.
14 Mpongozi wa Mose ataona zonse zimene iye amawachitira anthu anati, “Nʼchiyani chimene mukuwachitira anthuwa? Nʼchifukwa chiyani mulipo nokha woweruza, pamene anthu onsewa ayimirira kuyambira mmawa mpaka madzulo?”
When Moses' father-in-law saw all that he did for the people, he said, “What is this that you are doing with the people? Why is it that you sit alone and all the people stand about you from morning until evening?”
15 Mose anamuyankha kuti, “Chifukwa anthuwa anabwera kwa ine kudzafunsa zimene Mulungu akufuna.
Moses said to his father-in-law, “The people come to me to ask for God's direction.
16 Ngati munthu akangana ndi mʼbale wake, onse awiri amabwera kwa ine, ndipo ine ndimawaweruza. Ndimawawuzanso malamulo a Mulungu ndi malangizo ake.”
When they have a dispute, they come to me. I decide between one person and another, and I teach them God's statutes and laws.”
17 Mpongozi wa Mose anayankha kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino.
Moses' father-in-law said to him, “What you are doing is not very good.
18 Ntchitoyi ndi yayikulu kuposa mphamvu zanu. Inu simungathe kuyigwira nokha. Inu pamodzi ndi anthuwa amene amabwera kwa inu mudzatopa.
You will surely wear yourselves out, you and the people who are with you. This burden is too heavy for you. You are not able to do it by yourself.
19 Tsono tamverani ndikulangizeni, ndipo Mulungu akhale nanu. Inu muziwayimirira anthuwa pamaso pa Mulungu, ndipo mikangano yawo muzibwera nayo kwa Iye.
Listen to me. I will give you advice, and God will be with you, because you are the people's representative to God, and you bring their disputes to him.
20 Aphunzitseni mawu ndi malangizo a Mulungu. Aphunzitseni mmene ayenera kukhalira ndi zimene ayenera kuchita.
You must teach them his statutes and laws. You must show them the way to walk and the work to do.
21 Koma sankhani amuna odziwa ntchito yawo, anthu owopa Mulungu, anthu odalirika amene amadana ndi kupeza phindu mwachinyengo. Tsono muwayike kuti akhale oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 100, ena a anthu 50 ndi ena a anthu khumi.
Furthermore, you must choose capable men from all the people, men who honor God, men of truth who hate unjust gain. You must put them over people, to be leaders in charge of thousands, hundreds, fifties, and of tens.
22 Tsono amenewa aziweruza anthu nthawi zonse. Mlandu uliwonse waukulu azibwera nawo kwa inu, koma mlandu waungʼono aziweruza okha. Izi zidzachititsa kuti ntchito yanu ipepuke, popeza mudzagwira ntchito mothandizana.
They will judge the people in all routine cases, but the difficult cases they will bring to you. As for all the small cases, they can judge those themselves. In that way it will be easier for you, and they will carry the burden with you.
23 Ngati mutsatira malangizowa monga mmene Mulungu wakulamulirani ndiye kuti simudzafowoka ndipo anthu onsewa adzapita kwawo mu mtendere.”
If you do this, and if God commands you to do so, then you will be able to endure, and the entire people will be able to go home satisfied.”
24 Mose anamvera mpongozi wake ndi kuchita zonse zimene iye ananena.
So Moses listened to his father-in-law's words and did everything that he had said.
25 Iye anasankha amuna odziwa bwino ntchito zawo ndipo anawayika kuti akhale atsogoleri, oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 500, ena a anthu makumi asanu ndi ena a anthu khumi.
Moses chose capable men from all Israel and made them heads over the people, leaders in charge of thousands, hundreds, fifties, and tens.
26 Iwowa ankaweruza anthu nthawi zonse. Milandu yovuta ankabwera nayo kwa Mose, koma yosavuta ankayiweruza okha.
They judged the people in normal circumstances. The difficult cases they brought to Moses, but they themselves judged all the small cases.
27 Kenaka Mose analola kuti mpongozi wake, Yetero anyamuke kubwerera ku dziko la kwawo.
Then Moses let his father-in-law leave, and Jethro went back into his own land.

< Eksodo 18 >