< Eksodo 17 >

1 Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku chipululu cha Sini, ndi kumayenda malo ndi malo monga momwe anawalamulira Yehova. Iwo anamanga misasa yawo ku Refidimu koma kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa.
I podiže se iz pustinje Sina sav zbor sinova Izrailjevih putem svojim po zapovjesti Gospodnjoj, i stadoše u oko u Rafidinu; a ondje ne bješe vode da narod pije.
2 Kotero iwo anakangana ndi Mose nati, “Tipatse madzi akumwa.” Mose anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukukangana ndi ine? Chifukwa chiyani mukumuyesa Yehova?”
I narod se svaðaše s Mojsijem govoreæi: daj nam vode da pijemo. A on im reèe: što se svaðate sa mnom? što kušate Gospoda?
3 Koma anthu anali ndi ludzu pamenepo ndipo anangʼungʼudza pamaso pa Mose namufunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto kuti ife, ana athu pamodzi ndi ziweto zathu tife ndi ludzu?”
Ali narod bješe ondje žedan vode, te vikaše narod na Mojsija, i govoraše: zašto si nas izveo iz Misira da nas i sinove naše i stoku našu pomoriš žeðu?
4 Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, “Kodi ndichite chiyani ndi anthu awa? Iwo atsala pangʼono kundigenda ndi miyala.”
A Mojsije zavapi ka Gospodu govoreæi: šta æu èiniti s ovijem narodom? Još malo pa æe me zasuti kamenjem.
5 Yehova anati kwa Mose, “Pita patsogolo pa anthuwo. Tenga ndodo imene unamenyera nyanja ya Nailo pamodzi ndi akuluakulu ena a Israeli ndi kunyamuka.
A Gospod reèe Mojsiju: proði pred narod, i uzmi sa sobom starješine Izrailjske, i štap svoj kojim si udario vodu uzmi u ruku svoju, i idi.
6 Ine ndidzayima patsogolo pako pafupi ndi thanthwe la ku Horebu. Ukamenye thanthwelo, madzi adzatuluka kuti anthu amwe.” Motero Mose anachita zimenezi pamaso pa akuluakulu a Israeli.
A ja æu stajati pred tobom ondje na stijeni na Horivu; a ti udari u stijenu, i poteæi æe iz nje voda da pije narod. I uèini Mojsije tako pred starješinama Izrailjskim.
7 Ndipo iye anatcha malowo Masa ndi Meriba chifukwa Aisraeli anakangana ndi kuyesa Yehova ponena kuti, “Kodi pakati pathu pali Yehova kapena palibe?”
A mjesto ono prozva Masa i Meriva zato što se svaðaše sinovi Izrailjevi i što kušaše Gospoda govoreæi: je li Gospod meðu nama ili nije?
8 Amaleki anabwera ku Refidimu kudzamenyana ndi Aisraeli.
Ali doðe Amalik da se bije s Izrailjem u Rafidinu.
9 Mose anati kwa Yoswa, “Sankha amuna amphamvu ndipo upite ukamenyane ndi Amaleki. Mawa ndidzayima pamwamba pa phiri nditagwira ndodo ya Mulungu.”
A Mojsije reèe Isusu: izberi nam ljude, te izaði i bij se s Amalikom; a ja æu sjutra stati na vrh brda sa štapom Božjim u ruci.
10 Ndipo Yoswa anachitadi monga Mose anamulamulira. Iye anapita kukamenyana ndi Aamaleki ndipo Mose, Aaroni ndi Huri anapita pamwamba pa phiri.
I uèini Isus kako mu reèe Mojsije, i pobi se s Amalikom; a Mojsije i Aron i Or izaðoše na vrh brda.
11 Mose ankati akakweza manja ake, Aisraeli amapambana, koma akatsitsa manja akewo Amaleki amapambana.
I dokle Mojsije držaše u vis ruke svoje, nadbijahu Izrailjci, a kako bi spustio ruke, odmah nadbijahu Amalièani.
12 Manja a Mose atatopa, Aaroni ndi Huri anatenga mwala ndi kuyika pansi ndipo Mose anakhalapo. Aaroni ndi Huri anagwirizitsa manja a Mose wina mbali ina winanso mbali ina. Choncho manja a Mose analimba mpaka kulowa kwa dzuwa.
Ali ruke Mojsiju otežaše, zato uzeše kamen i podmetnuše poda nj, te sjede; a Aron i Or držahu mu ruke jedan s jedne strane a drugi s druge, i ne klonuše mu ruke do zahoda sunèanoga.
13 Kotero Yoswa anagonjetsa asilikali ankhondo a Amaleki ndi lupanga.
I razbi Isus Amalika i narod njegov oštrijem maèem.
14 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Lemba izi mʼbuku kuti zidzakumbukirike ndipo uwonetsetse kuti Yoswa amve zimenezi, chifukwa Ine ndidzafafaniziratu Amaleki pa dziko lapansi, kotero kuti palibe amene adzawakumbukire.”
Potom reèe Gospod Mojsiju: zapiši to za spomen u knjigu, i kaži Isusu neka pamti da æu sasvijem istrijebiti spomen Amalikov ispod neba.
15 Mose anamanga guwa lansembe ndipo analitcha Yehova Chipambano Changa (Yehova Nisi).
Tada naèini Mojsije oltar, i nazva ga: Gospod zastava moja.
16 Ndipo anati, “Kwezani mbendera ya Yehova. Yehova adzachitabe nkhondo ndi mibado yonse ya Aamaleki.”
I reèe: što se ruka bješe podigla na prijesto Gospodnji, Gospod æe ratovati na Amalika od koljena do koljena.

< Eksodo 17 >