< Eksodo 14 >

1 Kenaka Yehova anati kwa Mose,
I reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
2 “Uza Aisraeli abwerere ndi kukagona pafupi ndi Pihahiroti, pakati pa Migidoli ndi nyanja. Inu mumange zithando mʼmbali mwa nyanja moyangʼanana ndi Baala-Zefoni.
Kaži sinovima Izrailjevijem neka saviju i stanu u oko pred Pi-Airot izmeðu Migdola i mora prema Vel-Sefonu; prema njemu neka stanu u oko pokraj mora.
3 Farao adzaganiza kuti ‘Aisraeli asokonezeka nʼkumangozungulirazungulira mu dzikomo, chipululu chitawazinga.’
Jer æe Faraon reæi za sinove Izrailjeve: zašli su u zemlju, zatvorila ih je pustinja.
4 Ndidzawumitsa mtima wa Farao ndipo adzathamangira Aisraeliwo. Choncho ndikadzagonjetsa Farao ndi gulu lake lonse la nkhondo, Ine ndidzalemekezedwa.” Choncho Aisraeli aja anachita zimenezi.
I uèiniæu da otvrdne srce Faraonu, te æe poæi u potjeru za vama, i ja æu se proslaviti na njemu i na svoj vojsci njegovoj, i Misirci æe poznati da sam ja Gospod. I uèiniše tako.
5 Farao, mfumu ya Igupto atamva kuti anthu aja athawa, iye pamodzi ndi nduna zake anasintha maganizo awo pa Israeli ndipo anati, “Ife tachita chiyani? Tawalola Aisraeli kuti apite ndi kuleka kutitumikira?”
A kad bi javljeno caru Misirskom da je pobjegao narod, promijeni se srce Faraonovo i sluga njegovijeh prema narodu, te rekoše: šta uèinismo, te pustismo Izrailja da nam ne služi?
6 Choncho anakonzetsa galeta lake ndipo ananyamuka pamodzi ndi ankhondo ake.
I upreže u kola svoja, i uze narod svoj sa sobom.
7 Iye anatenga magaleta 600 abwino kwambiri pamodzi ndi magaleta ena a dziko la Igupto. Anatenganso akuluakulu onse ankhondo.
I uze šest stotina kola izabranih i što još bješe kola Misirskih, i nad svjema vojvode.
8 Yehova anawumitsa mtima wa Farao mfumu ya dziko la Igupto, kotero iye anawathamangira Aisraeli amene ankachoka mʼdzikomo mosavutika.
I Gospod uèini, te otvrdnu srce Faraonu caru Misirskom, i poðe u potjeru za sinovima Izrailjevijem, kad sinovi Izrailjevi otidoše pod rukom visokom.
9 Aigupto aja (kutanthauza akavalo ndi magaleta onse a Farao, okwera akavalowo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo) analondola Aisraeli aja ndipo anakawapeza pamalo pamene anamanga zithando paja, mʼmbali mwa nyanja, pafupi ndi Pihahiroti, moyangʼanana ndi Baala-Zefoni.
I tjeravši ih Misirci stigoše ih, sva kola Faraonova, konjici njegovi i vojska njegova, kad bjehu u okolu na moru kod Pi-Airota prema Vel-Sefonu.
10 Tsono Farao anayandikira. Ndipo Aisraeli ataona kuti Aigupto akuwatsatira, anachita mantha aakulu ndipo anafuwula kwa Yehova.
I kad se približi Faraon, podigoše sinovi Izrailjevi oèi svoje a to Misirci idu za njima, i uplašiše se vrlo, i povikaše sinovi Izrailjevi ka Gospodu.
11 Iwo anafunsa Mose kuti, “Kodi nʼchifukwa chakuti kunalibe manda ku dziko la Igupto kuti iwe utibweretse muno mʼchipululu kuti tidzafe? Chimene watichitachi nʼchiyani, kutitulutsa mʼdziko la Igupto?
I rekoše Mojsiju: zar ne bješe grobova u Misiru, nego nas dovede da izginemo u pustinji? Šta uèini, te nas izvede iz Misira?
12 Kodi sindizo zimene tinakuwuza mʼdziko la Igupto? Ife tinati, ‘Tileke titumikire Aigupto?’ Zikanatikomera kutumikira Aigupto kulekana ndi kufa mʼchipululu muno.”
Nijesmo li ti govorili u Misiru i rekli: proði nas se, neka služimo Misircima? jer bi nam bolje bilo služiti Misircima nego izginuti u pustinji.
13 Mose anayankha anthu kuti, “Musachite mantha. Imani, ndipo muone chipulumutso chimene Yehova akuchitireni lero. Aigupto amene mukuwaona lerowa simudzawaonanso.
A Mojsije reèe narodu: ne bojte se, stanite pa gledajte kako æe vas Gospod izbaviti danas; jer Misirce koje ste vidjeli danas, neæete ih nigda više vidjeti dovijeka.
14 Yehova adzakumenyerani nkhondo. Inu mungokhala chete.”
Gospod æe se biti za vas, a vi æete muèati.
15 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Chifukwa chiyani ukufuwulira kwa ine? Uwuze Aisraeli aziyenda.
A Gospod reèe Mojsiju: što vièeš k meni? kaži sinovima Izrailjevijem neka idu.
16 Nyamula ndodo yako ndi kutambasula dzanja lako kuloza ku nyanja, kugawa madzi kuti Aisraeli awoloke powuma.
A ti digni štap svoj i pruži ruku svoju na more, i rascijepi ga, pa neka idu sinovi Izrailjevi posred mora suhim.
17 Ine ndidzawumitsa mitima ya Aigupto kotero kuti adzatsatirabe Aisraeli. Ndipo ine ndikadzagonjetsa Farao ndi asilikali ake onse ankhondo, okwera magaleta ndi akavalo, ndidzapeza ulemerero.
I gle, ja æu uèiniti da otvrdne srce Misircima, te æe poæi za njima; i proslaviæu se na Faraonu i na svoj vojsci njegovoj, na kolima njegovijem i na konjicima njegovijem.
18 Aigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova akadzaona mmene ndipambanire Farao ndi magaleta ndi owayendetsa ake.”
I Misirci æe poznati da sam ja Gospod, kad se proslavim na Faraonu, na kolima njegovijem i na konjicima njegovijem.
19 Ndipo mngelo wa Mulungu amene amayenda patsogolo pa gulu lankhondo la Israeli anachoka ndi kupita kumbuyo kwawo. Chipilala cha mtambo chinasunthanso kuchoka kutsogolo ndi kupita kumbuyo kwawo.
I podiže se anðeo Gospodnji, koji iðaše pred vojskom Izrailjskom, i otide im za leða; i podiže se stup od oblaka ispred njih, i stade im za leða.
20 Choncho mtambowo unakhala pakati pa asilikali ankhondo a dziko la Igupto ndi a dziko la Israeli. Choncho panali mdima motero kuti magulu awiri ankhondowa sanathe kuyandikizana usiku wonse.
i došav meðu vojsku Misirsku i vojsku Izrailjsku bješe onijem oblak mraèan a ovijem svijetljaše po noæi, te ne pristupiše jedni drugima cijelu noæ.
21 Kenaka Mose anatambalitsa dzanja lake pa nyanja, ndipo Yehova pogwiritsa ntchito mphepo yamphamvu ya kummawa imene inawomba usiku wonse anabweza madzi ndi kuwumitsa nyanja ija. Choncho nyanja ija inagawanika.
I pruži Mojsije ruku svoju na more, a Gospod uzbi more vjetrom istoènijem, koji jako duvaše cijelu noæ, i osuši more, i voda se rastupi.
22 Ndipo Aisraeli anawoloka pakati pa nyanja powuma, madzi atasanduka khoma kumanja ndi kumanzere kwawo.
I poðoše sinovi Izrailjevi posred mora suhim, i voda im stajaše kao zid s desne strane i s lijeve strane.
23 Aigupto onse, Farao, ndi onse okwera pa magaleta ndi akavalo anawalondola ndipo analowa mʼmadzi.
I Misirci tjerajuæi ih poðoše za njima posred mora, svi konji Faraonovi, kola i konjici njegovi.
24 Kutatsala pangʼono kucha, Yehova ali mu chipilala chamoto ndi chamtambo, anayangʼana asilikali ankhondo a Igupto ndipo anabweretsa chisokonezo pakati pawo.
A u stražu jutrenju pogleda Gospod na vojsku Misirsku iz stupa od ognja i oblaka, i smete vojsku Misirsku.
25 Yehova anamanga matayala a magaleta kotero kuti ankavutika kuyenda. Ndipo Aigupto anati, “Tiyeni tiwathawe Aisraeli! Yehova akuwamenyera nkhondo kulimbana nafe.”
I pozbaca toèkove kolima njihovijem, te ih jedva vucijahu. Tada rekoše Misirci: bježimo od Izrailja, jer se Gospod bije za njih s Misircima.
26 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Tambasula dzanja lako pa nyanja kuti madzi amize Aigupto ndi magaleta awo ndi okwera pa akavalo.”
A Gospod reèe Mojsiju: pruži ruku svoju na more, neka se vrati voda na Misirce, na kola njihova i na konjike njihove.
27 Mose anatambasula dzanja lake pa nyanja, ndipo mmene kumacha nyanja inabwerera mʼmalo mwake. Aigupto pothawa anakumana nayo, ndipo Yehova anawakokera mʼnyanja momwemo.
I Mojsije pruži ruku svoju na more, i doðe opet more na silu svoju pred zoru, a Misirci nagoše bježati prema moru; i Gospod baci Misirce usred mora.
28 Madzi anabwerera ndi kumiza magaleta ndi okwera akavalo, asilikali ankhondo onse amene anatsatira Aisraeli mʼnyanja, palibe ndi mmodzi yemwe amene anapulumuka.
A vrativši se voda potopi kola i konjike sa svom vojskom Faraonovom, što ih god bješe pošlo za njima u more, i ne osta od njih nijedan.
29 Koma Aisraeli aja anawoloka nyanja pansi pali powuma, madzi atachita khoma kumanja ndi kumanzere kwawo.
I sinovi Izrailjevi iðahu posred mora suhim; i stajaše im voda kao zid s desne strane i s lijeve strane.
30 Tsiku limeneli Yehova anapulumutsa Israeli mʼmanja mwa Aigupto ndipo Israeli anaona Aigupto ali lambalamba mʼmbali mwa nyanja atafa
I izbavi Gospod Izrailja u onaj dan iz ruku Misirskih; i vidje Izrailj mrtve Misirce na brijegu morskom.
31 Choncho Aisraeli anaona dzanja lamphamvu la Yehova limene linagonjetsa Aigupto aja, ndipo iwo anaopa Yehova ndi kumukhulupirira pamodzi ndi mtumiki wake Mose.
I vidje Izrailj silu veliku, koju pokaza Gospod na Misircima, i narod se poboja Gospoda, i vjerova Gospodu i Mojsiju sluzi njegovu.

< Eksodo 14 >