< Eksodo 10 >

1 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa Farao, pakuti Ine ndawumitsa mtima wake ndi mitima ya nduna zake kuti ndichite zizindikiro zozizwitsa pakati pawo
A Gospod reèe Mojsiju: idi k Faraonu, jer sam ja uèinio da otvrdne srce njegovo i srce sluga njegovijeh, da uèinim ove znake svoje meðu njima,
2 kuti inu mudzawuze ana ndi zidzukulu zanu za mmene ndinawakhawulitsira Aigupto ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinachita pakati pawo ndiponso kuti inu mudziwe kuti ine ndine Yehova.”
I da pripovijedaš sinovima svojim i unucima svojim šta uèinih u Misiru i kakve znake svoje pokazah na njima, da biste znali da sam ja Gospod.
3 Ndipo Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndi kukanena kuti, “Yehova Mulungu wa Ahebri, akuti: ‘Kodi udzakanabe kudzichepetsa pamaso panga mpaka liti? Alole anthu anga apite kuti akandipembedze.
I otide Mojsije i Aron k Faraonu, i rekoše mu: ovako veli Gospod Bog Jevrejski: dokle æeš se protiviti da se ne poniziš preda mnom? Pusti narod moj da mi posluži.
4 Ngati ukana kuwalola, ndigwetsa dzombe mʼdziko lako lino mawa.
Jer ako neæeš pustiti naroda mojega, evo sjutra æu nanijeti skakavce na zemlju tvoju;
5 Dzombeli lidzakuta nthaka yonse moti sidzaoneka konse. Lidzadya kalikonse kakangʼono kamene sikanawonongedwe ndi matalala aja, kuphatikizapo mitengo yonse imene ikumera mʼminda yanu.
I pokriæe svu zemlju da se neæe vidjeti zemlje, i poješæe ostatak što se saèuvao, koji vam je ostao iza grada, i poješæe sva drveta što vam rastu u polju.
6 Dzombeli lidzadzaza nyumba zako ndi za nduna zako ndiponso za Aigupto onse, chinthu chimene ngakhale makolo anu kapena makolo awo sanachionepo kuyambira tsiku limene anakhala mʼdzikoli mpaka lero.’” Ndipo Mose ndi Aaroni anatembenuka ndi kumusiya Farao.
I napuniæe ih se kuæe tvoje i kuæe svijeh sluga tvojih i kuæe svijeh Misiraca, što nijesu vidjeli oci tvoji ni oci otaca tvojih, otkako su postali na zemlji do danas. I okrenuv se otide od Faraona.
7 Nduna za Farao zinamufunsa kuti, “Kodi munthu uyu adzativutitsa mpaka liti? Aloleni anthuwa apite, kuti akapembedze Yehova Mulungu wawo. Kodi simukuona kuti dziko la Igupto lawonongeka?”
A sluge rekoše Faraonu: dokle æe nas taj muèiti? Pusti ih neka posluže Gospodu Bogu svojemu. Zar još ne vidiš gdje propade Misir?
8 Choncho Mose ndi Aaroni anayitanidwanso kwa Farao ndipo anati, “Pitani kapembedzeni Yehova Mulungu wanu. Koma ndani amene adzapite?”
I dozvaše opet Mojsija i Arona pred Faraona, i reèe im: idite, poslužite Gospodu Bogu svojemu. A koji su što æe iæi?
9 Mose anayankha kuti, “Ife tidzapita tonse pamodzi; angʼonoangʼono ndi akuluakulu, ana athu aamuna ndi aakazi, ndiponso ziweto zathu ndi ngʼombe chifukwa tikakhala ndi chikondwerero cha kwa Yehova.”
A Mojsije reèe: s djecom svojom i sa starcima svojim iæi æemo, sa sinovima svojim i sa kæerima svojim, sa stokom svojom sitnom i krupnom iæi æemo, jer imamo praznik Gospodnji.
10 Farao anati, “Yehova akhale ndi inu ngati ndingakuloleni kupita pamodzi ndi akazi ndi ana anu! Zikuoneka kuti mwakonzeka kuchita choyipa.
A on im reèe: tako bio Gospod s vama, kako æu vas ja pustiti s djecom vašom! Vidite da zlo mislite.
11 Ndakana! Amuna okha ndiwo apite ndi kukapembedza Yehova pakuti izi ndi zimene mwakhala mukupempha.” Kenaka Mose ndi Aaroni anathamangitsidwa pamaso pa Farao.
Neæe biti tako; nego vi ljudi idite i poslužite Gospodu, jer to ištete. I otjera ih od sebe Faraon.
12 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Tambalitsa dzanja lako pa dziko la Igupto kuti dzombe lidze pa dziko la Igupto ndi kuwononga chilichonse chimene chikumera mʼminda ndi chilichonse chimene chinatsala pa nthawi ya matalala.”
Tada reèe Gospod Mojsiju: pruži ruku svoju na zemlju Misirsku, da doðu skakavci na zemlju Misirsku i pojedu sve bilje po zemlji, što god osta iza grada.
13 Kotero Mose anakweza ndodo yake pa dziko la Igupto, ndipo Yehova anawutsa mphepo ya kummawa imene inawomba pa dziko usana ndi usiku wonse. Mmene kumacha nʼkuti mphepoyo itabweretsa dzombe.
I pruži Mojsije štap svoj na zemlju Misirsku, i Gospod navede ustoku na zemlju, te duva cijeli dan i cijelu noæ; a kad svanu, donese ustoka skakavce.
14 Dzombelo linafika pa dziko lonse la Igupto ndi kukhala dera lililonse la dzikolo. Dzombe lambiri ngati limenelo silinakhaleponso nʼkale lonse ndipo silidzakhalapo ngakhale mʼtsogolo.
I doðoše skakavci na svu zemlju Misirsku, i popadaše po svijem krajevima Misirskim silni veoma, kakih prije nigda nije bilo niti æe kad biti onakih.
15 Dzombelo linaphimba nthaka yonse mpaka kuoneka kuti bii. Linadya zonse zimene zinatsala nthawi ya matalala, zomera za mʼmunda ndi zipatso. Panalibe chobiriwira chilichonse chimene chinatsala pa mtengo kapena pa chomera chilichonse mʼdziko lonse la Igupto.
I pokriše svu zemlju, da se zemlja ne viðaše, i pojedoše svu travu na zemlji i sav rod na drvetima, što osta iza grada, i ne osta ništa zeleno od drveta i od bilja poljskoga u svoj zemlji Misirskoj.
16 Mwamsangamsanga, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Ine ndachimwira Yehova Mulungu wanu ndiponso inu.
Tada Faraon brže dozva Mojsija i Arona, i reèe: zgriješih Gospodu Bogu vašemu i vama.
17 Tsopano ndikhululukirenso tchimo langa kano konkha ndipo pempherani kwa Yehova Mulungu wanu kuti andichotsere mliri wosakazawu.”
Ali mi još sada samo oprosti grijeh moj, i molite se Gospodu Bogu svojemu da ukloni od mene samo ovu smrt.
18 Mose anachoka kwa Farao nakapemphera kwa Yehova.
I otide Mojsije od Faraona, i pomoli se Gospodu.
19 Ndipo Yehova anasintha mphepo ija kuti ikhale ya mphamvu yochokera ku madzulo, ndipo inanyamula dzombe lija nʼkulikankhira mʼNyanja Yofiira. Panalibe dzombe ndi limodzi lomwe limene linatsala mu Igupto.
I okrenu Gospod vjetar od zapada vrlo jak, koji uze skakavce i baci ih u Crveno More, i ne osta nijedan skakavac u cijeloj zemlji Misirskoj.
20 Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole kuti Aisraeli apite.
Ali Gospod uèini te otvrdnu srce Faraonu, i ne pusti sinova Izrailjevijeh.
21 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Tambasulira dzanja lako kumwamba kuti kukhale mdima umene udzaphimba dziko lonse la Igupto, mdima wandiweyani.”
I reèe Gospod Mojsiju: pruži ruku svoju k nebu, i biæe tama po zemlji Misirskoj taka da æe je pipati.
22 Choncho Mose anakweza dzanja lake kumwamba ndipo mdima wandiweyani unaphimba dziko lonse la Igupto kwa masiku atatu.
I Mojsije pruži ruku svoju k nebu, i posta gusta tama po svoj zemlji Misirskoj za tri dana.
23 Palibe amene anatha kuona mnzake kapena kuchoka pa khomo pake kwa masiku atatu. Koma kumalo kumene kumakhala Aisraeli kunali kowala.
Ne viðahu jedan drugoga, i niko se ne maèe s mjesta gdje bješe za tri dana; ali se kod svijeh sinova Izrailjevijeh vidjelo po stanovima njihovijem.
24 Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kapembedzeni Yehova. Ngakhale akazi ndi ana anu apite pamodzi ndi inu. Koma musatenge ziweto zanu ndi ngʼombe zanu.”
Tada Faraon dozva Mojsija, i reèe: idite, poslužite Gospodu; samo stoka vaša sitna i krupna neka ostane, a djeca vaša neka idu s vama.
25 Koma Mose anati, “Ndiye inu mutipatse nsembe zopsereza zoti tikapereke kwa Yehova Mulungu wathu.
A Mojsije reèe: treba da nam daš i što æemo prinijeti i sažeæi na žrtvu Gospodu Bogu svojemu;
26 Koma ayi, ife tipita ndi ziweto zathu. Palibe chiweto chilichonse chimene chitatsale kuno, popeza tikasankha komweko ziweto zokapembedzera Yehova. Sitingadziwe zimene tikagwiritse ntchito popembedza Yehova mpaka titakafika kumeneko.”
Zato i stoka naša nek ide s nama, da ne ostane ni papka, jer izmeðu nje treba da uzmemo èim æemo poslužiti Gospodu Bogu svojemu, a ne znamo kojim æemo poslužiti Gospodu dokle ne doðemo onamo.
27 Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao ndipo sanafune kuwalola kuti apite.
Ali Gospod uèini te otvrdnu srce Faraonu, i ne htje ih pustiti.
28 Farao anati kwa Mose, “Choka pamaso panga! Uwonetsetse kuti usadzaonekerenso pamaso panga! Tsiku limene ndidzakuonenso udzafa.”
I reèe mu Faraon: idi od mene, i èuvaj se da mi više ne doðeš na oèi, jer ako mi doðeš na oèi, poginuæeš.
29 Mose anayankha kuti, “Monga momwe mwaneneramu, Ine sindidzaonekeranso pamaso panu.”
A Mojsije reèe: pravo si kazao; neæu ti više doæi na oèi.

< Eksodo 10 >