< Eksodo 1 >

1 Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
Сия имена сынов Израилевых, входящих во Египет вкупе со Иаковом отцем их, кийждо со всем домом своим внидоша:
2 Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
Рувим, Симеон, Левий, Иуда,
3 Isakara, Zebuloni, Benjamini;
Иссахар, Завулон и Вениамин,
4 Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
Дан и Неффалим, Гад и Асир: Иосиф же бяше во Египте.
5 Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
Бяше же всех душ изшедших из Иакова седмьдесят пять.
6 Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
Умре же Иосиф, и вся братия его, и весь род оный:
7 Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
сынове же Израилевы возрастоша и умножишася, и мнози быша и укрепишася зело зело: умножи же их земля.
8 Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
Воста же царь ин во Египте, иже не знаше Иосифа,
9 Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
рече же языку своему: се, род сынов Израилевых великое множество и укрепляется паче нас:
10 Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
приидите убо, прехитрим их, да не когда умножатся: и егда аще приключится нам брань, приложатся и сии к супостатом, и одолевше нам изыдут из земли (нашея).
11 Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
И пристави над ними приставники дел, да озлобят их в делех. И создаша грады тверды фараону: Пифо, и Рамесси, и он, иже есть Илиополь.
12 Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
По елику же их смиряху, толико множайшии бываху и укрепляхуся зело зело. И гнушахуся Египтяне сынми Израилевыми,
13 ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
и насилие творяху Египтяне сыном Израилевым нуждею,
14 Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
и болезненну тем жизнь творяху в делех жестоких брением и плинфоделанием, и всеми делы, яже в полях, во всех делех, имиже порабощаху их с нуждею.
15 Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
И рече царь Египетский бабам Еврейским: единей их имя Сепфора и имя вторей Фуа,
16 “Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
и рече (им): егда бабите Евреаныням, и суть к рождению, аще убо мужеский пол будет, убивайте его: аще же женский, снабдевайте его.
17 Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
Убояшася же бабы Бога, и не сотвориша, якоже повеле им царь Египетский, и живляху мужеский пол.
18 Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
Призва же царь Египетский бабы и рече им: что яко сотвористе вещь сию, и оживляете мужеский пол?
19 Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
Рекоша же бабы фараону: не яко жены Египтяныни, тако и жены Евреаныни: раждают бо прежде неже внити к ним бабам, и раждаху.
20 Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
Благо же творяше Бог бабам, и множахуся людие и укрепляхуся зело.
21 Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
И понеже бояхуся бабы Бога, сотвориша себе жилища.
22 Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”
Заповеда же фараон всем людем своим, глаголя: всяк мужеский пол, иже родится Евреом, в реку ввергайте, и всяк женский пол снабдевайте и жив.

< Eksodo 1 >