< Estere 8 >

1 Tsiku lomwelo mfumu Ahasiwero anamupatsa mfumukazi Estere nyumba ya Hamani, mdani wa Ayuda. Ndipo Mordekai anafika pamaso pa mfumu, popeza Estere anamuwuza ubale wawo.
Istoga dana dade car Asvir carici Jestiri kuæu Amana neprijatelja Judejskoga. A Mardohej izide pred cara, jer Jestira kaza šta joj je on;
2 Mfumu inavula mphete yake yodindira imene analanda kwa Hamani ndipo Estere anamusankha Mordekai kukhala woyangʼanira nyumba ya Hamani.
I car snimiv prsten svoj, koji bješe uzeo od Amana, dade ga Mardoheju; a Jestira postavi Mardoheja nad kuæom Amanovom.
3 Estere anayankhulanso ndi mfumu ndipo anadzigwetsa pa mapazi ake. Uku akulira iye anapempha mfumu kuti iletse choyipa, makamaka chiwembu chimene Hamani Mwagagi anakonza kuti awononge a Yuda.
Potom Jestira opet govori caru i padnuvši pred noge njegove i plaèuæi moljaše ga da ukloni zloæu Amana Agageja i misao njegovu koju bješe smislio na Judejce.
4 Ndipo mfumu inamuloza Estere ndi ndodo yake yagolide ndipo Estere anadzuka ndi kuyima pamaso pake.
Tada car pruži zlatnu palicu prema Jestiri, i Jestira usta i stade pred carem,
5 Iye anati, “Ngati chikomera mfumu ndi kukukondweretsani, ngati pempho langa muliona kuti ndi loyenera ndi kuti mukondwera nane tsono mfumu ilole kuti lamulo lilembedwe kusintha mawu a mʼmakalata amene Hamani mwana wa Hamedata, Mwagagi, anatumiza ku zigawo zonse za mfumu. Paja Hamani analemba kuti Ayuda onse awonongedwe.
I reèe: ako je ugodno caru i ako sam našla milost pred njim, i ako je pravo pred carem i ako sam mu mila, neka se piše da se poreku knjige u kojima je misao Amana sina Amedatina, Agageja, koje je raspisao da se istrijebe Judejci što su po svijem zemljama carevijem.
6 Kodi ndingapirire bwanji pamene ndi kuona tsoka likugwera anthu a mtundu wanga? Ndingapirire bwanji pamene abale anga akuwonongedwa?”
Jer kako bih mogla gledati zlo koje bi zadesilo moj narod? i kako bih mogla gledati da se potre rod moj?
7 Mfumu Ahasiwero anamuyankha mfumukazi Estere ndi Mordekai Myuda kuti, “Ndapereka nyumba ya Hamani kwa Estere ndipo Hamaniyo amupachika kale pa mtanda chifukwa anafuna kuwononga Ayuda.
A car Asvir reèe carici Jestiri i Mardoheju Judejcu: eto, dao sam kuæu Amanovu Jestiri a njega su objesili na vješala zato što šæaše dignuti ruku svoju na Judejce.
8 Tsono inu awiri, lembani za Ayudawo monga mufunira. Mulembe mʼdzina la mfumu ndipo musindikize chizindikiro cha mphete ya mfumu popeza kuti cholembedwa mʼdzina la mfumu ndi kusindikizidwa ndi chizindikiro cha mphete ya mfumu sichingasinthidwe.”
Vi dakle pišite za Judejce kako vam je drago u ime carevo i zapeèatite prstenom carevijem; jer što se piše u ime carevo i zapeèati prstenom carevijem ne može se poreæi.
9 Nthawi yomweyo, pa tsiku la 23 la mwezi wachitatu wa Sivani, mfumu inayitana alembi ake. Analemba zonse zokhudza Ayuda monga ananenera Mordekai. Analembera akazembe, abwanamkubwa ndi nduna za zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi. Zimene analamula Mordekai zinalembedwa mʼzilembo za chigawo chilichonse ndi chiyankhulo cha mtundu uliwonse wa anthu. Ayudanso anawalembera mʼmalemba awo ndi chiyankhulo chawo.
I dozvaše pisare careve u isto vrijeme, treæega mjeseca, koje je mjesec Sivan, dvadeset treæega dana, i pisa se sve, kako zapovjedi Mardohej, Judejcima i namjesnicima i knezovima i upraviteljima po zemljama, od Indije do Etiopije, sto i dvadeset i sedam zemalja, u svaku zemlju njezinijem pismom i svakom narodu njegovijem jezikom, i Judejcima njihovijem pismom i njihovijem jezikom.
10 Mordekai analemba makalatawo mʼdzina la mfumu Ahasiwero, nawadinda ndi chizindikiro cha mphete ya mfumu. Ndipo anawatumiza ndi anthu amithenga amene anakwera pa akavalo a ufumu othamanga kwambiri obadwa mu khola la ufumu.
A napisa u ime cara Asvira i zapeèati prstenom carevijem, i razasla knjige po glasnicima koji jahahu na brzijem konjma i na mladijem mazgama:
11 Mʼmakalata amenewa mfumu inalola kuti Ayuda okhala mu mzinda uliwonse akhale ndi ufulu wokumana ndi kudzitchinjiriza komanso kuwononga, kupha ndi kufafaniziratu gulu lililonse la nkhondo la anthu a mtundu uliwonse kapena chigawo chimene chingawathire nkhondo. Ayudawo analoledwa kuwononga gulu lankhondo lija, ana awo ndi akazi awo komanso kuti afunkhe katundu wawo.
Da je car dopustio Judejcima što su u kome god gradu da se skupe i brane život svoj, da potru i pobiju i istrijebe svaku vojsku kojega mu drago naroda i zemlje, koji bi udarili na njih, i djecu njihovu i žene njihove, a imanje njihovo da razgrabe.
12 Ayuda analoledwa kuchita zimenezi mʼzigawo zonse za Mfumu Ahasiwero pa tsiku limodzi lokha la 13 la mwezi wa 12, mwezi wa Adara.
U isti dan po svijem zemljama cara Asvira, trinaestoga dana mjeseca dvanaestoga, koje je mjesec Adar.
13 Mawu a mʼmakalatawo anayenera kudziwitsidwa kwa anthu a mtundu uliwonse mu chigawo chilichonse kuti ndi lamulo ndithu kwa anthu a mtundu uliwonse ndi kuti Ayuda adzakhale okonzeka pa tsikulo kulipsira kwa adani awo.
U knjigama se govoraše da se oglasi zapovijest po svijem zemljama i da se objavi svijem narodima da Judejci budu gotovi za onaj dan da se osvete svojim neprijateljima.
14 Atawalamulira a mfumu, amithenga aja anapita nawo makalata mwachangu, atakwera pa akavalo a mfumu. Ndipo lamulolo analiperekanso ku likulu la mzinda wa Susa.
Glasnici koji jahahu na brzijem konjma i mazgama otidoše brzo i hitno po zapovijesti carevoj; i zapovijest bi oglašena u Susanu carskom gradu.
15 Mordekai anachoka pamaso pa mfumu atavala zovala zaufumu zooneka ngati mtambo ndi zofewa zoyera, chipewa chachikulu cha golide ndi mkanjo wapepo. Ndipo mzinda wa Susa unafuwula mokondwa.
A Mardohej otide od cara u carskom odijelu ljubièastom i bijelom i pod zlatnijem vijencem velikim i u plaštu od tankoga platna i skerleta, i grad Susan radovaše se i veseljaše se.
16 Kwa Ayuda inali nthawi ya nkhope zowala ndi za chimwemwe, chikondwerero ndi ulemu.
Judejcima doðe svjetlost i veselje i radost i slava.
17 Mʼchigawo chilichonse ndi mu mzinda uliwonse, kumene mawu a mfumu onena za lamulo lake anafika, kunali chimwemwe ndi chikondwerero pakati pa Ayuda. Linali tsiku la phwando ndi chikondwerero. Ndipo anthu ambiri a mitundu ina anazitcha Ayuda chifukwa anachita mantha ndi Ayudawo.
I u svakoj zemlji i u svakom gradu, gdje god doðe zapovijest careva i naredba njegova, bješe radost i veselje meðu Judejcima, gozba i blagi dani, i mnogi iz naroda zemaljskih postajahu Judejci, jer ih popade strah od Jevreja.

< Estere 8 >