< Estere 3 >

1 Zitachitika izi, mfumu Ahasiwero anamukweza Hamani mwana wa Hamedata Mwagagi, anamulemekeza ndikumupatsa mpando wa ulemu kuposa nduna zina zonse.
Aftir these thingis kyng Assuerus enhaunside Aaman, the sone of Amadathi, that was of the kynrede of Agag, and settide his trone aboue alle the princes whiche he hadde.
2 Atumiki onse a mfumu amene anali pa chipata cha nyumba ya mfumu ankagwadira ndi kuweramira Hamani monga mwa lamulo la mfumu. Koma Mordekai sankamugwadira kapena kumuweramira.
And alle the seruauntis of the kyng, that lyuyden in the yatis of the paleis, kneliden, and worschipiden Aaman; for the emperour hadde comaundid so to hem; Mardochee aloone bowide not the knees, nethir worschipide hym.
3 Kenaka atumiki a mfumu amene anali pa chipata anafunsa Mordekai kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani sumvera lamulo la mfumu?”
`To whom the children of the kyng seiden, that saten bifore at the yatis of the paleis, Whi kepist `thou not the comaundementis of the kyng, othere wise than othere men?
4 Tsiku ndi tsiku ankayankhula naye koma iye sanamverebe. Choncho anamuwuza Hamani kuti aone ngati angavomereze khalidwe lotere la Mordekai, popeza anawawuza kuti anali Myuda.
And whanne thei seiden ful ofte these thingis, and he nolde here, thei tolden to Aaman, `and wolden wite, whether he contynuede in sentence; for he hadde seid to hem, that he was a Jew.
5 Hamani ataona kuti Mordekai sankamugwadira kapena kumuweramira, anapsa mtima kwambiri.
And whanne Aaman hadde herd this thing, and hadde preued `bi experience, that Mardochee bowide not the kne to hym, nethir worschipide hym, he was ful wrooth,
6 Hamani atamva kuti Mordekai anali Myuda, anatsimikiza kuti ndi kosakwanira kulanga Mordekai yekha. Mʼmalo mwake anapeza njira yowonongera Ayuda onse okhala mʼdziko lonse limene mfumu Ahasiwero ankalamulira.
and he ledde for nouyt to sette hise hondis on Mardochee aloone; for he hadde herd, that Mardochee was of the folc of Jewis, and more he wolde leese al the nacioun of Jewis, that weren in the rewme of Assuerus.
7 Mwezi woyamba, umene ndi mwezi wa Nisani, chaka cha khumi ndi chiwiri cha ufumu wa Ahasiwero anachita maere, otchedwa Purimu pamaso pa Hamani kuti apeze tsiku ndi mwezi woyenera. Ndipo maere anagwera pa mwezi wa khumi ndi chiwiri ndiwo mwezi wa Adara.
In the firste monethe, whos nam is Nysan, in the tweluethe yeer of the rewme of Assuerus, lot was sent in to a vessel, which lot is seid in Ebrew phur, `bifor Aaman, in what dai and in what monethe the folk of Jewis ouyte to be slayn; and the tweluethe monethe yede out, which is clepid Adar.
8 Kenaka Hamani anakawuza mfumu Ahasiwero kuti, “Pali mtundu wina wa anthu umene unabalalika ndipo wamwazikana pa mitundu ina mʼzigawo zonse za ufumu wanu umene miyambo yawo ndi yosiyana ndi ya anthu ena onse ndiponso amene safuna kumvera malamulo a mfumu, kotero si chinthu cha phindu kuti mfumu iwalekerere anthu otere.
And Aaman seide to the king Assuerus, A puple is scaterid bi alle the prouynces of thi rewme, and is departid fro it silf togidere, and vsith newe lawis and cerymonyes, and ferthermore it dispisith also the comaundementis of the kyng; and thou knowest best, that it spedith not to thi rewme, `that it encreesse in malice bi licence.
9 Ngati chingakukomereni mfumu, ikani lamulo kuti tiwawononge, ndipo ndidzalipira matalente 10,000 asiliva mosungiramo chuma cha mfumu za anthu amene adzachite ntchito imeneyi.”
If it plesith thee, `deme thou that it perisch, and Y schal paie ten thousynde of talentis to the keperis of thi tresour.
10 Choncho mfumu inavula mphete yodindira ku chala chake ndi kumupatsa Hamani mwana wa Hamedata Mwagagi, mdani wa Ayuda.
Therfor the kyng took `fro his hond the ryng which he vside, and yaf it to Aaman, the sone of Amadathi, of the kynrede of Agag, to the enemy of Jewis.
11 Mfumu inati kwa Hamani, “Sunga ndalamazo, ndipo uchite ndi anthuwo monga ufunira.”
And the kyng seide to hym, The siluer, which thou bihiytist, be thin; do thou of the puple that, that plesith thee.
12 Alembi analemba zonse zimene Hamani analamula mʼmakalata opita kwa akazembe a mfumu, abwanamkubwa a zigawo zonse ndi kwa oyangʼanira mtundu uliwonse wa anthu. Kalatazo zinali za mʼchiyankhulo cha mtundu uliwonse ndipo zinalembedwa mʼdzina la Mfumu Ahasiwero ndi kusindikizidwa ndi mphete yake.
And the scryuens of the kyng weren clepid in the firste monethe Nysan, in the threttenthe dai of the same monethe; and it was writun, as Aaman hadde comaundid, to alle prynces of the kyng, and to domesmen of prouynces and of dyuerse folkis, that ech folk myyte rede and here, `for dyuersite of langagis, bi the name of kyng Assuerus. And lettris aseelid with
13 Makalatawa anawatumiza amithenga ku zigawo zonse za mfumu kuti awononge, aphe ndi kufafaniziratu a Yuda onse, anyamata, anthu okalamba, ana ndi amayi, pa tsiku limodzi la 13 la mwezi wa Adara ndipo alande katundu wawo.
the ring of the kyng weren sent bi the corouris of the kyng to alle hise prouynces, that thei schulden sle, and `do awei alle Jewis, fro a child to an eld man, litle children and wymmen, in o dai, that is, in the thrittenthe dai of the tweluethe monethe, which is clepid Adar; and that thei schulden take awei the goodis of Jewis.
14 Mwachidule kalatayi inanena kuti mawu olembedwamowo anayenera kuperekedwa ngati lamulo mʼchigawo chilichonse ndi kuti anthu a mtundu uliwonse adziwe ndi kukhala okonzeka pa tsikulo.
Forsothe the sentence `in schort of the pistlis was this, that alle prouyncis schulden wite, and make hem redi to the forseid dai.
15 Potsata lamulo la mfumu, amithenga aja anapita mwachangu ndipo lamuloli linaperekedwanso ku Susa, likulu la dziko. Mfumu ndi Hamani anakhala pansi ndikumamwa, koma mzinda onse wa Susa unasokonezeka.
And the coroures, that weren sent, hastiden to fille the comaundement of the kyng; and anoon the comaundement hangide in Susa, `while the kyng and Aaman maden feeste, and `the while that alle Jewis wepten, that weren in the citee.

< Estere 3 >