< Aefeso 3 >

1 Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.
For this cause, I Paul, the prisoner of Christ Jesus for you the nations,
2 Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu,
if, indeed, you heard of the dispensation of the grace of God that was given to me in regard to you,
3 ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule.
that by revelation He made known to me the secret, according as I wrote before in few [words]—
4 Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu,
in regard to which you are able, reading [it], to understand my knowledge in the secret of the Christ,
5 chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri.
which in other generations was not made known to the sons of men, as it was now revealed to His holy apostles and prophets in the Spirit—
6 Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.
that the nations are fellow-heirs, and of the same body, and partakers of His promise in the Christ, through the good news,
7 Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu.
of which I became a servant, according to the gift of the grace of God that was given to me, according to the working of His power;
8 Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu.
to me—the less than the least of all the holy ones—was given this grace, among the nations to proclaim good news—the untraceable riches of the Christ,
9 Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. (aiōn g165)
and to cause all to see what [is] the fellowship of the secret that has been hid from the ages in God, who created all things by Jesus Christ, (aiōn g165)
10 Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu.
that there might be made known now to the principalities and the authorities in the heavenly [places], through the Assembly, the manifold wisdom of God,
11 Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōn g165)
according to a purpose of the ages, which He made in Christ Jesus our Lord, (aiōn g165)
12 Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima.
in whom we have the freedom and the access in confidence through the faith of Him,
13 Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.
for this reason, I ask [you] not to faint in my tribulations for you, which is your glory.
14 Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate,
For this cause I bow my knees to the Father of our Lord Jesus Christ,
15 amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo.
of whom the whole family in the heavens and on earth is named,
16 Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake,
that He may give to you, according to the riches of His glory, to be strengthened through His Spirit with might, in regard to the inner man,
17 kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi
that the Christ may dwell through the faith in your hearts, having been rooted and founded in love,
18 kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu.
that you may be in strength to comprehend, with all the holy ones, what [is] the breadth, and length, and depth, and height,
19 Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.
to know also the love of the Christ that is exceeding the knowledge, that you may be filled—to all the fullness of God;
20 Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife,
and to Him who is able to do exceedingly [and] abundantly above all things that we ask or think, according to the power that is working in us,
21 Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
to Him [is] the glory in the Assembly in Christ Jesus, to all the generations of the age of the ages. Amen. (aiōn g165)

< Aefeso 3 >