< Mlaliki 7 >

1 Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino, ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
Bolje je ime nego dobro ulje, i dan smrtni nego dan u koji se ko rodi.
2 Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero: Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense; anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
Bolje je iæi u kuæu gdje je žalost nego iæi u kuæu gdje je gozba, jer je ondje kraj svakoga èovjeka, i ko je živ, slaže u srce svoje.
3 Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka, pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
Bolja je žalost nego smijeh, jer kad je lice neveselo, srce postaje bolje.
4 Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa, koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
Srce je mudrijeh ljudi u kuæi gdje je žalost, a srce bezumnijeh u kuæi gdje je veselje.
5 Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
Bolje je slušati karanje mudroga nego da ko sluša pjesmu bezumnijeh.
6 Kuseka kwa zitsiru kuli ngati kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika, izinso ndi zopandapake.
Jer kao što prašti trnje pod loncem, taki je smijeh bezumnikov; i to je taština.
7 Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru, ndipo chiphuphu chimawononga mtima.
Nasilje obezumljuje mudroga, i poklon izopaèuje srce.
8 Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake, ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
Bolji je kraj stvari nego poèetak joj; bolji je ko je strpljiva duha negoli ko je ponosita duha.
9 Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako, pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.
Ne budi nagao u duhu svom na gnjev, jer gnjev poèiva u njedrima bezumnijeh.
10 Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?” pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.
Ne govori: šta je to, te su preðašnji dani bili bolji od ovijeh? jer ne bi bilo mudro da za to pitaš.
11 Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
Dobra je mudrost s imanjem, i korisna je onima koji vide sunce.
12 Nzeru ndi chitetezo, monganso ndalama zili chitetezo, koma phindu la chidziwitso ndi ili: kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.
Jer je mudrost zaklon, i novci su zaklon; ali je pretežnije znanje mudrosti tijem što daje život onome ko je ima.
13 Taganizirani zimene Mulungu wazichita: ndani angathe kuwongola chinthu chimene Iye anachipanga chokhota?
Pogledaj djelo Božije; jer ko može ispraviti što on iskrivi?
14 Pamene zinthu zili bwino, sangalala; koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino: Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo, ndiponso nthawi imene si yabwinoyo. Choncho munthu sangathe kuzindikira chilichonse cha mʼtsogolo mwake.
U dobro vrijeme uživaj dobro, a u zlo vrijeme gledaj, jer je Bog stvorio jedno prema drugom zato da èovjek ne zna šta æe biti.
15 Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi: munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake, ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
Svašta vidjeh za vremena taštine svoje: pravednika koji propada u pravdi svojoj, i bezbožnika koji dugo živi u svojoj zloæi.
16 Usakhale wolungama kwambiri kapena wanzeru kwambiri, udziwonongerenji wekha?
Ne budi suviše pravedan ni suviše mudar; zašto bi sebe upropastio?
17 Usakhale woyipa kwambiri, ndipo usakhale chitsiru, uferenji nthawi yako isanakwane?
Ne budi suviše bezbožan ni lud; zašto bi umro prije vremena?
18 Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi, ndipo usataye njira inayo. Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.
Dobro je da držiš jedno a drugo da ne puštaš iz ruke; jer ko se boji Boga izbaviæe se od svega.
19 Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru kupambana olamulira khumi a mu mzinda.
Mudrost krijepi èovjeka više nego deset knezova koji su u gradu.
20 Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.
Doista nema èovjeka pravedna na zemlji koji tvori dobro i ne griješi.
21 Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula, mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
Ne uzimaj na um svašta što se govori, ako bi i slugu svojega èuo gdje te psuje;
22 pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.
Jer srce tvoje zna da si i ti više puta psovao druge.
23 Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati, “Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,” koma nzeruyo inanditalikira.
Sve to ogledah mudrošæu i rekoh: biæu mudar; ali mudrost bješe daleko od mene.
24 Nzeru zimene zilipo, zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri, ndani angathe kuzidziwa?
Što je tako daleko i vrlo duboko, ko æe naæi?
25 Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe, ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru ndiponso kupusa kwake kwa misala.
Okretoh se srcem svojim da poznam i izvidim i iznaðem mudrost i razum, i da poznam bezbožnost ludosti i ludost bezumlja.
26 Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa, mkazi amene ali ngati khoka, amene mtima wake uli ngati khwekhwe, ndipo manja ake ali ngati maunyolo. Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo, koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.
I naðoh da je grèa od smrti žena kojoj je srce mreža i pruglo, kojoj su ruke okovi; ko je mio Bogu, saèuvaæe se od nje, a grješnika æe uhvatiti ona.
27 Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi: “Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
Gle, to naðoh, veli propovjednik, jedno prema drugom, tražeæi da razumijem.
28 pamene ine ndinali kufufuzabe koma osapeza kanthu, ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000, koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
Još traži duša moja, ali ne naðoh. Èovjeka jednoga u tisuæi naðoh, ali žene meðu svjema ne naðoh.
29 Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi: Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama, koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”
Samo, gle, ovo naðoh: da je Bog stvorio èovjeka dobra; a oni traže svakojake pomisli.

< Mlaliki 7 >