< Mlaliki 12 >

1 Uzikumbukira mlengi wako masiku a unyamata wako, masiku oyipa asanafike, nthawi isanafike pamene udzanena kuti, “Izi sizikundikondweretsa.”
Ali opominji se tvorca svojega u mladosti svojoj prije nego doðu dani zli i prispiju godine, za koje æeš reæi: nijesu mi mile;
2 Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala, mwezi ndi nyenyezi zidzada. Mitambo idzabweranso mvula itagwa.
Prije nego pomrkne sunce i vidjelo i mjesec i zvijezde, i opet doðu oblaci iza dažda,
3 Nthawi imene manja ako adzanjenjemera, miyendo yako idzafowoka, pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka, ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.
Kad æe drktati stražari kuæni i pognuti se junaci, i stati mlinarice, što ih je malo, i potamnjeti koji gledaju kroz prozore,
4 Makutu ako adzatsekeka, ndipo sudzamva phokoso lakunja; sudzamvanso kusinja kwa pa mtondo kapena kulira kwa mbalame mmawa.
I kad æe se zatvoriti vrata s ulice, i oslabiti zveka od mljevenja, i kad æe se ustajati na ptièji glas i prestati sve pjevaèice,
5 Imeneyi ndiyo nthawi imene anthu amaopa kupita kumalo okwera, amaopa kuyenda mʼmisewu; Mutu umatuwa kuti mbuu, amayenda modzikoka ngati ziwala ndipo chilakolako chimatheratu. Nthawi imeneyo munthu amapita ku nyumba yake yamuyaya ndipo anthu olira maliro amayendayenda mʼmisewu.
I visokoga mjesta kad æe se bojati i strašiti se na putu, kad æe badem ucvjetati i skakavac otežati i želja proæi, jer èovjek ide u kuæu svoju vjeènu, i pokajnice æe hoditi po ulicama;
6 Kumbukira Iye chingwe cha siliva chisanaduke, kapena mbale yagolide isanasweke; mtsuko usanasweke ku kasupe, kapena mkombero usanathyoke ku chitsime.
Prije nego se prekine uže srebrno, èaša se zlatna razbije i raspe se vijedro na izvoru i slomi se toèak na studencu,
7 Iyi ndi nthawi imene thupi lidzabwerera ku dothi, kumene linachokera, mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene anawupereka.
I vrati se prah u zemlju, kako je bio, a duh se vrati k Bogu, koji ga je dao.
8 “Zopanda phindu! Zopandapake!” akutero Mlaliki. “Zonse ndi zopandapake!”
Taština nad taštinama, veli propovjednik, sve je taština.
9 Mlaliki sanali wozindikira zinthu kokha ayi, komanso ankaphunzitsa anthu. Iye ankasinkhasinkha ndi kufufuzafufuza ndi kulemba mwadongosolo miyambi yambiri.
A ne samo mudar bijaše propovjednik, nego još i narod uèaše mudrosti, i motreæi i istražujuæi složi mnogo prièa.
10 Mlaliki anafufuzafufuza kuti apeze mawu oyenera, ndipo zimene analemba zinali zolondola ndiponso zoona.
Staraše se propovjednik da naðe ugodne rijeèi, i napisa što je pravo, rijeèi istine.
11 Mawu a anthu anzeru ali ngati zisonga, zokamba zawo zimene anasonkhanitsa zili ngati misomali yokhomera, yoperekedwa ndi mʼbusa mmodzi.
Rijeèi su mudrijeh ljudi kao žalci i kao klini udareni; rijeèi onijeh koji ih složiše dao je jedan pastir.
12 Samalira mwana wanga, za kuwonjezera chilichonse pa zimenezi. Kulemba mabuku ambiri sikutha, ndipo kuphunzira kwambiri kumatopetsa thupi.
I tako, sine moj, èuvaj se onoga što je preko ovoga, jer nema kraja sastavljanju mnogih knjiga, i mnogo èitanje umor je tijelu.
13 Basi zonse zamveka; mathero a nkhaniyi ndi awa: uziopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake, pakuti umenewu ndiwo udindo wa anthu onse.
Glavno je svemu što si èuo: Boga se boj, i zapovijesti njegove drži, jer to je sve èovjeku.
14 Pakuti Mulungu adzaweruza zochita zonse, kuphatikizanso zinthu zonse zobisika, kaya zabwino kapena zoyipa.
Jer æe svako djelo Bog iznijeti na sud i svaku tajnu, bila dobra ili zla.

< Mlaliki 12 >