< Mlaliki 10 >

1 Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira, choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.
[A few] dead flies in [a bottle of] perfume cause [all] the perfume to stink. Similarly [SIM], a small amount of acting foolishly can have a greater effect than acting wisely.
2 Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino, koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.
If people think sensibly, it will lead them to do what is right; if they think foolishly, it causes them to do what is wrong.
3 Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu, zochita zake ndi zopanda nzeru ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.
Even while foolish people walk along the road, they show that they do not have good sense; they show everyone that they are not wise.
4 Ngati wolamulira akukwiyira, usachoke pa ntchito yako; kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.
Do not quit working for a ruler when he is angry with you; if you remain calm, he will [probably] stop being angry.
5 Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano, kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:
There is something [else] that I have seen here on this earth, something that rulers sometimes do that is wrong/inappropriate:
6 Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba, pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.
They appoint foolish people to have important positions, while they appoint rich [people] to have unimportant positions.
7 Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.
They allow slaves [to ride] on horses [like rich people usually do], [but] they force officials to walk [like slaves usually do].
8 Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha; amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.
[It is possible that] those who dig pits will fall into one of those pits. [It is possible that] someone who tears down a wall will be bitten by a snake [that is in that wall].
9 Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo; amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.
If you work in a quarry, [it is possible that] a stone [will fall on you and] injure you. [It is possible that] men who split logs will be injured by one of those logs.
10 Ngati nkhwangwa ili yobuntha yosanoledwa, pamafunika mphamvu zambiri potema, koma luso limabweretsa chipambano.
If your axe is not sharp [DOU], you will need to work harder [to cut down a tree], but by being wise, you will succeed.
11 Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka ngati njokayo yakuluma kale.
If a snake bites a man before he charms/tames it, his ability to charm snakes will not benefit him.
12 Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa, koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
Wise people say [MTY] what is sensible, and because of that, people honor them; but foolish people are destroyed by what they say [MTY].
13 Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa; potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala
When foolish people start to talk, they say things that are foolish, and they end by saying things that are both wicked and foolish.
14 ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu. Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?
They talk (too much/without ceasing). None of us knows what will happen in the future, or what will happen after we die.
15 Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa; ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.
Foolish people become [so] exhausted by the work that they do that they are unable to find the road to their town/homes.
16 Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana, ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.
Terrible things will happen to the people of a nation whose ruler is a foolish young man, and whose [other] leaders continually eat, all day long, every day.
17 Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake, kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.
[But] a nation will prosper if its ruler is from a (noble/well-educated) family, and if its [other] leaders feast [only] at the proper times, and [if they eat and drink only] to be strong, not to become drunk.
18 Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka; ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.
Some men are very lazy [and do not repair the rafters], with the result that the rafters sag [and collapse]; and if they do not repair the roof, water will leak into the house [when it rains].
19 Phwando ndi lokondweretsa anthu, ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo, koma ndalama ndi yankho la chilichonse.
Eating food and drinking wine causes us to laugh and be happy, [but] we are able to enjoy those things only if we have money [to buy them].
20 Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako, kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako, pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako nʼkukafotokoza zomwe wanena.
Do not even think about cursing the king, or cursing rich [people, even] when you are [alone] in your bedroom, because [it is possible that] a little bird will hear [what you are saying], [and] tell those people what you said [about them].

< Mlaliki 10 >