< Deuteronomo 8 >

1 Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu.
Držite i tvorite sve zapovijesti koje vam ja zapovijedam danas, da biste živi bili i umnožili se, i da biste ušli u zemlju za koju se Gospod zakleo ocima vašim, i da biste je naslijedili.
2 Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi.
I opominji se svega puta kojim te je vodio Gospod Bog tvoj èetrdeset godina po pustinji, da bi te namuèio i iskušao, da se zna šta ti je u srcu, hoæeš li držati zapovijesti njegove ili neæeš.
3 Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova.
I muèio te je, i glaðu te morio; ali te je opet hranio manom, za koju ti nijesi znao ni oci tvoji, da bi ti pokazao da èovjek ne živi o samom hljebu nego o svemu što izlazi iz usta Gospodnjih.
4 Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe.
Odijelo tvoje ne ovetša na tebi niti noga tvoja oteèe za ovijeh èetrdeset godina;
5 Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.
Zato poznaj u srcu svom da te Gospod Bog tvoj gaji kao što èovjek gaji svoje dijete.
6 Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye.
I drži zapovijesti Gospoda Boga svojega hodeæi putovima njegovijem i bojeæi se njega.
7 Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri,
Jer Gospod Bog tvoj uvešæe te sada u dobru zemlju, u zemlju u kojoj ima dosta potoka i izvora i jezera, što izviru po dolinama i po brdima;
8 dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi;
U zemlju izobilnu pšenicom i jeèmom i vinovom lozom i smokvama i šipcima, zemlju izobilnu maslinom, od koje biva ulje, i medom;
9 dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.
U zemlju, gdje neæeš sirotinjski jesti hljeba, gdje ti neæe ništa nedostajati; u zemlju, gdje je kamenje gvožðe i gdje æeš iz brda njezinijeh sjeæi mjed.
10 Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani.
Ješæeš i biæeš sit, pa blagosiljaj Gospoda Boga svojega za dobru zemlju koju ti da.
11 Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero,
I èuvaj se da ne zaboraviš Gospoda Boga svojega bacivši u nemar zapovijesti njegove i zakone njegove i uredbe njegove, koje ti ja zapovijedam danas.
12 kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo,
I kad uzjedeš i nasitiš se, i dobre kuæe naèiniš i u njima staneš živjeti,
13 ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka,
I kad se goveda tvoja i ovce tvoje naplode, i kad ti se namnoži srebro i zlato, i što god imaš kad ti se namnoži,
14 mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo.
Nemoj da se ponese srce tvoje i zaboraviš Gospoda Boga svojega, koji te je izveo iz zemlje Misirske, iz kuæe ropske;
15 Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma.
Koji te je vodio preko one pustinje velike i strašne gdje žive zmije vatrene i skorpije, gdje je suša a nema vode; koji ti je izveo vodu iz tvrdoga kamena;
16 Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino.
Koji te je hranio u pustinji manom, za koju ne znaše oci tvoji, da bi te namuèio i iskušao te, i najposlije da bi ti dobro uèinio.
17 Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.”
Niti govori u srcu svojem: moja snaga, i sila moje ruke dobavila mi je ovo blago.
18 Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.
Nego se opominji Gospoda Boga svojega; jer ti on daje snagu da dobavljaš blago, da bi potvrdio zavjet svoj, za koji se zakleo ocima tvojim, kao što se vidi danas.
19 Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu.
Ako li zaboraviš Gospoda Boga svojega, i poðeš za drugim bogovima i njima staneš služiti i klanjati se, svjedoèim vam danas da æete zacijelo propasti,
20 Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.
Propašæete kao narodi koje Gospod potire ispred vas, jer ne poslušaste glasa Gospoda Boga svojega.

< Deuteronomo 8 >