< Deuteronomo 33 >

1 Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe.
A to jest błogosławieństwo, którym Mojżesz, mąż Boży, pobłogosławił synów Izraela przed swoją śmiercią.
2 Iye anati: “Yehova anabwera kuchokera ku Sinai ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri; anawala kuchokera pa Phiri la Parani. Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.
Powiedział: PAN przyszedł z Synaju i z Seiru wzeszedł dla nich, zajaśniał z góry Paran i przyszedł z dziesięcioma tysiącami świętych; z jego prawicy [wyszło] dla nich ogniste prawo.
3 Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu; opatulika ake onse ali mʼmanja mwake. Onse amagwada pansi pa mapazi anu kuchokera kwa inu amalandira malangizo,
Doprawdy, on umiłował lud; wszyscy jego święci są w twych rękach i oni usiedli u twoich stóp; przyjmują twoje słowa.
4 malamulo amene Mose anatipatsa, chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.
Mojżesz dał nam prawo, dziedzictwo zgromadzenia Jakuba.
5 Iye anali mfumu ya Yesuruni pamene atsogoleri a anthu anasonkhana, pamodzi ndi mafuko a Israeli.
I był królem w Jeszurunie, gdy się zebrali naczelnicy ludu wraz z pokoleniami Izraela.
6 “Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe, anthu ake asachepe pa chiwerengero.”
Niech żyje Ruben i niech nie umiera; niech jego mężczyzn będzie dużo.
7 Ndipo ponena za Yuda anati: “Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda; mubweretseni kwa anthu ake. Ndi manja ake omwe adziteteze yekha. Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”
Potem też dał [błogosławieństwo] dla Judy i powiedział: Wysłuchaj, PANIE, głosu Judy, i przyprowadź go do jego ludu. Niech starczy mu [sił] jego rąk, a [ty] bądź mu pomocą przeciw jego wrogom.
8 Za fuko la Alevi anati: “Tumimu wanu ndi Urimu ndi za mtumiki wanu wokhulupirika. Munamuyesa ku Masa; munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.
A o Lewim powiedział: [Niech] twoje Tummim i Urim [będą] przy twoim świętym, którego doświadczyłeś w Massa, z którym spierałeś się u wód Meriba;
9 Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti, ‘Sindilabadira za iwo.’ Sanasamale za abale ake kapena ana ake, koma anayangʼanira mawu anu ndipo anateteza pangano lanu.
Który powiedział swemu ojcu i matce: Nie widziałem go; nie znał też swych braci ani nie znał swych synów. Oni bowiem przestrzegają twoich słów i zachowują twoje przymierze.
10 Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu ndi malamulo anu kwa Israeli. Amafukiza lubani pamaso panu ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.
Będą uczyć Jakuba twoich sądów, a Izraela twego prawa. Będą kłaść kadzidło przed tobą i całopalenia na twoim ołtarzu.
11 Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake. Menyani adani awo mʼchiwuno kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”
Błogosław, PANIE, jego siłę, i przyjmij dzieło jego rąk; skrusz biodra jego wrogów i tych, którzy go nienawidzą, aby już nie powstali.
12 Za fuko la Benjamini anati: “Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye, pakuti amamuteteza tsiku lonse, ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”
[A] o Beniaminie powiedział: Umiłowany przez PANA będzie mieszkał przy nim bezpiecznie; [PAN] będzie go bronił każdego dnia, a on będzie przebywał między jego ramionami.
13 Za fuko la Yosefe anati: “Yehova adalitse dziko lake ndi mame ambiri ochokera kumwamba ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;
O Józefie powiedział: Niech jego ziemia będzie błogosławiona przez PANA, z najlepszych rzeczy niebios, z rosy i z otchłani rozłożonej pod ziemią.
14 ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;
I z najcenniejszych plonów słońca, z najcenniejszych plonów księżyca;
15 ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;
I z najlepszych skarbów gór starożytnych, z najlepszych darów odwiecznych pagórków;
16 ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto. Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe, wapaderadera pakati pa abale ake.
I z najcenniejszych [owoców] ziemi i jej obfitości oraz z przychylności tego, który przebywał w krzaku. Niech to [błogosławieństwo] spłynie na głowę Józefa i na czubek głowy tego, który został oddzielony od swoich braci.
17 Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa; nyanga zake zili ngati za njati. Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina, ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi. Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu; nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”
Jego chwała jest [jak] pierworodny wół, a jego rogi jak rogi jednorożca. Nimi będzie bódł wszystkie narody aż po krańce ziemi; a są to dziesiątki tysięcy Efraima i tysiące Manassesa.
18 Za fuko la Zebuloni anati: “Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka, ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.
A o Zebulonie powiedział: Wesel się, Zebulonie, gdy wyruszasz, a [ty], Issacharze, w swoich namiotach.
19 Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri, kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo; kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja, chuma chobisika mu mchenga.”
Zwołują ludy na górę, tam będą składać ofiary sprawiedliwości. Będą bowiem ssać z obfitości morza i ze skarbów ukrytych w piasku.
20 Za fuko la Gadi anati: “Wodala amene amakulitsa malire a Gadi! Gadi amakhala kumeneko ngati mkango, kukhadzula mkono kapena mutu.
A o Gadzie powiedział: Błogosławiony ten, kto rozprzestrzeni Gada. Będzie mieszkać jak lew, a urwie ramię i głowę.
21 Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri; gawo la mtsogoleri anasungira iye. Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana, anachita chifuniro cha Yehova molungama, ndiponso malamulo onena za Israeli.”
Upatrzył sobie najlepszą [część], gdyż tam został mu wyznaczony dział przez prawodawcę; przyszedł z naczelnikami ludu i wykonał sprawiedliwość PANA i jego sądy z Izraelem.
22 Za fuko la Dani anati: “Dani ndi mwana wamkango, amene akutuluka ku Basani.”
A o Danie powiedział: Dan [to] szczenię lwie, wyskoczy z Baszanu.
23 Za fuko la Nafutali anati: “Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake; cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”
A o Neftalim powiedział: Neftali, nasycony przychylnością i pełen błogosławieństwa PANA, posiądź zachód i południe.
24 Za fuko la Aseri anati: “Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri; abale ake amukomere mtima, ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.
A o Aszerze powiedział: Aszer będzie błogosławiony dziećmi, niech się podoba swoim braciom i niech kąpie swoje nogi w oliwie.
25 Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa, ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.
Twoje obuwie będzie z żelaza i miedzi; a ile twoich dni, [taka będzie] twoja siła.
26 “Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni, amene amakwera pa thambo kukuthandizani ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.
Nikt nie jest jak Bóg Jeszuruna, który jeździ po niebie, by tobie pomóc, i po obłokach w swym majestacie.
27 Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu, ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha. Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu, adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’
Twoim schronieniem jest wieczny Bóg, a pod tobą [są] wieczne ramiona. On wypędzi przed tobą wroga i powie: Wyniszcz [go].
28 Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere; zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano, kumene thambo limagwetsa mame.
Wtedy Izrael będzie mieszkać bezpiecznie sam. Źródło Jakuba – w ziemi zboża i wina, a niebiosa spuszczą rosę.
29 Iwe Israeli, ndiwe wodala! Wofanana nanu ndani anthu opulumutsidwa ndi Yehova? Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu ndi lupanga lanu la ulemerero. Adani ako adzakugonjera, ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”
Błogosławiony jesteś, Izraelu! Któż do ciebie podobny, ludu zbawiony przez PANA, który jest tarczą twego ratunku i mieczem twego dostojeństwa! Twoi wrogowie poddadzą się tobie obłudnie, a ty zdepczesz ich wyniosłość.

< Deuteronomo 33 >