< Danieli 9 >

1 Mʼchaka choyamba cha Dariyo mwana wa Ahasiwero (wochokera kwa Amedi), amene anakhala mfumu ya ku Babuloni,
Prve godine Darija sina Asvirova od plemena Midskoga, koji se zacari nad carstvom Haldejskim,
2 ine Danieli ndinazindikira powerenga mawu a Yehova opatsidwa kwa mneneri Yeremiya, kuti Yerusalemu adzakhala bwinja kwa zaka 70.
Prve godine njegova carovanja ja Danilo razumjeh iz knjiga broj godina, koje bješe rekao Gospod Jeremiji proroku da æe se navršiti razvalinama Jerusalimskim, sedamdeset godina.
3 Choncho ndinatembenukira kwa Ambuye Mulungu ndipo ndinamudandaulira ndi kupempha posala kudya, ndi kuvala chiguduli ndi kudzola phulusa.
I okretoh lice svoje ka Gospodu Bogu tražeæi ga molitvom i molbama s postom i s kostrijeti i pepelom.
4 Ndinapemphera kwa Yehova Mulungu wanga ndi kuvomereza kuti tinachimwa: Ndinati, “Inu Ambuye, Mulungu wamkulu ndi woopsa, amene mumasunga pangano lanu la chikondi kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu,
I pomolih se Gospodu Bogu svojemu i ispovijedajuæi se rekoh: o Gospode, Bože veliki i strašni, koji držiš zavjet i milost onima koji te ljube i drže zapovijesti tvoje;
5 tachimwa ndipo tachita zolakwa ndi zoyipa. Takuwukirani posiya malangizo ndi malamulo anu.
Zgriješismo i zlo èinismo i bismo bezbožni, i odmetnusmo se i otstupismo od zapovijesti tvojih i od zakona tvojih.
6 Sitinamvere aneneri atumiki anu, amene anayankhula mʼdzina lanu kwa mafumu athu, kwa akalonga athu, makolo athu, ndi kwa anthu onse a mʼdziko.
I ne slušasmo sluga tvojih proroka, koji govorahu u tvoje ime carevima našim, knezovima našim i ocima našim i svemu narodu zemaljskom.
7 “Ambuye ndinu olungama, koma lero tili ndi manyazi, ife anthu a ku Yuda, a ku Yerusalemu ndi Israeli yense, apafupi ndi akutali omwe, ku mayiko onse kumene munatipirikitsira chifukwa cha kusakhulupirika kwathu.
U tebe je, Gospode, pravda a u nas sram na licu, kako je danas, u Judejaca i u Jerusalimljana i u svijeh Izrailjaca, koji su blizu i koji su daleko po svijem zemljama kuda si ih razagnao za grijehe njihove, kojima ti griješiše.
8 Inu Yehova, ife ndi mafumu athu, akalonga athu ndi makolo athu tili ndi manyazi chifukwa takuchimwirani.
Gospode, u nas je sram na licu, u careva naših, u knezova naših i u otaca naših, jer ti zgriješismo.
9 Ambuye Mulungu wathu ndi wachifundo ndi wokhululuka, ngakhale kuti tamuwukira:
U Gospoda je Boga našega milost i praštanje, jer se odmetnusmo od njega,
10 Ife sitinamvere Yehova Mulungu wathu kapena kusunga malamulo ake amene anatipatsa kudzera mwa aneneri atumiki ake.
I ne slušasmo glasa Gospoda Boga svojega da hodimo po zakonima njegovijem, koje nam je dao preko sluga svojih proroka.
11 Aisraeli onse anachimwira lamulo lanu motero anapatuka, nakana kukumverani. “Choncho matemberero ndi olumbira amene alembedwa mʼmalamulo a Mose, mtumiki wa Mulungu, atigwera chifukwa takuchimwirani.
I sav Izrailj prestupi zakon tvoj, i otstupi da ne sluša glasa tvojega; zato se izli na nas prokletstvo i zakletva napisana u zakonu Mojsija sluge Božijega, jer mu zgriješismo.
12 Inu mwakwaniritsa mawu amene munayankhula otitsutsa ife ndi otsutsa otilamulira potibweretsera tsoka lalikulu. Pa dziko lapansi sipanachitikenso zinthu ngati zimene zaonekera Yerusalemu.
I on potvrdi rijeèi svoje koje je govorio za nas i za sudije naše, koje su nam sudile, pustivši na nas zlo veliko, da tako ne bi pod svijem nebom kako bi u Jerusalimu.
13 Monga kunalembedwa mʼMalamulo a Mose, tsoka lililonse latifikira chikhalirecho sitinapemphe Yehova Mulungu wathu kuti atikomere mtima. Sitinasiye machimo athu, ndipo sitinasamale choonadi chanu.
Kako je pisano u zakonu Mojsijevu, sve to zlo doðe na nas, i opet se ne molismo Gospodu Bogu svojemu da bismo se vratili od bezakonja svojega i pazili na istinu tvoju.
14 Choncho Yehova anakonza kuti atigwetsere tsoka limeneli, ndipo wachitadi popeza Yehova Mulungu wathu ndi wolungama mu chilichonse amachita; chikhalirecho ife sitinamumvere.
I Gospod nasta oko zla i navede ga na nas; jer je pravedan Gospod Bog naš u svijem djelima svojim koja èini, jer ne slušasmo glasa njegova.
15 “Inu Ambuye Mulungu wathu, munatulutsa anthu anu ku Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo dzina lanu ndi lotchuka mpaka lero. Ife tachimwa, tachita zolakwa.
Ali sada, Gospode Bože naš, koji si izveo narod svoj iz zemlje Misirske rukom krjepkom, i stekao si sebi ime, kako je danas, zgriješismo, bezbožni bismo.
16 Inu Ambuye, molingana ndi zochita zanu zolungama, tikukupemphani kuti muchotse mkwiyo ndi ukali wanu pa Yerusalemu mzinda wanu, phiri lanu loyera. Machimo athu ndi mphulupulu za makolo athu zachititsa kuti onse otizungulira atonze Yerusalemu ndi anthu anu.
Gospode, po svoj pravdi tvojoj neka se odvrati gnjev tvoj i jarost tvoja od grada tvojega Jerusalima, svete gore tvoje; jer sa grijeha naših i s bezakonja otaca naših Jerusalim i tvoj narod posta rug u svijeh koji su oko nas.
17 “Tsopano Mulungu wathu, imvani mapemphero ndi zopempha za mtumiki wanu. Kuti anthu onse akudziweni kuti ndinu Ambuye, komerani mtima malo anu opatulika amene asanduka bwinja.
Sada dakle poslušaj, Bože naš, molitvu sluge svojega i molbe njegove, i obasjaj licem svojim opustjelu svetinju svoju, Gospoda radi.
18 Tcherani khutu, Inu Mulungu, ndipo imvani; tsekulani maso anu ndipo onani mabwinja athu ndi mzinda umene umadziwika ndi dzina lanu. Sitikupempha chifukwa chakuti ndife olungama, koma chifukwa cha kukula kwa chifundo chanu.
Bože moj, prigni uho svoje, i èuj; otvori oèi svoje, i vidi pustoš našu i grad, na koji je prizvano ime tvoje, jer ne pravde svoje radi nego radi velike milosti tvoje padamo pred tobom moleæi se.
19 Inu Ambuye imvani mawu athu! Ambuye khululukani! Ambuye timvereni, ndipo muchitepo kanthu! Kuti anthu adziwe kuti Inu ndinu Mulungu wanga musachedwe chifukwa mzinda wanu ndi anthu anu amadziwika ndi dzina lanu.”
Gospode, usliši, Gospode, oprosti, Gospode, pazi i uèini, ne èasi, sebe radi, Bože moj, jer je tvoje ime prizvano na ovaj grad i na tvoj narod.
20 Ndikuyankhula ndi kupemphera, kuvomereza machimo anga ndi machimo a anthu anga Aisraeli ndi kupempherera phiri lake loyera kwa Yehova Mulungu wanga,
A dok ja još govorah i moljah se i ispovijedah grijeh svoj i grijeh naroda svojega Izrailja, i padah moleæi se pred Gospodom Bogom svojim za svetu goru Boga svojega,
21 Gabrieli, munthu uja amene ndinamuona mʼmasomphenya poyambirira, anabwera kwa ine mowuluka. Iyi inali nthawi ya nsembe ya madzulo.
Dok još govorah moleæi se, onaj èovjek Gavrilo, kojega vidjeh prije u utvari, doletje brzo i dotaèe me se o veèernjoj žrtvi.
22 Anandilangiza kuti, “Danieli ndabwera tsopano kuti ndikupatse nzeru kuti uzitha kumvetsa zinthu.
I nauèi me i govori sa mnom i reèe: Danilo, sada izidoh da te urazumim.
23 Utangoyamba kupemphera, Mulungu anayankha. Tsono ine ndabwera kudzakuwuza yankholo, popeza ndiwe wokondedwa kwambiri. Choncho mvetsetsa pamene ndikufotokoza za zinthu zimene unaziona mʼmasomphenya.
U poèetku molitve tvoje izide rijeè, i ja doðoh da ti kažem, jer si mio; zato slušaj rijeè, i razumij utvaru.
24 “Zaka 490 zinayikidwa kuti anthu a mtundu wako ndi mzinda wanu woyera aleke zoyipa, asiye tchimo. Iwo adzapereka dipo kupepesera zolakwa zawo. Zikadzatero anthu adzaonetsa moyo wachilungamo nthawi zonse. Izi zidzatsimikiza zimene unaziona mʼmasomphenya zija ndi zimene ananenera aneneri. Malo opatulika adzakhazikitsidwa.
Sedamdeset je nedjelja odreðeno tvome narodu i tvome gradu svetom da se svrši prijestup i da nestane grijeha i da se oèisti bezakonje i da se dovede vjeèna pravda, i da se zapeèati utvara i proroštvo, i da se pomaže sveti nad svetima.
25 “Tsono udziwe ndipo uzindikire izi kuti kuyambira pamene lamulo linaperekedwa kuti Yerusalemu akonzedwenso mpaka pamene mfumu Yodzozedwa idzafike padzapita zaka 49. Pa zaka 434 mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso, ndipo mabwalo ndi ngalande zake zidzatetezedwa. Koma nthawiyi idzakhala ya masautso.
Zato znaj i razumij: otkad izide rijeè da se Jerusalim opet sazida do pomazanika vojvode biæe sedam nedjelja, i šezdeset i dvije nedjelje da se opet pograde ulice i zidovi, i to u teško vrijeme.
26 Patatha zaka 434, Wodzozedwayo adzaphedwa ndipo sadzakhala ndi aliyense. Anthu a wolamulira amene adzabwere adzawononga mzinda ndi Nyumba ya Mulungu. Kutha kwake kudzafika ngati chigumula. Komabe nkhondo idzapitirira mpaka chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu chitachitika.
A poslije te šezdeset i dvije nedjelje pogubljen æe biti pomazanik i ništa mu neæe ostati; narod æe vojvodin doæi i razoriti grad i svetinju; i kraj æe mu biti s potopom, i odreðeno æe pustošenje biti do svršetka rata.
27 Adzachita pangano lolimba ndi anthu ambiri kwa zaka zisanu ndi ziwiri. Koma pakatinʼpakati pa sabata limodzilo iye adzaletsa kupereka nsembe ndi chopereka. Chonyansa chosakaza chija adzachiyika mʼNyumba ya Mulungu, ndipo chidzakhalapobe mpaka wochita zimenezi atalangidwa ndi chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu.”
I utvrdiæe zavjet s mnogima za nedjelju dana, a u polovinu nedjelje ukinuæe žrtvu i prinos; i krilima mrskim, koja pustoše, do svršetka odreðenoga izliæe se na pustoš.

< Danieli 9 >