< Danieli 6 >

1 Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
It pleased Darius to appoint over the kingdom 120 provincial governors who would rule over all the kingdom.
2 ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
Over them there were three chief administrators, and Daniel was one of them. These chief administrators were appointed so that they might supervise the provincial governors, so that the king should suffer no loss.
3 Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
Daniel was distinguished above the other chief administrators and the provincial governors because he had an extraordinary spirit. The king was planning to put him over the whole kingdom.
4 Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
Then the other chief administrators and the provincial governors looked for mistakes in the work Daniel did for the kingdom, but they could find no corruption or failure in his duty because he was faithful. No mistakes or negligence was found in him.
5 Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
Then these men said, “We cannot find any reason to complain against this Daniel unless we find something against him regarding the law of his God.”
6 Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
Then these administrators and governors brought a plan before the king. They said to him, “King Darius, may you live forever!
7 Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
All the chief administrators of the kingdom, the regional governors, and the provincial governors, the advisors, and the governors have consulted together and decided that you, the king, should issue a decree and should enforce it, so that whoever makes a petition to any god or man for thirty days, except to you, king, that person must be thrown into the den of lions.
8 Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
Now, King, issue a decree and sign the document so that it may not be changed, as directed by the laws of the Medes and Persians, so it cannot be repealed.”
9 Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
So king Darius signed the document making the decree into a law.
10 Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
When Daniel learned that the document had been signed into law, he went into his house (now his windows were open in his upper room toward Jerusalem), and he got down on his knees, as he did three times a day, and prayed and gave thanks before his God, as he had done before.
11 Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
Then these men who had formed the plot together saw Daniel make requests and seek help from God.
12 Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
Then they approached the king and spoke with him about his decree: “Did you not make a decree that everyone who makes a petition to any god or human being during the next thirty days, except to you, king, must be throw into the den of lions?” The king answered, “The matter is settled, as directed by the law of the Medes and Persians; it cannot be repealed.”
13 Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
Then they replied to the king, “That person Daniel, who is one of the people of the exile from Judah, pays no attention to you, king, or to the decree that you have signed. He prays to his God three times a day.”
14 Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
When the king heard this, he was terribly distressed, and he applied his mind to rescue Daniel from this ruling. He labored until sunset to try to save Daniel.
15 Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
Then these men who had formed the plot gathered together with the king and said to him, “Know, king, that it is a law of the Medes and Persians, that no decree or statute that the king issues can be changed.”
16 Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
Then the king gave an order, and they brought in Daniel, and they threw him into the lions' den. The king said to Daniel, “May your God, whom you serve continually, rescue you.”
17 Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
A stone was brought over the entrance to the den, and the king sealed it with his own signet ring and with the signet rings of his nobles so that nothing might be changed concerning Daniel.
18 Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
Then the king went to his palace and he went through the night fasting. No entertainment was brought before him, and sleep fled from him.
19 Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
Then at daybreak the king got up and he quickly went to the lions' den.
20 Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
As he came near to the den, he called out to Daniel in a sad voice, saying to Daniel, “Daniel, servant of the living God, has your God, whom you serve continually, been able to save you from the lions?”
21 Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
Then said Daniel to the king, “King, live forever!
22 Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
My God has sent his messenger and has shut the lions' mouths, and they have not hurt me. For I was found blameless before him and also before you, king, and I have done you no harm.”
23 Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
Then the king was very happy. He gave an order that they should take Daniel up out of the den. So Daniel was lifted up out of the den. No harm was found on him, because he had trusted in his God.
24 Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
The king gave an order, and they brought those men who had accused Daniel and threw them into the den of lions—they, their children, and their wives. Before they reached the floor, the lions overpowered them and broke all their bones to pieces.
25 Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
Then King Darius wrote to all the peoples, nations, and languages that live in all the earth: “May peace increase for you.
26 “Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
I hereby make a decree that in all the dominion of my kingdom men tremble and fear before the God of Daniel, for he is the living God and lives forever, and his kingdom shall not be destroyed; his dominion shall be to the end.
27 Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
He makes us safe and rescues us, and he does signs and wonders in heaven and in earth; he has kept Daniel safe from the strength of the lions.”
28 Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.
So Daniel prospered during the reign of Darius and during the reign of Cyrus the Persian.

< Danieli 6 >