< Danieli 2 >

1 Chaka chachiwiri cha ulamuliro wake, Nebukadinezara analota maloto; anavutika mu mtima mwake ndipo analephera kugona.
A druge godine carovanja Navuhodonosorova usni Navuhodonosor san, i uznemiri mu se duh i san ga proðe.
2 Tsono mfumu inayitana amatsenga, owombeza, amawula ndi oyangʼana nyenyezi kuti amufotokozere zomwe analota. Pamene iwo analowa ndi kuyima pamaso pa mfumu,
I reèe car da dozovu vraèe i zvjezdare i gatare i Haldeje da kažu caru san njegov. I doðoše i staše pred carem.
3 mfumuyo inawawuza kuti, “Ndalota loto lomwe likundisautsa ndipo ndikufuna kudziwa tanthauzo lake.”
I reèe im car: usnih san, i uznemiri mi se duh kako bih doznao što sam snio.
4 Pamenepa alawuli anati kwa mfumu mʼChiaramu, “Mukhale ndi moyo wautali mfumu! Tiwuzeni ife atumiki anu zimene mwalota, ndipo tidzakuwuzani tanthauzo lake.”
A Haldeji rekoše caru Sirski: care, da si živ dovijeka! pripovjedi san slugama svojim, pa æemo ti kazati što znaèi.
5 Mfumu inayankha alawuliwo kuti, “Zimene ndatsimikiza kuchita ndi izi: Ngati inu simundifotokozera zimene ndalota ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli ndipo nyumba zanu ndidzazisandutsa bwinja.
A car odgovori i reèe Haldejima: zaboravio sam; ako mi ne kažete što sam snio i što znaèi, biæete isjeèeni i kuæe æe vaše biti buništa.
6 Koma ngati mundiwuza zimene ndalota ndi tanthauzo lake, ndidzakupatsani mphatso ndi mphotho ndi ulemu waukulu. Choncho mundiwuze zimene ndalota ndi tanthauzo lake.”
Ako li mi kažete što sam snio i što znaèi, dobiæete od mene dare i poklone i veliku èast; kažite mi dakle što sam snio i što znaèi.
7 Iwo anayankhanso kachiwiri kuti, “Mfumu iwuze atumiki ake chimene yalota, ndipo ife tidzatanthauzira.”
Odgovoriše opet i rekoše: neka car pripovjedi san slugama svojim, pa æemo kazati što znaèi.
8 Ndipo mfumu inayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti mukungozengereza kufuna kutaya nthawi chabe chifukwa mukuzindikira kuti izi ndi zimene ndatsimikiza kuchita.
Car odgovori i reèe: doista vidim da hoæete vremena da dobijete; jer vidite da sam zaboravio.
9 Ngati simundiwuza zimene ndalota, chilango chake ndi chimodzi. Inu mwagwirizana kuti mundiwuze ine bodza ndi chinyengo ndi kuyembekeza kuti ine ndisintha. Tsono mundiwuze zimene ndalota, ndipo ine ndidzadziwa kuti mukhoza kunditanthauzira.”
Ali ako mi ne kažete što sam snio i što znaèi, jedan vam je sud; jer ste se dogovorili da kažete preda mnom laž i prijevaru dok se promijeni vrijeme; zato kažite mi san, pa æu vidjeti da mi možete kazati što znaèi.
10 Alawuli anayankha mfumu kuti, “Palibe munthu pa dziko lapansi amene akhoza kuchita chimene mfumu ikufunsa! Palibe mfumu, kaya yayikulu kapena yamphamvu bwanji imene inafunsapo amatsenga, owombeza kapena alawuli aliwonse zimenezi.
Odgovoriše Haldeji caru i rekoše: nema èovjeka na zemlji koji bi mogao kazati caru to što ište; zato nijedan car ni knez ni vlastelin nije nigda iskao tako što od vraèa ili zvjezdara ili Haldejca.
11 Zimene mfumu yafunsa ndi zapatali. Palibe wina amene angathe kuwulula izi kwa mfumu kupatula milungu, ndipo sikhala pakati pa anthu.”
I što car ište vrlo je teško; niti ima drugoga koji bi mogao kazati caru osim bogova, koji ne žive meðu ljudima.
12 Zimenezi zinapsetsa mtima mfumu ndipo inakwiya kwambiri kotero inalamula kuti anzeru onse a ku Babuloni aphedwe.
Zato se car razljuti i razgnjevi vrlo, i zapovjedi da se pogube svi mudarci Vavilonski.
13 Choncho lamulo linaperekedwa kuti anthu anzeru aphedwe, ndipo anatuma anthu kukafunafuna Danieli ndi anzake kuti iwonso aphedwe.
I kad izide zapovijest, te ubijahu mudarce, tražahu i Danila i drugove njegove da ih ubiju.
14 Danieli anayankhula mwanzeru ndi mwaulemu kwa Ariyoki, mkulu wa asilikali olondera mfumu amene anatumidwa kukapha anthu anzeru a ku Babuloni.
Tada Danilo odgovori mudro i razumno Ariohu zapovjedniku stražarskom, koji bijaše izašao da ubija mudarce Vavilonske;
15 Danieli anafunsa Ariyoki kapitawo wa mfumu kuti, “Chifukwa chiyani mfumu yapereka lamulo lankhanza lotere?” Kenaka Ariyoki anafotokoza nkhaniyi kwa Danieli.
Odgovori i reèe Ariohu vlastelinu carevu: zašto je tako nagla zapovijest od cara? Tada Arioh kaza stvar Danilu.
16 Danieli anapita mofulumira kwa mfumu ndipo anamupempha kuti amupatse nthawi kuti amuwuze zimene walota ndi tanthauzo lake.
A Danilo otide i zamoli cara da mu ostavi vremena, pak æe kazati caru što san znaèi.
17 Kenaka Danieli anabwerera ku nyumba kwake ndi kukafotokozera anzake aja zimenezi: Hananiya, Misaeli ndi Azariya.
Potom otide Danilo kuæi svojoj, i kaza stvar Ananiji, Misailu i Azariji, drugovima svojim,
18 Danieli anadandaulira anzake kuti apemphe kwa Mulungu wakumwamba kuti awachitire chifundo ndi kumuwululira chinsinsi, kuti iye ndi anzakewo asanyongedwe pamodzi ndi anzeru ena onse a ku Babuloni.
Da se mole za milost Bogu nebeskomu radi te tajne, da ne bi poginuli Danilo i drugovi mu s ostalijem mudarcima Vavilonskim.
19 Usiku Yehova anamuwululira Danieli chinsinsi chija mʼmasomphenya. Pamenepo Danieli anatamanda Mulungu wakumwamba,
I objavi se tajna Danilu u noænoj utvari; tada Danilo blagoslovi Boga nebeskoga.
20 ndipo anati: “Litamandike dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi; nzeru ndi mphamvu zonse ndi zake.
Progovori Danilo i reèe: da je blagosloveno ime Gospodnje od vijeka do vijeka; jer je njegova mudrost i sila;
21 Amasintha nthawi ndi nyengo; amakweza mafumu ndipo amawatsitsanso. Amapatsa nzeru kwa anzeru ndi chidziwitso kwa ozindikira zinthu.
I on mijenja vremena i èase; smeæe careve, i postavlja careve; daje mudrost mudrima i razum razumnima.
22 Amavumbulutsa zinthu zozama ndi zobisika; amadziwa zimene zili mu mdima, ndipo kuwunika kumakhala ndi Iye.
On otkriva što je duboko i sakriveno, zna što je u mraku, i svjetlost kod njega stanuje.
23 Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga: mwandipatsa nzeru ndi mphamvu, mwandiwululira zomwe tinakupemphani, mwatiwululira maloto a mfumu.”
Tebe, Bože otaca mojih, hvalim i slavim, što si mi dao mudrost i silu, i što si mi objavio za što te molismo objaviv nam stvar carevu.
24 Motero Danieli anapita kwa Ariyoki, amene mfumu inamusankha kuti akaphe anthu anzeru a ku Babuloni, ndipo anati kwa iye, “Musaphe anthu anzeru a ku Babuloni. Ndiperekezeni kwa mfumu, ndipo ndidzayimasulira maloto ake.”
Tada otide Danilo k Ariohu, kojega car bješe odredio da pogubi mudarce Vavilonske; i došav ovako mu reèe: ne gubi mudaraca Vavilonskih; izvedi me pred cara da kažem caru što san znaèi.
25 Ariyoki anapita naye Danieli kwa mfumu nthawi yomweyo ndipo anati, “Ndapeza munthu pakati pa akapolo ochokera ku Yuda amene akhoza kuwuza mfumu zimene maloto ake akutanthauza.”
Tada Arioh brže izvede Danila pred cara, i ovako mu reèe: naðoh èovjeka izmeðu roblja Judina, koji æe kazati caru što san znaèi.
26 Mfumu inafunsa Danieli (wotchedwanso Belitesezara) kuti, “Kodi ukhoza kundiwuza zomwe ine ndinaona mʼmaloto anga ndi tanthauzo lake?”
A car progovori i reèe Danilu, koji se zvaše Valtasar: možeš li mi kazati san koji sam snio i što znaèi?
27 Danieli anayankha kuti, “Palibe munthu wanzeru, wowombeza, wamatsenga kapena wamawula amene akhoza kufotokozera mfumu chinsinsi chimene mwafuna kudziwa,
Odgovori Danilo caru i reèe: tajne koje car ište ne mogu kazati caru mudarci ni zvjezdari ni vraèi ni gatari.
28 koma kuli Mulungu kumwamba amene amawulula zinsinsi. Iye waonetsera mfumu Nebukadinezara zimene zidzachitika mʼmasiku akutsogolo. Maloto ndi masomphenya anu amene munawaona mukugona pa bedi lanu ndi awa:
Nego ima Bog na nebu koji otkriva tajne i javlja caru Navuhodonosoru što æe biti do pošljetka. San tvoj i što ti je vidjela glava na postelji tvojoj ovo je:
29 “Mukugona pa bedi, inu Mfumu, maganizo anakufikirani a zinthu zakutsogolo, ndipo Yehova wowulula zinsinsi anakuonetserani zimene zidzachitika.
Tebi, care, doðoše misli na postelji što æe biti poslije, i onaj koji objavljuje tajne pokaza ti što æe biti.
30 Koma chinsinsi ichi chavumbulutsidwa kwa ine, si chifukwa chakuti ndili ndi nzeru zochuluka kuposa anthu ena onse, koma kuti mfumu mudziwe tanthauzo la maloto anu ndi kuti muzindikire maganizo amene anali mu mtima mwanu.
A meni se ova tajna nije objavila mudrošæu koja bi u mene bila mimo sve žive, nego zato da se javi caru što san znaèi i da doznaš misli srca svojega.
31 “Inu mfumu, munaona chinthu chowumba chachikulu chimene chinayima pamaso panu. Chowumbachi chinali chonyezimira mʼmaonekedwe.
Ti, care, vidje a to lik velik; velik bijaše lik i svjetlost mu silna, i stajaše prema tebi, i strašan bijaše na oèima.
32 Mutu wa chowumbacho unali wagolide wabwino kwambiri. Chifuwa ndi manja ake zinali zasiliva. Mimba ndi ntchafu zake zinali zamkuwa.
Glava tome liku bijaše od èistoga zlata, prsi i mišice od srebra, trbuh i bedra od mjedi,
33 Miyendo yake inali yachitsulo, mapazi ake anali achitsulo chosakaniza ndi dongo.
Golijeni mu od gvožða, a stopala koje od gvožða koje od zemlje.
34 Inu mukuona, mwala unagamuka, koma osati ndi manja a munthu. Unagwera fanolo pa mapazi ake achitsulo chosakaniza ndi dongo aja ndi kuwaphwanya.
Ti gledaše dokle se odvali kamen bez ruku, i udari lik u stopala mjedena i zemljana, i satr ih.
35 Tsono chitsulo, dongo, mkuwa, siliva ndi golide zonse zinaphwanyika pamodzi ndikukhala tizidutswa towuluka ndi mphepo ngati mungu wa mowombera tirigu nthawi ya chilimwe. Zonse zinawuluka ndi mphepo osasiyako chilichonse. Koma mwala umene unagwera pa chowumba chija unasanduka phiri lalikulu ndi kudzaza dziko lonse lapansi.
Tada se satr i gvožðe i zemlja i mjed i srebro i zlato, i posta kao pljeva na gumnu u ljeto, te odnese vjetar, i ne naðe mu se mjesto; a kamen, koji udari lik, posta gora velika i ispuni svu zemlju.
36 “Maloto aja ndi amenewa; tidzafotokoza tanthauzo lake kwa mfumu.
To je san; a sada æemo kazati caru što znaèi.
37 Inu mfumu, ndinu mfumu ya mafumu. Mulungu wakumwamba wakupatsani ufumu, ulamuliro ndi mphamvu ndi ulemerero;
Ti si, care, car nad carevima, jer ti Bog nebeski dade carstvo, silu i krjepost i slavu;
38 Iye anayika mʼmanja mwanu anthu ndi nyama zakuthengo ndi mbalame zamlengalenga. Kulikonse kumene zikhala, iye anakuyikani wolamulira wa zonse. Inu ndinu mutu wagolidewo.
I gdje god žive sinovi ljudski, zvijeri poljske i ptice nebeske, dao ti je u ruke, i postavio te gospodarem nad svijem tijem. Ti si ona glava zlatna.
39 “Pambuyo pa inu, ufumu wina udzadzuka, wochepa mphamvu poyerekeza ndi wanuwu. Padzabweranso ufumu wachitatu, wamkuwa, udzalamulira dziko lonse lapansi.
A nakon tebe nastaæe drugo carstvo, manje od tvojega; a potom treæe carstvo, mjedeno, koje æe vladati po svoj zemlji.
40 Pomaliza, padzakhala ufumu wachinayi, wolimba ngati chitsulo popeza chitsulo chimaphwanya ndi kutikita chilichonse. Ndipo monga chitsulo chimaphwanya zinthu ndikuteketeratu, choncho udzawononga ndi kuphwanya maufumu ena onse.
A èetvrto æe carstvo biti tvrdo kao gvožðe, jer gvožðe satire i troši sve, i kao gvožðe što sve lomi, tako æe satrti i polomiti.
41 Ndipo monga munaonera kuti mapazi ndi zala zake zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho uwu udzakhala ufumu wogawikana; komabe udzakhala ndi mphamvu zina zachitsulo zotikita.
A što si vidio stopala i prste koje od kala lonèarskoga koje od gvožða, biæe carstvo razdijeljeno, ali æe biti u njemu tvrðe od gvožða, jer si vidio gvožðe pomiješano s kalom lonèarskim.
42 Monga zala zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho ufumu uwu udzakhala pangʼono wolimba ndi pangʼono wofowoka.
I što prsti u nogu bijahu koje od gvožða koje od kala, carstvo æe biti nešto jako a nešto trošno.
43 Ndipo monga munaona chitsulo chosakanizidwa ndi dongo, choncho anthu adzakhala wosakanizana ndipo sadzagwirizana, monga muja chitsulo sichingasakanizike ndi dongo.
A što si vidio gvožðe pomiješano sa kalom lonèarskim, to æe se oni pomiješati sjemenom èovjeèijim, ali neæe prionuti jedan za drugoga kao što se gvožðe ne može smiješati s kalom.
44 “Pa nthawi ya mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa, kapenanso kuperekedwa kwa anthu ena. Udzawononga maufumu onse aja ndi kuwatheratu, koma iwo wokha udzakhalapobe mpaka muyaya.
A u vrijeme tijeh careva Bog æe nebeski podignuti carstvo koje se dovijeka neæe rasuti, i to se carstvo neæe ostaviti drugom narodu; ono æe satrti i ukinuti sva ta carstva, a samo æe stajati dovijeka,
45 Limeneli ndilo tanthauzo la masomphenya a mwala umene unagamuka pa phiri, koma osati ndi manja a anthu; mwala umene unaphwanya chitsulo, mkuwa, dongo, siliva ndi golide mʼtizidutswa. “Mulungu wamkulu wakuonetsani mfumu chimene chidzachitika kutsogolo. Malotowo ndi woona ndipo tanthauzo lake ndi lodalirika.”
Kako si vidio gdje se od gore odvali kamen bez ruku i satr gvožðe, mjed, kao, srebro i zlato. Bog veliki javi caru što æe biti poslije; san je istinit, i tumaèenje mu vjerno.
46 Pamenepo mfumu Nebukadinezara inadzigwetsa chafufumimba pamaso pa Danieli ndi kumupatsa ulemu. Ndipo inalamula kuti anthu onse amuthirire Danieli nsembe ndi kumufukizira lubani.
Tada car Navuhodonosor pade na lice svoje, i pokloni se Danilu, i zapovjedi da mu prinesu prinos i kad.
47 Mfumu inati kwa Danieli, “Zoonadi, Mulungu wako ndi Mulungu wa milungu ndi Ambuye wa mafumu ndi wowulula zinsinsi, pakuti iwe wathadi kuwulula chinsinsi ichi.”
Car progovori Danilu i reèe: doista, vaš je Bog Bog nad bogovima i gospodar nad carevima, i koji objavljuje tajne, kad si mogao otkriti ovu tajnu.
48 Ndipo mfumu inamukweza Danieli ndi kumupatsa mphatso zambiri. Anamuyika kuti akhale wolamulira chigawo chonse cha Babuloni ndi kutinso akhale woyangʼanira anthu ake onse anzeru.
Tada car uzvisi Danila, i dade mu mnoge velike darove i uèini ga gospodarem svoj zemlji Vavilonskoj i poglavarem nad svijem mudarcima Vavilonskim.
49 Komanso, monga mwa pempho la Danieli, mfumu inayika Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti akhale oyangʼanira chigawo cha Babuloni, pamene Danieliyo ankakhazikika mʼbwalo la mfumu.
I Danilo izmoli u cara, te postavi nad poslovima zemlje Vavilonske Sedraha, Misaha i Avdenaga, a Danilo osta na dvoru carevu.

< Danieli 2 >