< Danieli 2 >

1 Chaka chachiwiri cha ulamuliro wake, Nebukadinezara analota maloto; anavutika mu mtima mwake ndipo analephera kugona.
In the secounde yeer of the rewme of Nabugodonosor, Nabugodonosor siy a dreem; and his spirit was aferd, and his dreem fledde awei fro hym.
2 Tsono mfumu inayitana amatsenga, owombeza, amawula ndi oyangʼana nyenyezi kuti amufotokozere zomwe analota. Pamene iwo analowa ndi kuyima pamaso pa mfumu,
Therfor the kyng comaundide, that the dyuynours, and astronomyens, and witchis, and Caldeis schulden be clepid togidere, that thei schulden telle to the kyng hise dremys; and whanne thei weren comun, thei stoden bifor the king.
3 mfumuyo inawawuza kuti, “Ndalota loto lomwe likundisautsa ndipo ndikufuna kudziwa tanthauzo lake.”
And the king seide to hem, Y siy a dreem, and Y am schent in mynde, and Y knowe not what Y siy.
4 Pamenepa alawuli anati kwa mfumu mʼChiaramu, “Mukhale ndi moyo wautali mfumu! Tiwuzeni ife atumiki anu zimene mwalota, ndipo tidzakuwuzani tanthauzo lake.”
And Caldeis answeriden the kyng bi Sirik langage, Kyng, liue thou with outen ende; seie thi dreem to thi seruauntis, and we schulen schewe to thee the expownyng therof.
5 Mfumu inayankha alawuliwo kuti, “Zimene ndatsimikiza kuchita ndi izi: Ngati inu simundifotokozera zimene ndalota ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli ndipo nyumba zanu ndidzazisandutsa bwinja.
And the kyng answeride, and seide to Caldeis, The word is goen awei fro me; if ye schewen not to me the dreem, and expownyng therof, ye schulen perische, and youre housis schulen be forfetid.
6 Koma ngati mundiwuza zimene ndalota ndi tanthauzo lake, ndidzakupatsani mphatso ndi mphotho ndi ulemu waukulu. Choncho mundiwuze zimene ndalota ndi tanthauzo lake.”
Forsothe if ye tellen the dreem, and the expownyng therof, ye schulen take of me meedis and yiftis, and myche onour; therfor schewe ye to me the dreem, and the interpretyng therof.
7 Iwo anayankhanso kachiwiri kuti, “Mfumu iwuze atumiki ake chimene yalota, ndipo ife tidzatanthauzira.”
Thei answeriden the secounde tyme, and seiden, The kyng seie the dreem to hise seruauntis, and we schulen schewe the interpretyng therof.
8 Ndipo mfumu inayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti mukungozengereza kufuna kutaya nthawi chabe chifukwa mukuzindikira kuti izi ndi zimene ndatsimikiza kuchita.
The kyng answeride, and seide, Certis Y woot, that ye ayenbien the tyme, and witen that the word is goen awei fro me.
9 Ngati simundiwuza zimene ndalota, chilango chake ndi chimodzi. Inu mwagwirizana kuti mundiwuze ine bodza ndi chinyengo ndi kuyembekeza kuti ine ndisintha. Tsono mundiwuze zimene ndalota, ndipo ine ndidzadziwa kuti mukhoza kunditanthauzira.”
Therfor if ye schewen not to me the dreem, o sentence is of you, for ye maken an interpretyng bothe fals and ful of disseit, that ye speke to me til the tyme passe; therfor seie ye the dreem to me, that Y wite, that ye speke also the veri interpretyng therof.
10 Alawuli anayankha mfumu kuti, “Palibe munthu pa dziko lapansi amene akhoza kuchita chimene mfumu ikufunsa! Palibe mfumu, kaya yayikulu kapena yamphamvu bwanji imene inafunsapo amatsenga, owombeza kapena alawuli aliwonse zimenezi.
Therfor Caldeis answeriden bifor the kyng, and seiden, Kyng, no man is on erthe, that mai fille thi word; but nether ony greet man and myyti of kyngis axith siche a word of ony dyuynour, and astronomyen, and of a man of Caldee.
11 Zimene mfumu yafunsa ndi zapatali. Palibe wina amene angathe kuwulula izi kwa mfumu kupatula milungu, ndipo sikhala pakati pa anthu.”
For the word which thou, kyng, axist, is greuouse, nether ony schal be foundun, that schal schewe it in the siyt of the king, outakun goddis, whos lyuyng is not with men.
12 Zimenezi zinapsetsa mtima mfumu ndipo inakwiya kwambiri kotero inalamula kuti anzeru onse a ku Babuloni aphedwe.
And whanne this word was herd, the kyng comaundide, in woodnesse and in greet ire, that alle the wise men of Babiloyne schulden perische.
13 Choncho lamulo linaperekedwa kuti anthu anzeru aphedwe, ndipo anatuma anthu kukafunafuna Danieli ndi anzake kuti iwonso aphedwe.
And bi the sentence goon out, the wise men weren slayn; and Danyel and hise felows weren souyt, that thei schulden perische.
14 Danieli anayankhula mwanzeru ndi mwaulemu kwa Ariyoki, mkulu wa asilikali olondera mfumu amene anatumidwa kukapha anthu anzeru a ku Babuloni.
Thanne Danyel axide of the lawe and sentence, of Ariok, prynce of chyualrie of the kyng, that was gon out to sle the wise men of Babiloyne.
15 Danieli anafunsa Ariyoki kapitawo wa mfumu kuti, “Chifukwa chiyani mfumu yapereka lamulo lankhanza lotere?” Kenaka Ariyoki anafotokoza nkhaniyi kwa Danieli.
And he axide hym, that hadde take power of the kyng, for what cause so cruel a sentence yede out fro the face of the kyng. Therfor whanne Ariok hadde schewid the thing to Danyel,
16 Danieli anapita mofulumira kwa mfumu ndipo anamupempha kuti amupatse nthawi kuti amuwuze zimene walota ndi tanthauzo lake.
Danyel entride, and preyede the kyng, that he schulde yyue tyme to hym to schewe the soilyng to the kyng.
17 Kenaka Danieli anabwerera ku nyumba kwake ndi kukafotokozera anzake aja zimenezi: Hananiya, Misaeli ndi Azariya.
And he entride in to his hous, and schewide the nede to Ananye, and to Misael, and Asarie,
18 Danieli anadandaulira anzake kuti apemphe kwa Mulungu wakumwamba kuti awachitire chifundo ndi kumuwululira chinsinsi, kuti iye ndi anzakewo asanyongedwe pamodzi ndi anzeru ena onse a ku Babuloni.
hise felowis, that thei schulden axe merci of the face of God of heuene on this sacrament; and that Danyel and hise felowis schulden not perische with othere wise men of Babiloyne.
19 Usiku Yehova anamuwululira Danieli chinsinsi chija mʼmasomphenya. Pamenepo Danieli anatamanda Mulungu wakumwamba,
Thanne the priuyte was schewid to Danyel bi a visioun in nyyt. And Danyel blesside God of heuene, and seide,
20 ndipo anati: “Litamandike dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi; nzeru ndi mphamvu zonse ndi zake.
The name of the Lord be blessid fro the world, and til in to the world, for wisdom and strengthe ben hise;
21 Amasintha nthawi ndi nyengo; amakweza mafumu ndipo amawatsitsanso. Amapatsa nzeru kwa anzeru ndi chidziwitso kwa ozindikira zinthu.
and he chaungith tymes and ages, he translatith rewmes and ordeyneth; he yyueth wisdom to wise men, and kunnyng to hem that vndurstonden techyng, ether chastisyng;
22 Amavumbulutsa zinthu zozama ndi zobisika; amadziwa zimene zili mu mdima, ndipo kuwunika kumakhala ndi Iye.
he schewith deepe thingis and hid, and he knowith thingis set in derknessis, and liyt is with hym.
23 Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga: mwandipatsa nzeru ndi mphamvu, mwandiwululira zomwe tinakupemphani, mwatiwululira maloto a mfumu.”
God of oure fadris, Y knowleche to thee, and Y herie thee, for thou hast youe wisdom and strengthe to me; and now thou hast schewid to me tho thingis, whiche we preieden thee, for thou hast openyd to vs the word of the kyng.
24 Motero Danieli anapita kwa Ariyoki, amene mfumu inamusankha kuti akaphe anthu anzeru a ku Babuloni, ndipo anati kwa iye, “Musaphe anthu anzeru a ku Babuloni. Ndiperekezeni kwa mfumu, ndipo ndidzayimasulira maloto ake.”
Aftir these thingis Danyel entride to Ariok, whom the kyng hadde ordeyned, that he schulde leese the wise men of Babiloyne, and thus he spak to hym, Leese thou not the wise men of Babiloyne; leede thou me in bifor the siyt of the kyng, and Y schal telle the soilyng to the kyng.
25 Ariyoki anapita naye Danieli kwa mfumu nthawi yomweyo ndipo anati, “Ndapeza munthu pakati pa akapolo ochokera ku Yuda amene akhoza kuwuza mfumu zimene maloto ake akutanthauza.”
Thanne Ariok hastynge ledde in Danyel to the kyng, and seide to him, Y haue foundun a man of the sones of passyng ouer of Juda, that schal telle the soilyng to the kyng.
26 Mfumu inafunsa Danieli (wotchedwanso Belitesezara) kuti, “Kodi ukhoza kundiwuza zomwe ine ndinaona mʼmaloto anga ndi tanthauzo lake?”
The kyng answeride, and seide to Danyel, to whom the name was Balthasar, Whethir gessist thou, that thou maist verili schewe to me the dreem which Y siy, and the interpretyng therof?
27 Danieli anayankha kuti, “Palibe munthu wanzeru, wowombeza, wamatsenga kapena wamawula amene akhoza kufotokozera mfumu chinsinsi chimene mwafuna kudziwa,
And Danyel answeride bifore the king, and seide, The priuytee which the kyng axith, wise men, and astronomyens, and dyuynours, and lokeris of auteris, moun not schewe to the kyng.
28 koma kuli Mulungu kumwamba amene amawulula zinsinsi. Iye waonetsera mfumu Nebukadinezara zimene zidzachitika mʼmasiku akutsogolo. Maloto ndi masomphenya anu amene munawaona mukugona pa bedi lanu ndi awa:
But God is in heuene, that schewith priuytees, which hath schewid to thee, thou king Nabugodonosor, what thingis schulen come in the laste tymes. Thi dreem and visiouns of thin heed, in thi bed, ben sich.
29 “Mukugona pa bedi, inu Mfumu, maganizo anakufikirani a zinthu zakutsogolo, ndipo Yehova wowulula zinsinsi anakuonetserani zimene zidzachitika.
Thou, kyng, bigunnest to thenke in thi bed, what was to comynge aftir these thingis; and he that schewith priuetees, schewide to thee what thingis schulen come.
30 Koma chinsinsi ichi chavumbulutsidwa kwa ine, si chifukwa chakuti ndili ndi nzeru zochuluka kuposa anthu ena onse, koma kuti mfumu mudziwe tanthauzo la maloto anu ndi kuti muzindikire maganizo amene anali mu mtima mwanu.
And this sacrament is schewid to me, not bi wisdom which is in me more than in alle lyuynge men, but that the interpretyng schulde be maad opyn to the kyng, and thou schuldist knowe the thouytis of thi soule.
31 “Inu mfumu, munaona chinthu chowumba chachikulu chimene chinayima pamaso panu. Chowumbachi chinali chonyezimira mʼmaonekedwe.
Thou, kyng, siyest, and lo! as o greet ymage; thilke ymage was greet, and hiy in stature, and stood bifore thee, and the loking therof was ferdful.
32 Mutu wa chowumbacho unali wagolide wabwino kwambiri. Chifuwa ndi manja ake zinali zasiliva. Mimba ndi ntchafu zake zinali zamkuwa.
The heed of this ymage was of best gold, but the brest and armes weren of siluer; certis the wombe and thies weren of bras,
33 Miyendo yake inali yachitsulo, mapazi ake anali achitsulo chosakaniza ndi dongo.
but the leggis weren of irun; forsothe sum part of the feet was of irun, sum was of erthe.
34 Inu mukuona, mwala unagamuka, koma osati ndi manja a munthu. Unagwera fanolo pa mapazi ake achitsulo chosakaniza ndi dongo aja ndi kuwaphwanya.
Thou siyest thus, til a stoon was kit doun of the hil, with outen hondis, and smoot the ymage in the irun feet therof and erthene feet, and al to-brak tho.
35 Tsono chitsulo, dongo, mkuwa, siliva ndi golide zonse zinaphwanyika pamodzi ndikukhala tizidutswa towuluka ndi mphepo ngati mungu wa mowombera tirigu nthawi ya chilimwe. Zonse zinawuluka ndi mphepo osasiyako chilichonse. Koma mwala umene unagwera pa chowumba chija unasanduka phiri lalikulu ndi kudzaza dziko lonse lapansi.
Thanne the irun, tijl stoon, ether erthene vessel, bras, siluer, and gold, weren al to-brokun togidere, and dryuun as in to a deed sparcle of a large somer halle, that ben rauyschid of wynd, and no place is foundun to tho; forsothe the stoon, that smoot the ymage, was maad a greet hil, and fillide al erthe.
36 “Maloto aja ndi amenewa; tidzafotokoza tanthauzo lake kwa mfumu.
This is the dreem. Also, thou kyng, we schulen seie bifor thee the interpretyng therof.
37 Inu mfumu, ndinu mfumu ya mafumu. Mulungu wakumwamba wakupatsani ufumu, ulamuliro ndi mphamvu ndi ulemerero;
Thou art kyng of kyngis, and God of heuene yaf to thee rewme, strengthe, and empire, and glorie;
38 Iye anayika mʼmanja mwanu anthu ndi nyama zakuthengo ndi mbalame zamlengalenga. Kulikonse kumene zikhala, iye anakuyikani wolamulira wa zonse. Inu ndinu mutu wagolidewo.
and he yaf in thin hond alle thingis, in whiche the sones of men, and the beestis of the feeld, and the briddis of the eir dwellen, and ordeynede alle thingis vndur thi lordschip; therfor thou art the goldun heed.
39 “Pambuyo pa inu, ufumu wina udzadzuka, wochepa mphamvu poyerekeza ndi wanuwu. Padzabweranso ufumu wachitatu, wamkuwa, udzalamulira dziko lonse lapansi.
And another rewme lesse than thou schal rise aftir thee; and the thridde rewme, an other of bras, that schal haue the empire of al erthe.
40 Pomaliza, padzakhala ufumu wachinayi, wolimba ngati chitsulo popeza chitsulo chimaphwanya ndi kutikita chilichonse. Ndipo monga chitsulo chimaphwanya zinthu ndikuteketeratu, choncho udzawononga ndi kuphwanya maufumu ena onse.
And the fourthe rewme schal be as irun, as irun makith lesse, and makith tame alle thingis, so it schal make lesse, and schal al to-breke alle these rewmes.
41 Ndipo monga munaonera kuti mapazi ndi zala zake zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho uwu udzakhala ufumu wogawikana; komabe udzakhala ndi mphamvu zina zachitsulo zotikita.
Forsothe that thou siest a part of the feet and fyngris of erthe of a pottere, and a part of irun, the rewme shal be departid; which netheles schal rise of the plauntyng of irun, `bi that that thou siest irun meynd with a tijl stoon of clei,
42 Monga zala zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho ufumu uwu udzakhala pangʼono wolimba ndi pangʼono wofowoka.
and the toos of the feet in parti of irun, and in parti of erthe, in parti the rewme schal be sad, and in parti to-brokun.
43 Ndipo monga munaona chitsulo chosakanizidwa ndi dongo, choncho anthu adzakhala wosakanizana ndipo sadzagwirizana, monga muja chitsulo sichingasakanizike ndi dongo.
Forsothe that thou siest irun meynd with a tiel stoon of clei, sotheli tho schulen be meynd togidere with mannus seed; but tho schulen not cleue to hem silf, as irun mai not be meddlid with tyel stoon.
44 “Pa nthawi ya mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa, kapenanso kuperekedwa kwa anthu ena. Udzawononga maufumu onse aja ndi kuwatheratu, koma iwo wokha udzakhalapobe mpaka muyaya.
Forsothe in the daies of tho rewmes, God of heuene shal reise a rewme, that schal not be distried with outen ende, and his rewme schal not be youun to another puple; it schal make lesse, and schal waste alle these rewmes, and it schal stonde with outen ende,
45 Limeneli ndilo tanthauzo la masomphenya a mwala umene unagamuka pa phiri, koma osati ndi manja a anthu; mwala umene unaphwanya chitsulo, mkuwa, dongo, siliva ndi golide mʼtizidutswa. “Mulungu wamkulu wakuonetsani mfumu chimene chidzachitika kutsogolo. Malotowo ndi woona ndipo tanthauzo lake ndi lodalirika.”
bi this that thou siest, that a stoon was kit doun of the hil with outen hondis, and maad lesse the tiel stoon, and irun, and bras, and siluer, and gold. Greet God hath schewid to the kyng, what thingis schulen come aftirward; and the dreem is trewe, and the interpretyng therof is feithful.
46 Pamenepo mfumu Nebukadinezara inadzigwetsa chafufumimba pamaso pa Danieli ndi kumupatsa ulemu. Ndipo inalamula kuti anthu onse amuthirire Danieli nsembe ndi kumufukizira lubani.
Thanne king Nabugodonosor felle doun on his face, and worschipide Danyel, and comaundide sacrifices and encense to be brouyt, that tho schulden be sacrifised to hym.
47 Mfumu inati kwa Danieli, “Zoonadi, Mulungu wako ndi Mulungu wa milungu ndi Ambuye wa mafumu ndi wowulula zinsinsi, pakuti iwe wathadi kuwulula chinsinsi ichi.”
Therfor the kyng spak, and seide to Danyel, Verili youre God is God of goddis, and Lord of kyngis, that schewith mysteries, for thou miytist opene this sacrament.
48 Ndipo mfumu inamukweza Danieli ndi kumupatsa mphatso zambiri. Anamuyika kuti akhale wolamulira chigawo chonse cha Babuloni ndi kutinso akhale woyangʼanira anthu ake onse anzeru.
Thanne the kyng reiside Danyel an hiy, and yaf many yiftis and grete to hym; and ordeynede hym prince and prefect, ether cheef iustise, ouer alle the prouynces of Babiloyne, and maister ouer alle the wise men of Babiloyne.
49 Komanso, monga mwa pempho la Danieli, mfumu inayika Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti akhale oyangʼanira chigawo cha Babuloni, pamene Danieliyo ankakhazikika mʼbwalo la mfumu.
Forsothe Danyel axide of the kyng, and ordeynede Sidrac, Misaac, and Abdenago ouer alle the werkis of the prouynce of Babiloyne; but Danyel hym silf was in the yatis of the kyng.

< Danieli 2 >