< Danieli 2 >

1 Chaka chachiwiri cha ulamuliro wake, Nebukadinezara analota maloto; anavutika mu mtima mwake ndipo analephera kugona.
And in the seconde yeere of the raygne of Nebuchad-nezzar, Nebuchad-nezzar dreamed dreames wherewith his spirite was troubled, and his sleepe was vpon him.
2 Tsono mfumu inayitana amatsenga, owombeza, amawula ndi oyangʼana nyenyezi kuti amufotokozere zomwe analota. Pamene iwo analowa ndi kuyima pamaso pa mfumu,
Then the King commanded to call the inchanters, and the astrologians and the sorcerers, and the Caldeans for to shewe the King his dreames: so they came and stoode before the King.
3 mfumuyo inawawuza kuti, “Ndalota loto lomwe likundisautsa ndipo ndikufuna kudziwa tanthauzo lake.”
And the King sayde vnto them, I haue dreamed a dreame, and my spirite was troubled to knowe the dreame.
4 Pamenepa alawuli anati kwa mfumu mʼChiaramu, “Mukhale ndi moyo wautali mfumu! Tiwuzeni ife atumiki anu zimene mwalota, ndipo tidzakuwuzani tanthauzo lake.”
Then spake the Caldeans to the King in the Aramites language, O King, liue for euer: shewe thy seruants thy dreame, and wee shall shewe the interpretation.
5 Mfumu inayankha alawuliwo kuti, “Zimene ndatsimikiza kuchita ndi izi: Ngati inu simundifotokozera zimene ndalota ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli ndipo nyumba zanu ndidzazisandutsa bwinja.
And the King answered and sayd to the Caldeans, The thing is gone from me. If ye will not make me vnderstande the dreame with the interpretation thereof, ye shall be drawen in pieces, and your houses shall be made a iakes.
6 Koma ngati mundiwuza zimene ndalota ndi tanthauzo lake, ndidzakupatsani mphatso ndi mphotho ndi ulemu waukulu. Choncho mundiwuze zimene ndalota ndi tanthauzo lake.”
But if yee declare the dreame and the interpretation thereof, ye shall receyue of me gifts and rewardes, and great honour: therefore shewe me the dreame and the interpretation of it.
7 Iwo anayankhanso kachiwiri kuti, “Mfumu iwuze atumiki ake chimene yalota, ndipo ife tidzatanthauzira.”
They answered againe, and sayde, Let the King shewe his seruantes the dreame, and wee will declare the interpretation thereof.
8 Ndipo mfumu inayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti mukungozengereza kufuna kutaya nthawi chabe chifukwa mukuzindikira kuti izi ndi zimene ndatsimikiza kuchita.
Then the King answered, and sayd, I knowe certeinly that ye would gaine the time, because ye see the thing is gone from me.
9 Ngati simundiwuza zimene ndalota, chilango chake ndi chimodzi. Inu mwagwirizana kuti mundiwuze ine bodza ndi chinyengo ndi kuyembekeza kuti ine ndisintha. Tsono mundiwuze zimene ndalota, ndipo ine ndidzadziwa kuti mukhoza kunditanthauzira.”
But if ye will not declare mee the dreame, there is but one iudgement for you: for ye haue prepared lying and corrupt wordes, to speake before me till the time bee changed: therefore tell me the dreame, that I may knowe, if yee can declare me the interpretation thereof.
10 Alawuli anayankha mfumu kuti, “Palibe munthu pa dziko lapansi amene akhoza kuchita chimene mfumu ikufunsa! Palibe mfumu, kaya yayikulu kapena yamphamvu bwanji imene inafunsapo amatsenga, owombeza kapena alawuli aliwonse zimenezi.
Then the Caldeans answered before the King, and sayde, There is no man vpon earth that can declare the Kings matter: yea, there is neither king nor prince nor lorde that asked such things at an inchanter or astrologian or Caldean.
11 Zimene mfumu yafunsa ndi zapatali. Palibe wina amene angathe kuwulula izi kwa mfumu kupatula milungu, ndipo sikhala pakati pa anthu.”
For it is a rare thing that the King requireth, and there is none other that can declare it before the King, except the gods whose dwelling is not with flesh.
12 Zimenezi zinapsetsa mtima mfumu ndipo inakwiya kwambiri kotero inalamula kuti anzeru onse a ku Babuloni aphedwe.
For this cause the king was angrie and in great furie, and commanded to destroy all the wise men of Babel.
13 Choncho lamulo linaperekedwa kuti anthu anzeru aphedwe, ndipo anatuma anthu kukafunafuna Danieli ndi anzake kuti iwonso aphedwe.
And when sentence was giuen, the wise men were slayne: and they sought Daniel and his fellowes to be put to death.
14 Danieli anayankhula mwanzeru ndi mwaulemu kwa Ariyoki, mkulu wa asilikali olondera mfumu amene anatumidwa kukapha anthu anzeru a ku Babuloni.
Then Daniel answered with counsel and wisedome to Arioch the Kings chiefe stewarde, which was gone foorth to put to death the wise men of Babel.
15 Danieli anafunsa Ariyoki kapitawo wa mfumu kuti, “Chifukwa chiyani mfumu yapereka lamulo lankhanza lotere?” Kenaka Ariyoki anafotokoza nkhaniyi kwa Danieli.
Yea, he answered and sayde vnto Arioch the kings captaine, Why is the sentence so hastie from the king? Then Arioch declared the thing to Daniel.
16 Danieli anapita mofulumira kwa mfumu ndipo anamupempha kuti amupatse nthawi kuti amuwuze zimene walota ndi tanthauzo lake.
So Daniel went and desired the king that he woulde giue him leasure and that he woulde shewe the king the interpretation thereof.
17 Kenaka Danieli anabwerera ku nyumba kwake ndi kukafotokozera anzake aja zimenezi: Hananiya, Misaeli ndi Azariya.
The Daniel went to his house and shewed the matter to Hananiah, Mishael, and Azariah his companions,
18 Danieli anadandaulira anzake kuti apemphe kwa Mulungu wakumwamba kuti awachitire chifundo ndi kumuwululira chinsinsi, kuti iye ndi anzakewo asanyongedwe pamodzi ndi anzeru ena onse a ku Babuloni.
That they should beseech the God of heauen for grace in this secrete, that Daniel and his fellowes should not perish with the rest of ye wise men of Babel.
19 Usiku Yehova anamuwululira Danieli chinsinsi chija mʼmasomphenya. Pamenepo Danieli anatamanda Mulungu wakumwamba,
Then was the secret reueiled vnto Daniel in a vision by night: therefore Daniel praysed the God of heauen.
20 ndipo anati: “Litamandike dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi; nzeru ndi mphamvu zonse ndi zake.
And Daniel answered and sayde, The Name of God be praysed for euer and euer: for wisedome and strength are his,
21 Amasintha nthawi ndi nyengo; amakweza mafumu ndipo amawatsitsanso. Amapatsa nzeru kwa anzeru ndi chidziwitso kwa ozindikira zinthu.
And hee changeth the times and seasons: he taketh away kings: he setteth vp kings: he giueth wisedome vnto the wise, and vnderstanding to those that vnderstand.
22 Amavumbulutsa zinthu zozama ndi zobisika; amadziwa zimene zili mu mdima, ndipo kuwunika kumakhala ndi Iye.
Hee discouereth the deepe and secrete things: he knoweth what is in darkenes, and the light dwelleth with him.
23 Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga: mwandipatsa nzeru ndi mphamvu, mwandiwululira zomwe tinakupemphani, mwatiwululira maloto a mfumu.”
I thanke thee and prayse thee, O thou God of my fathers, that thou hast giuen mee wisedome and strength, and hast shewed me nowe the thing that wee desired of thee: for thou hast declared vnto vs the kings matter.
24 Motero Danieli anapita kwa Ariyoki, amene mfumu inamusankha kuti akaphe anthu anzeru a ku Babuloni, ndipo anati kwa iye, “Musaphe anthu anzeru a ku Babuloni. Ndiperekezeni kwa mfumu, ndipo ndidzayimasulira maloto ake.”
Therefore Daniel went vnto Arioch, whome the King had ordeyned to destroy the wise men of Babel: he went and sayde thus vnto him, Destroy not the wise men of Babel, but bring me before the King, and I will declare vnto the King the interpretation.
25 Ariyoki anapita naye Danieli kwa mfumu nthawi yomweyo ndipo anati, “Ndapeza munthu pakati pa akapolo ochokera ku Yuda amene akhoza kuwuza mfumu zimene maloto ake akutanthauza.”
Then Arioch brought Daniel before the King in all haste, and sayd thus vnto him, I haue found a man of the children of Iudah that were brought captiues, that will declare vnto the King the interpretation.
26 Mfumu inafunsa Danieli (wotchedwanso Belitesezara) kuti, “Kodi ukhoza kundiwuza zomwe ine ndinaona mʼmaloto anga ndi tanthauzo lake?”
Then answered the King, and sayde vnto Daniel, whose name was Belteshazzar, Art thou able to shew me the dreame, which I haue seene, and the interpretation thereof?
27 Danieli anayankha kuti, “Palibe munthu wanzeru, wowombeza, wamatsenga kapena wamawula amene akhoza kufotokozera mfumu chinsinsi chimene mwafuna kudziwa,
Daniel answered in the presence of the King, and sayd, The secret which the King hath demanded, can neither the wise, the astrologians, the inchanters, nor the southsayers declare vnto the King.
28 koma kuli Mulungu kumwamba amene amawulula zinsinsi. Iye waonetsera mfumu Nebukadinezara zimene zidzachitika mʼmasiku akutsogolo. Maloto ndi masomphenya anu amene munawaona mukugona pa bedi lanu ndi awa:
But there is a God in heauen that reueileth secrets, and sheweth the King Nebuchad-nezzar what shall bee in the latter dayes. Thy dreame, and the things which thou hast seene in thine heade vpon thy bed, is this.
29 “Mukugona pa bedi, inu Mfumu, maganizo anakufikirani a zinthu zakutsogolo, ndipo Yehova wowulula zinsinsi anakuonetserani zimene zidzachitika.
O King, when thou wast in thy bedde, thoughts came into thy mind, what should come to passe hereafter, and he that reueyleth secretes, telleth thee, what shall come.
30 Koma chinsinsi ichi chavumbulutsidwa kwa ine, si chifukwa chakuti ndili ndi nzeru zochuluka kuposa anthu ena onse, koma kuti mfumu mudziwe tanthauzo la maloto anu ndi kuti muzindikire maganizo amene anali mu mtima mwanu.
As for me, this secret is not shewed mee for any wisedome that I haue, more then any other liuing, but onely to shewe the King the interpretation, and that thou mightest knowe the thoughts of thine heart.
31 “Inu mfumu, munaona chinthu chowumba chachikulu chimene chinayima pamaso panu. Chowumbachi chinali chonyezimira mʼmaonekedwe.
O King, thou sawest, and beholde, there was a great image: this great image whose glory was so excellent, stood before thee, and the forme thereof was terrible.
32 Mutu wa chowumbacho unali wagolide wabwino kwambiri. Chifuwa ndi manja ake zinali zasiliva. Mimba ndi ntchafu zake zinali zamkuwa.
This images head was of fine golde, his breast and his armes of siluer, his bellie and his thighs of brasse,
33 Miyendo yake inali yachitsulo, mapazi ake anali achitsulo chosakaniza ndi dongo.
His legges of yron, and his feete were part of yron, and part of clay.
34 Inu mukuona, mwala unagamuka, koma osati ndi manja a munthu. Unagwera fanolo pa mapazi ake achitsulo chosakaniza ndi dongo aja ndi kuwaphwanya.
Thou beheldest it til a stone was cut without hands, which smote the image vpon his feete, that were of yron and clay, and brake them to pieces.
35 Tsono chitsulo, dongo, mkuwa, siliva ndi golide zonse zinaphwanyika pamodzi ndikukhala tizidutswa towuluka ndi mphepo ngati mungu wa mowombera tirigu nthawi ya chilimwe. Zonse zinawuluka ndi mphepo osasiyako chilichonse. Koma mwala umene unagwera pa chowumba chija unasanduka phiri lalikulu ndi kudzaza dziko lonse lapansi.
Then was the yron, the clay, the brasse, the siluer and the golde broken all together, and became like the chaffe of the sommer floures, and the winde caryed them away, that no place was founde for them: and the stone that smote the image, became a great mountaine, and filled the whole earth.
36 “Maloto aja ndi amenewa; tidzafotokoza tanthauzo lake kwa mfumu.
This is the dreame, and we will declare before the King the interpretation thereof.
37 Inu mfumu, ndinu mfumu ya mafumu. Mulungu wakumwamba wakupatsani ufumu, ulamuliro ndi mphamvu ndi ulemerero;
O King, thou art a king of Kings: for the God of heauen hath giuen thee a kingdome, power, and strength, and glorie.
38 Iye anayika mʼmanja mwanu anthu ndi nyama zakuthengo ndi mbalame zamlengalenga. Kulikonse kumene zikhala, iye anakuyikani wolamulira wa zonse. Inu ndinu mutu wagolidewo.
And in all places where the children of men dwell, the beasts of the fielde, and the foules of the heauen hath he giuen into thine hand, and hath made thee ruler ouer them al: thou art this heade of golde.
39 “Pambuyo pa inu, ufumu wina udzadzuka, wochepa mphamvu poyerekeza ndi wanuwu. Padzabweranso ufumu wachitatu, wamkuwa, udzalamulira dziko lonse lapansi.
And after thee shall rise another kingdome, inferiour to thee, of siluer, and another third kingdome shalbe of brasse, which shall beare rule ouer all the earth.
40 Pomaliza, padzakhala ufumu wachinayi, wolimba ngati chitsulo popeza chitsulo chimaphwanya ndi kutikita chilichonse. Ndipo monga chitsulo chimaphwanya zinthu ndikuteketeratu, choncho udzawononga ndi kuphwanya maufumu ena onse.
And the fourth kingdome shall be strong as yron: for as yron breaketh in pieces, and subdueth all things, and as yron bruiseth all these things, so shall it breake in pieces, and bruise all.
41 Ndipo monga munaonera kuti mapazi ndi zala zake zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho uwu udzakhala ufumu wogawikana; komabe udzakhala ndi mphamvu zina zachitsulo zotikita.
Where as thou sawest the feete and toes, parte of potters clay, and part of yron: the kingdome shalbe deuided, but there shalbe in it of the strength of the yron, as thou sawest the yron mixt with the clay, and earth.
42 Monga zala zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho ufumu uwu udzakhala pangʼono wolimba ndi pangʼono wofowoka.
And as the toes of the feete were parte of yron, and parte of clay, so shall the kingdome be partly strong, and partly broken.
43 Ndipo monga munaona chitsulo chosakanizidwa ndi dongo, choncho anthu adzakhala wosakanizana ndipo sadzagwirizana, monga muja chitsulo sichingasakanizike ndi dongo.
And where as thou sawest yron mixt with clay and earth, they shall mingle themselues with the seede of men: but they shall not ioyne one with another, as yron can not bee mixed with clay.
44 “Pa nthawi ya mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa, kapenanso kuperekedwa kwa anthu ena. Udzawononga maufumu onse aja ndi kuwatheratu, koma iwo wokha udzakhalapobe mpaka muyaya.
And in the dayes of these Kings, shall the God of heauen set vp a kingdome, which shall neuer be destroyed: and this kingdome shall not be giuen to another people, but it shall breake, and destroy al these kingdomes, and it shall stand for euer.
45 Limeneli ndilo tanthauzo la masomphenya a mwala umene unagamuka pa phiri, koma osati ndi manja a anthu; mwala umene unaphwanya chitsulo, mkuwa, dongo, siliva ndi golide mʼtizidutswa. “Mulungu wamkulu wakuonetsani mfumu chimene chidzachitika kutsogolo. Malotowo ndi woona ndipo tanthauzo lake ndi lodalirika.”
Where as thou sawest, that the stone was cut of the mountaine without handes, and that it brake in pieces the yron, the brasse, the clay, the siluer, and the golde: so the great God hath shewed the King, what shall come to passe hereafter, and the dreame is true, and the interpretation thereof is sure.
46 Pamenepo mfumu Nebukadinezara inadzigwetsa chafufumimba pamaso pa Danieli ndi kumupatsa ulemu. Ndipo inalamula kuti anthu onse amuthirire Danieli nsembe ndi kumufukizira lubani.
Then the King Nebuchad-nezzar fell vpon his face, and bowed himselfe vnto Daniel, and commanded that they should offer meate offrings, and sweete odours vnto him.
47 Mfumu inati kwa Danieli, “Zoonadi, Mulungu wako ndi Mulungu wa milungu ndi Ambuye wa mafumu ndi wowulula zinsinsi, pakuti iwe wathadi kuwulula chinsinsi ichi.”
Also the King answered vnto Daniel, and said, I know of a trueth that your God is a God of gods, and the Lord of Kings, and the reueiler of secrets, seeing thou couldest open this secret.
48 Ndipo mfumu inamukweza Danieli ndi kumupatsa mphatso zambiri. Anamuyika kuti akhale wolamulira chigawo chonse cha Babuloni ndi kutinso akhale woyangʼanira anthu ake onse anzeru.
So the King made Daniel a great man, and gaue him many and great giftes. Hee made him gouernour ouer the whole prouince of Babel, and chiefe of the rulers, and aboue all the wise men of Babel.
49 Komanso, monga mwa pempho la Danieli, mfumu inayika Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti akhale oyangʼanira chigawo cha Babuloni, pamene Danieliyo ankakhazikika mʼbwalo la mfumu.
Then Daniel made request to the King, and hee set Shadrach, Meshach, and Abednego ouer the charge of the prouince of Babel: but Daniel sate in the gate of the King.

< Danieli 2 >