< Akolose 2 >

1 Ndikufuna mudziwe kuti ndikukuvutikirani kwambiri, inuyo pamodzi ndi anzanu a ku Laodikaya, ndi ena onse amene sitinaonane maso ndi maso.
Så vill jag att I veta skolen, hvilken kamp jag hafver om eder, och om dem som äro i Laodicea, och om alla dem som min person i köttet icke sett hafva;
2 Cholinga changa nʼchakuti alimbikitsidwe ndi kuyanjana pamodzi mʼchikondi, akhale odzaza ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndi kuti azindikire chinsinsi cha Mulungu, chimene ndi Khristu.
På det deras hjerta måga få någon hugnad, och sammanfogade varda i kärlekenom, till all rikedom uti fullkomligit förstånd, till att kunna besinna Guds hemlighet, både Fadrens och Christi;
3 Mwa Iyeyu muli chuma chonse chobisidwa cha nzeru ndi chidziwitso.
Uti hvilkom fördolda ligga alla visdoms och förstånds håfvor.
4 Ndikukuwuzani zimenezi kuti wina aliyense asakunamizeni ndi kukukopani ndi mawu ake.
Men detta säger jag, på det ingen skall bedraga eder med klok ord.
5 Pakuti ngakhale sindili pakati panu mʼthupi, ndili nanu pamodzi mu mzimu, ndipo ndikukondwa kuona kuti mukulongosola bwino zonse ndiponso kuti chikhulupiriro chanu mwa Khristu ndi chokhazikika ndithu.
Ty ändock jag är ifrån eder efter köttet, är jag dock när eder i Andanom, fröjdar mig, och ser edor skickelse, och edar tros stadighet på Christum.
6 Tsono popeza munavomereza Khristu Yesu kukhala Ambuye anu, mupitirire kukhala mwa Iyeyo.
Såsom I nu anammat hafven Herran Christum Jesum, så vandrer i honom;
7 Mukhale ozikika mizu mwa Iye, ndipo moyo wanu umangike pa Iye. Mulimbike mʼchikhulupiriro monga momwe munaphunzirira, ndipo kuyamika kwanu kusefukire.
Och varer rotade och uppbyggde i honom, och varer faste i trone, såsom I lärde ären, och varer i henne rikeliga tacksamme.
8 Musalole kuti wina aliyense akutengeni ukapolo ndi mʼnzeru zachinyengo zolongosola zinthu zozama, zomwe zimachokera ku miyambo ya anthu ndi ku maganizo awo okhudza za dziko lapansi osati kwa Khristu.
Ser till, att eder icke någor bortröfvar med Philosophia och fåfängt bedrägeri, efter menniskors stadgar, och efter verldenes stadgar, och icke efter Christum;
9 Pakuti mʼthupi la Khristu mumakhala umulungu wonse wathunthu.
Ty i honom bor all Gudomsens fullhet lekamliga.
10 Ndipo inunso ndinu athunthu mwa Khristu. Iye ndiye mtsogoleri wa pamwamba pa maufumu onse ndi maulamuliro wonse.
Och I ären i honom fullkomne, hvilken är hufvudet öfver all Förstadöme och väldighet;
11 Mwa Iye inunso munachita mdulidwe mʼthupi lanu, osati mdulidwe ochitidwa ndi manja a anthu ayi, koma ochitidwa ndi Khristu pamene anavula khalidwe lanu lauchimo lija.
I hvilkom I ock omskorne ären med den omskärelse, som sker utan händer, då I afladen syndakroppen i köttet, nämliga med Christi omskärelse;
12 Mu ubatizo, munayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Khristu ndi kuukitsidwa naye pamodzi, pokhulupirira mphamvu za Mulungu amene anamuukitsa kwa akufa.
I det, att I med honom begrafne ären genom dopet; i hvilkom I ock uppståndne ären genom trona, den Gud verkar, hvilken honom uppväckt hafver ifrå de döda.
13 Pamene munali akufa chifukwa cha machimo anu ndi osachita mdulidwe mʼmitima mwanu, Mulungu anakupatsani moyo mwa Khristu. Iye anatikhululukira machimo athu onse.
Han hafver ock gjort eder lefvande med honom, då I döde voren i synderna, och uti edars kötts förhud; och hafver förlåtit oss alla synder;
14 Anafafaniza kalata ya ngongole yathu, pomwe panali milandu yotitsutsa ife. Iye anayichotsa, nayikhomera pa mtanda.
Och afplånat den handskrift, som oss emot var; hvilken af stadgarna kom, och var oss emot; och den hafver han tagit oss af vägen, och naglat vid korset;
15 Ndipo atalanda zida maufumu ndi maulamuliro, Iye anawachititsa manyazi powayendetsa pamaso pa anthu onse atawagonjetsa ndi mtanda.
Och hafver blottat Förstadömen, och väldigheterna, och fört dem uppenbarliga, och gjort en härlig seger af dem, genom sig sjelf.
16 Nʼchifukwa chake musalole wina aliyense kukuzengani mlandu chifukwa cha zimene mumadya kapena kumwa, kapena za masiku achikondwerero cha chipembedzo, za chikondwerero cha mwezi watsopano, kapena za tsiku la Sabata.
Så låter nu ingen göra eder samvet öfver mat, eller dryck, eller öfver bestämda helgedagar, eller nymånader, eller Sabbather;
17 Zimenezi ndi chithunzithunzi chabe cha zinthu zimene zikubwera, koma choonadi chenicheni chikupezeka mwa Khristu.
Hvilket är skuggen af det som tillkommande var; men kroppen sjelf är i Christo.
18 Musalole kuti wina aliyense amene amakonda kudzichepetsa mwachiphamaso ndi kumapembedza angelo akulepheretseni kukalandira mphotho. Munthu woteroyu amayankhulanso mwatsatanetsatane zinthu zimene akuti anaziona mʼmasomphenya. Anthuwa ndi odzitukumula ndi fundo zopanda pake zochokera mʼmaganizo mwawo amene si auzimu.
Låter ingen taga eder lönen ifrå, den som vandrar efter egen godtycko i Änglaödmjukhet och andelighet, i de ting han aldrig sett hafver, och är förgäfves uppblåst i sitt köttsliga sinne;
19 Iwo sakulumikizananso ndi mutu, kumene kumachokera thupi lonse, logwirizidwa ndi kumangiriridwa pamodzi ndi mʼmitsempha yake ndi mnofu, limene limakula monga mmene Mulungu afunira kuti likulire.
Och håller sig icke vid hufvudet, af hvilko hele lekamenen genom leder och ledamot kraft får och tillsammans hänger, och tillväxer i den förökelse som Gud gifver.
20 Popeza munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nayo miyambo ya dziko lapansi lino, nʼchifukwa chiyani mukukhalanso ngati a dziko lapansi lino? Bwanji mukumvera malamulo monga awa:
Efter I nu döde ären med Christo, ifrå de verldsliga stadgar; hvi låten I eder då begripas med beskrefna stadgar, lika som I ännu lefden i verldene?
21 “Usagwire chakuti,” “Usalawe chakuti,” “Usakhudze chakuti?”
De der säga: Du skall icke komma vid det; icke smaka det; icke handtera det;
22 Malamulo amenewa amakhudza zinthu zimene zimatha zikamagwiritsidwa ntchito, ndipo malamulo ndi zophunzitsa za anthu chabe.
Hvilket dock allt förgås i brukningene, och är efter menniskors bud och lärdom;
23 Ndithu malamulo oterewa amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamulira anthu ambiri pa zachipembedzo ndi pa zakudzichepetsa kwa chiphamaso, ndi pa zakuzunza thupi lawo, koma alibe mphamvu zoletsa kuchita zofuna za thupilo.
Hvilke hafva väl ett sken af visdom, genom sjelftagen andelighet och ödmjukhet, och derigenom att de icke skona kroppen, och göra icke köttena dess äro till dess nödtorft.

< Akolose 2 >