< Akolose 2 >

1 Ndikufuna mudziwe kuti ndikukuvutikirani kwambiri, inuyo pamodzi ndi anzanu a ku Laodikaya, ndi ena onse amene sitinaonane maso ndi maso.
Sillä minä tahdon, että te tiedätte, kuinka suuri kilvoittelu minulla on teidän tähtenne ja laodikealaisten ja kaikkien tähden, jotka eivät ole minun ruumiillisia kasvojani nähneet,
2 Cholinga changa nʼchakuti alimbikitsidwe ndi kuyanjana pamodzi mʼchikondi, akhale odzaza ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndi kuti azindikire chinsinsi cha Mulungu, chimene ndi Khristu.
että heidän sydämensä, yhteenliittyneinä rakkaudessa, saisivat kehoitusta omistamaan täyden ymmärtämyksen koko rikkauden ja pääsisivät tuntemaan Jumalan salaisuuden, Kristuksen,
3 Mwa Iyeyu muli chuma chonse chobisidwa cha nzeru ndi chidziwitso.
jossa kaikki viisauden ja tiedon aarteet ovat kätkettyinä.
4 Ndikukuwuzani zimenezi kuti wina aliyense asakunamizeni ndi kukukopani ndi mawu ake.
Tämän minä sanon, ettei kukaan teitä pettäisi suostuttelevilla puheilla.
5 Pakuti ngakhale sindili pakati panu mʼthupi, ndili nanu pamodzi mu mzimu, ndipo ndikukondwa kuona kuti mukulongosola bwino zonse ndiponso kuti chikhulupiriro chanu mwa Khristu ndi chokhazikika ndithu.
Sillä jos ruumiillisesti olenkin poissa, olen kuitenkin teidän kanssanne hengessä ja iloitsen nähdessäni järjestyksen, joka teidän keskuudessanne vallitsee, ja teidän lujan uskonne Kristukseen.
6 Tsono popeza munavomereza Khristu Yesu kukhala Ambuye anu, mupitirire kukhala mwa Iyeyo.
Niinkuin te siis olette omaksenne ottaneet Kristuksen Jeesuksen, Herran, niin vaeltakaa hänessä,
7 Mukhale ozikika mizu mwa Iye, ndipo moyo wanu umangike pa Iye. Mulimbike mʼchikhulupiriro monga momwe munaphunzirira, ndipo kuyamika kwanu kusefukire.
juurtuneina häneen ja hänessä rakentuen ja uskossa vahvistuen, niinkuin teille on opetettu; ja olkoon teidän kiitoksenne ylitsevuotavainen.
8 Musalole kuti wina aliyense akutengeni ukapolo ndi mʼnzeru zachinyengo zolongosola zinthu zozama, zomwe zimachokera ku miyambo ya anthu ndi ku maganizo awo okhudza za dziko lapansi osati kwa Khristu.
Katsokaa, ettei kukaan saa teitä saaliikseen järkeisopilla ja tyhjällä petoksella, pitäytyen ihmisten perinnäissääntöihin ja maailman alkeisvoimiin eikä Kristukseen.
9 Pakuti mʼthupi la Khristu mumakhala umulungu wonse wathunthu.
Sillä hänessä asuu jumaluuden koko täyteys ruumiillisesti,
10 Ndipo inunso ndinu athunthu mwa Khristu. Iye ndiye mtsogoleri wa pamwamba pa maufumu onse ndi maulamuliro wonse.
ja te olette täytetyt hänessä, joka on kaiken hallituksen ja vallan pää,
11 Mwa Iye inunso munachita mdulidwe mʼthupi lanu, osati mdulidwe ochitidwa ndi manja a anthu ayi, koma ochitidwa ndi Khristu pamene anavula khalidwe lanu lauchimo lija.
ja hänessä te myös olette ympärileikatut, ette käsintehdyllä ympärileikkauksella, vaan lihan ruumiin poisriisumisella, Kristuksen ympärileikkauksella:
12 Mu ubatizo, munayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Khristu ndi kuukitsidwa naye pamodzi, pokhulupirira mphamvu za Mulungu amene anamuukitsa kwa akufa.
ollen haudattuina hänen kanssaan kasteessa, jossa te myös hänen kanssaan olette herätetyt uskon kautta, jonka vaikuttaa Jumala, joka herätti hänet kuolleista.
13 Pamene munali akufa chifukwa cha machimo anu ndi osachita mdulidwe mʼmitima mwanu, Mulungu anakupatsani moyo mwa Khristu. Iye anatikhululukira machimo athu onse.
Ja teidät, jotka olitte kuolleet rikoksiinne ja lihanne ympärileikkaamattomuuteen, teidät hän teki eläviksi yhdessä hänen kanssaan, antaen meille anteeksi kaikki rikokset,
14 Anafafaniza kalata ya ngongole yathu, pomwe panali milandu yotitsutsa ife. Iye anayichotsa, nayikhomera pa mtanda.
ja pyyhki pois sen kirjoituksen säädöksineen, joka oli meitä vastaan ja oli meidän vastustajamme; sen hän otti meidän tieltämme pois ja naulitsi ristiin.
15 Ndipo atalanda zida maufumu ndi maulamuliro, Iye anawachititsa manyazi powayendetsa pamaso pa anthu onse atawagonjetsa ndi mtanda.
Hän riisui aseet hallituksilta ja valloilta ja asetti heidät julkisen häpeän alaisiksi; hän sai heistä hänen kauttaan voiton riemun.
16 Nʼchifukwa chake musalole wina aliyense kukuzengani mlandu chifukwa cha zimene mumadya kapena kumwa, kapena za masiku achikondwerero cha chipembedzo, za chikondwerero cha mwezi watsopano, kapena za tsiku la Sabata.
Älköön siis kukaan teitä tuomitko syömisestä tai juomisesta, älköön myös minkään juhlan tai uudenkuun tai sapatin johdosta,
17 Zimenezi ndi chithunzithunzi chabe cha zinthu zimene zikubwera, koma choonadi chenicheni chikupezeka mwa Khristu.
jotka vain ovat tulevaisten varjo, mutta ruumis on Kristuksen.
18 Musalole kuti wina aliyense amene amakonda kudzichepetsa mwachiphamaso ndi kumapembedza angelo akulepheretseni kukalandira mphotho. Munthu woteroyu amayankhulanso mwatsatanetsatane zinthu zimene akuti anaziona mʼmasomphenya. Anthuwa ndi odzitukumula ndi fundo zopanda pake zochokera mʼmaganizo mwawo amene si auzimu.
Älköön teiltä riistäkö voittopalkintoanne kukaan, joka on mieltynyt nöyryyteen ja enkelien palvelemiseen ja pöyhkeilee näyistään ja on lihallisen mielensä turhaan paisuttama
19 Iwo sakulumikizananso ndi mutu, kumene kumachokera thupi lonse, logwirizidwa ndi kumangiriridwa pamodzi ndi mʼmitsempha yake ndi mnofu, limene limakula monga mmene Mulungu afunira kuti likulire.
eikä pitäydy häneen, joka on pää ja josta koko ruumis, nivelten ja jänteiden avulla koossa pysyen, kasvaa Jumalan antamaa kasvua.
20 Popeza munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nayo miyambo ya dziko lapansi lino, nʼchifukwa chiyani mukukhalanso ngati a dziko lapansi lino? Bwanji mukumvera malamulo monga awa:
Jos te olette Kristuksen kanssa kuolleet pois maailman alkeisvoimista, miksi te, ikäänkuin eläisitte maailmassa, sallitte määrätä itsellenne säädöksiä:
21 “Usagwire chakuti,” “Usalawe chakuti,” “Usakhudze chakuti?”
"Älä tartu, älä maista, älä koske!"
22 Malamulo amenewa amakhudza zinthu zimene zimatha zikamagwiritsidwa ntchito, ndipo malamulo ndi zophunzitsa za anthu chabe.
-sehän on kaikki tarkoitettu katoamaan käyttämisen kautta-ihmisten käskyjen ja oppien mukaan?
23 Ndithu malamulo oterewa amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamulira anthu ambiri pa zachipembedzo ndi pa zakudzichepetsa kwa chiphamaso, ndi pa zakuzunza thupi lawo, koma alibe mphamvu zoletsa kuchita zofuna za thupilo.
Tällä kaikella tosin on viisauden maine itsevalitun jumalanpalveluksen ja nöyryyden vuoksi ja sentähden, ettei se ruumista säästä; mutta se on ilman mitään arvoa, ja se tapahtuu lihan tyydyttämiseksi.

< Akolose 2 >