< Akolose 1 >

1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, ndi Timoteyo mʼbale wathu.
پولس به اراده خدا رسول مسیح عیسی وتیموتاوس برادر،۱
2 Kulembera abale oyera mtima ndi okhulupirira a ku Kolose mwa Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu.
به مقدسان در کولسی و برادران امین، در مسیح فیض و سلامتی از جانب پدر ما خداو عیسی مسیح خداوند بر شما باد.۲
3 Timayamika Mulungu Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu, nthawi zonse pamene tikukupemphererani.
خدا و پدر خداوند خود عیسی مسیح راشکر می‌کنیم و پیوسته برای شما دعا می‌نماییم،۳
4 Timayamika chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse.
چونکه ایمان شما را در مسیح عیسی و محبتی را که با جمیع مقدسان می‌نمایید شنیدیم،۴
5 Chikhulupiriro ndi chikondi, gwero lake ndi chiyembekezo chomwe muli nacho chodzalandira zimene anakusungirani kumwamba. Munamva kale za zimenezi kudzera mʼmawu a choonadi, Uthenga Wabwino
به‌سبب امیدی که بجهت شما در آسمان گذاشته شده است که خبر آن را در کلام راستی انجیل سابق شنیدید،۵
6 umene unafika kwa inu. Pa dziko lonse lapansi Uthenga Wabwino ukubereka chipatso ndi kukula monga momwe zakhala zikuchitikira pakati panu kuyambira tsiku limene munawumva ndi kuzindikira chisomo cha Mulungu mu choonadi chonse.
که به شما وارد شد چنانکه درتمامی عالم نیز و میوه می‌آورد و نمو می‌کند، چنانکه در میان شما نیز از روزی که آن را شنیدیدو فیض خدا را در راستی دانسته‌اید.۶
7 Inu munaphunzira zimenezi kuchokera kwa Epafra, mtumiki mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu mʼmalo mwathu.
چنانکه ازاپفراس تعلیم یافتید که همخدمت عزیز ما وخادم امین مسیح برای شما است.۷
8 Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.
و او ما را نیز ازمحبت شما که در روح است خبر داد.۸
9 Chifukwa cha ichi, kuyambira tsiku limene tinamva za inu, sitinasiye kukupemphererani ndi kumupempha Mulungu kuti akudzazeni ndi chidziwitso cha chifuniro chake kudzera mu nzeru yonse yauzimu ndi kumvetsetsa.
و از آن جهت ما نیز از روزی که این راشنیدیم، باز نمی ایستیم از دعا کردن برای شما ومسالت نمودن تا از کمال معرفت اراده او در هرحکمت و فهم روحانی پر شوید،۹
10 Ndipo tikupempherera zimenezi ndi cholinga chakuti inu mukhale moyo oyenera Ambuye ndi kumukondweretsa mʼnjira zonse. Kubereka chipatso pa ntchito iliyonse yabwino, ndi kukula mʼchidziwitso cha Mulungu.
تا شما به طریق شایسته خداوند به‌کمال رضامندی رفتارنمایید و در هر عمل نیکو بار آورید و به معرفت کامل خدا نمو کنید،۱۰
11 Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe
و به اندازه توانایی جلال او به قوت تمام زورآور شوید تا صبر کامل وتحمل را با شادمانی داشته باشید؛۱۱
12 ndi kuyamika Atate nthawi zonse, amene wakuyenerezani kuti mulandire nawo chuma cha oyera mtima mu ufumu wa kuwunika.
و پدر راشکر گزارید که ما را لایق بهره میراث مقدسان درنور گردانیده است،۱۲
13 Pakuti Iye anatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima ndi kutibweretsa mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa.
و ما را از قدرت ظلمت رهانیده، به ملکوت پسر محبت خود منتقل ساخت،۱۳
14 Mwa Iyeyu ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo.
که در وی فدیه خود یعنی آمرزش گناهان خویش را یافته‌ایم.۱۴
15 Mwanayu ndiye chithunzi cha Mulungu wosaonekayo. Iye ndiye Mwana wake woyamba kubadwa ndi wolamulira zolengedwa zonse.
و او صورت خدای نادیده است، نخست زاده تمامی آفریدگان.۱۵
16 Pakuti zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye. Zinthu zakumwamba ndi za pa dziko lapansi, zooneka ndi zosaoneka, maufumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu. Zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye ndipo anazilengera Iyeyo.
زیرا که در اوهمه‌چیز آفریده شد، آنچه در آسمان و آنچه برزمین است از چیزهای دیدنی و نادیدنی و تختهاو سلطنتها و ریاسات و قوات؛ همه بوسیله او وبرای او آفریده شد.۱۶
17 Iyeyo analipo zinthu zonse zisanalengedwe ndipo zinthu zonse zimamangika pamodzi mwa Iye.
و او قبل از همه است و دروی همه‌چیز قیام دارد.۱۷
18 Iye ndiyenso mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndiye chiyambi chake, woyamba kuuka kwa akufa, kuti Iyeyo akhale wopambana zonse.
و او بدن یعنی کلیسا راسر است، زیرا که او ابتدا است و نخست زاده ازمردگان تا در همه‌چیز او مقدم شود.۱۸
19 Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu.
زیرا خدارضا بدین داد که تمامی پری در او ساکن شود،۱۹
20 Ndipo kudzera mwa Iye Mulungu ayanjanitsenso zinthu zonse ndi Iye mwini, zinthu za pa dziko lapansi, kapena zinthu za kumwamba. Iye anachita mtendere kudzera mʼmagazi ake, wokhetsedwa pa mtanda.
و اینکه بوساطت او همه‌چیز را با خودمصالحه دهد، چونکه به خون صلیب وی سلامتی را پدید آورد. بلی بوسیله او خواه آنچه بر زمین وخواه آنچه در آسمان است.۲۰
21 Kale inu munali kutali ndi Mulungu ndipo munali adani a Mulungu mʼmaganizo mwanu chifukwa cha khalidwe lanu loyipa.
و شما را که سابق از نیت دل در اعمال بد خویش اجنبی و دشمن بودید، بالفعل مصالحه داده است،۲۱
22 Koma tsopano Iye anakuyanjanitsani mʼthupi la Khristu kudzera mu imfa kuti akuperekeni pamaso pake oyera, opanda banga ndi opanda chotsutsidwa nacho
در بدن بشری خود بوسیله موت تا شما را در حضورخود مقدس و بی‌عیب و بی‌ملامت حاضر سازد،۲۲
23 ngati mupitirirabe kukhala mʼchikhulupiriro chanu, okhazikika ndi olimba, osasunthidwa kuchoka pa chiyembekezo chimene munachigwira mu Uthenga Wabwino. Uwu ndi Uthenga Wabwino umene munawumva, umene wakhala ukulalikidwa kwa olengedwa onse a pansi pa thambo, ndi umenenso, ine Paulo ndinakhala mtumiki wake.
به شرطی که در ایمان بنیاد نهاده و قایم بمانیدو جنبش نخورید از امید انجیل که در آن تعلیم یافته‌اید و به تمامی خلقت زیر آسمان بدان موعظه شده است و من پولس خادم آن شده‌ام.۲۳
24 Tsopano ine ndikukondwa kuti ndinavutika chifukwa cha inu, ndipo ndikukwaniritsa mʼthupi langa zimene zikuperewera pa masautso a Khristu, chifukwa cha thupi lake, limene ndi Mpingo.
الان از زحمتهای خود در راه شما شادی می‌کنم و نقصهای زحمات مسیح را در بدن خودبه‌کمال می‌رسانم برای بدن او که کلیسا است،۲۴
25 Ine ndakhala mtumiki wake mwa lamulo limene Mulungu anandipatsa kuti ndipereke Mawu a Mulungu athunthu,
که من خادم آن گشته‌ام برحسب نظارت خداکه به من برای شما سپرده شد تا کلام خدا را به‌کمال رسانم؛۲۵
26 chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. (aiōn g165)
یعنی آن سری که از دهرها وقرنها مخفی داشته شده بود، لیکن الحال به مقدسان او مکشوف گردید، (aiōn g165)۲۶
27 Kwa iwo amene Mulungu anawasankha kuti awadziwitse pakati pa a mitundu ina, ulemerero wa chuma cha chinsinsi ichi, amene ndi Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero.
که خدا اراده نمودتا بشناساند که چیست دولت جلال این سر درمیان امت‌ها که آن مسیح در شما و امید جلال است.۲۷
28 Ife tikulalikira Khristu, kulangiza ndi kuphunzitsa aliyense mwa nzeru zonse kuti timupereke aliyense wangwiro mwa Khristu.
و ما او را اعلان می‌نماییم، در حالتیکه هر شخص را تنبیه می‌کنیم و هر کس را به هرحکمت تعلیم می‌دهیم تا هرکس را کامل درمسیح عیسی حاضر سازیم.۲۸
29 Ndi cholinga chimenechi, ine ndikugwira ntchito molimbika ndi mwamphamvu zonse zimene Iye anachita mwa ine.
و برای این نیزمحنت می‌کشم و مجاهده می‌نمایم بحسب عمل او که در من به قوت عمل می‌کند.۲۹

< Akolose 1 >