< Amosi 9 >

1 Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati: “Kantha mitu ya nsanamira kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke. Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse, onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe, palibe amene adzapulumuke.
Je vis le Seigneur debout sur l'autel; et Il dit: Frappe le chapiteau à faire trembler les seuils, et fais-en tomber les pièces sur la tête d'eux tous! et par l'épée je tuerai les survivants; aucun d'eux ne pourra échapper par la fuite, ni aucun d'eux se sauver.
2 Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol h7585)
S'ils forcent les Enfers, de là ma main les tirera; et s'ils montent dans les Cieux, je les en précipiterai; (Sheol h7585)
3 Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli, Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira. Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu, ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
s'ils se cachent à la cime du Carmel, je saurai les y surprendre et les y saisir, et s'ils vont se dérober à mes regards au fond de la mer, de là j'ordonnerai au serpent de les blesser;
4 Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo, ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko. Ndidzawayangʼanitsitsa kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
et s'ils marchent captifs en avant de leurs ennemis, de là j'ordonnerai à l'épée de les tuer, et je tournerai mes regards sur eux, non pour leur bien, mais pour leur malheur.
5 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka, onse amene amakhala mʼmenemo amalira. Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo, kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
C'est le Seigneur, l'Éternel des armées, qui touche la terre et elle se dissout, et tous ses habitants sont dans le deuil, et elle se soulève tout entière comme le fleuve, et s'affaisse comme le fleuve d'Egypte;
6 Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba, ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi, Iye amene amayitana madzi a ku nyanja ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova.
c'est lui qui élève dans les Cieux ses hautes salles et fait poser ses voûtes sur la terre, qui appelle les eaux de la mer et les verse sur la face de la terre. L'Éternel est son nom.
7 “Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli chimodzimodzi ndi Akusi?” Akutero Yehova. “Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto, Afilisti ku Kafitori ndi Aaramu ku Kiri?
N'êtes-vous pas pour moi ce que me sont les Éthiopiens, enfants d'Israël? dit l'Éternel. N'ai-je pas tiré Israël de la terre d'Égypte, et les Philistins de Caphthor, et les Syriens de Kir?
8 “Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wochimwawu. Ndidzawufafaniza pa dziko lapansi. Komabe sindidzawononga kotheratu nyumba ya Yakobo,” akutero Yehova.
Voici, les yeux du Seigneur Éternel sont sur le royaume criminel, et je le ferai disparaître de la surface de la terre; seulement ne détruirai-je pas toute la maison de Jacob, dit l'Éternel.
9 “Pakuti ndidzalamula, ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli pakati pa mitundu yonse ya anthu monga momwe amasefera ufa mʼsefa, koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
Car voici, je vais en donner l'ordre et agiter la maison d'Israël entre toutes les nations, comme on agite avec le crible; mais le grain ne tombera pas à terre. Ils mourront par l'épée,
10 Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga adzaphedwa ndi lupanga, onse amene amanena kuti, ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’
tous les pécheurs de mon peuple qui disent: La calamité ne nous atteindra pas et ne nous assaillira pas.
11 “Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso monga inalili poyamba,
Je veux dans ce même temps relever la hutte déchue de David, refermer ses brèches, et réparer ses ruines, et l'édifier comme aux jours d'autrefois,
12 kuti adzatengenso otsala a Edomu ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,” akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.
afin qu'ils fassent la conquête des restes d'Édom et de tous les peuples qui porteront mon nom; ainsi parle l'Éternel qui le fera.
13 Yehova akunena kuti “Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu. Mapiri adzachucha vinyo watsopano ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
Voici viennent des jours, dit l'Éternel, où le laboureur se rapprochera du moissonneur, et celui qui foule le raisin de celui qui répand la semence; et les montagnes seront découlantes de moût et toutes les collines ruisselantes.
14 Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli; mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo. Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake; adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
Et je ramènerai les captifs de mon peuple d'Israël, et ils rebâtiront les villes dévastées et les habiteront, et ils planteront des vignes et en boiront le vin, et ils établiront des jardins et en mangeront les fruits.
15 Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo, ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko limene Ine ndawapatsa,” akutero Yehova Mulungu wako.
Et je les replanterai dans leur sol, afin qu'ils ne soient plus arrachés de leur sol que je leur ai donné, dit l'Éternel, ton Dieu.

< Amosi 9 >