< Amosi 2 >

1 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
Ovako veli Gospod: za tri zla i za èetiri što uèini Moav, neæu mu oprostiti, jer sažeže kosti cara Edomskoga u kreè.
2 Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
Nego æu pustiti oganj na Moava, te æe proždrijeti dvorove u Kariotu, i Moav æe poginuti s vrevom, s vikom i s glasom trubnijem.
3 Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
I istrijebiæu sudiju iz njega i sve knezove njegove pobiæu s njim, veli Gospod.
4 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
Ovako veli Gospod: za tri zla i za èetiri što uèini Juda, neæu mu oprostiti, jer prezreše zakon Gospodnji i uredaba njegovijeh ne držaše, i prevariše se lažima svojim, za kojima hodiše oci njihovi.
5 Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
Nego æu pustiti oganj u Judu, te æe proždrijeti dvore Jerusalimske.
6 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
Ovako veli Gospod: za tri zla i za èetiri što uèini Izrailj, neæu mu oprostiti, jer prodavaše pravednika za novce i ubogoga za jedne opanke.
7 Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
Èeznu za prahom zemaljskim na glavi siromasima, i prevraæaju put smjernima; i sin i otac odlaze k jednoj djevojci da skvrne sveto ime moje.
8 Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
I na haljinama u zalogu uzetijem leže kod svakoga oltara, i vino oglobljenijeh piju u kuæi bogova svojih.
9 “Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
A ja istrijebih ispred njih Amoreje, koji bijahu visoki kao kedri i jaki kao hrastovi, i potrh rod njihov ozgo i žile njihove ozdo.
10 “Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
I ja vas izvedoh iz zemlje Misirske, i vodih vas po pustinji èetrdeset godina da biste naslijedili zemlju Amorejsku.
11 Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
I podizah izmeðu sinova vaših proroke i izmeðu mladiæa vaših nazireje. Nije li tako? sinovi Izrailjevi, govori Gospod.
12 “Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
A vi pojiste nazireje vinom, i prorocima zabranjivaste govoreæi: ne prorokujte.
13 “Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
Evo, ja æu vas pritisnuti na mjestu vašem kao što se pritiskuju kola puna snoplja.
14 Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
I neæe biti bijega brzomu, i jaki neæe utvrditi krjeposti svoje, i hrabri neæe spasti duše svoje.
15 Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
I strijelac neæe se održati, i laki na nogu neæe se izbaviti, niti æe konjik spasti duše svoje.
16 Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.
Nego æe najhrabriji meðu junacima go pobjeæi u onaj dan, govori Gospod.

< Amosi 2 >