< 2 Samueli 5 >

1 Mafuko onse a Israeli anabwera kwa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife mafupa ndi mnofu wanu.
Tada doðoše sva plemena Izrailjeva k Davidu u Hevron, i rekoše mu govoreæi: evo, mi smo kost tvoja i tijelo tvoje.
2 Kale lija, pamene Sauli anali mfumu yathu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova anakuwuzani kuti, ‘Udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
I prije, dok Saul bijaše car nad nama, ti si odvodio i dovodio Izrailja; i Gospod ti je rekao: ti æeš pasti narod moj Izrailja i ti æeš biti voð Izrailju.
3 Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, mfumu inachita nawo pangano ku Hebroni pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli.
Tako doðoše sve starješine Izrailjeve k caru u Hevron, i uèini s njima car David vjeru u Hevronu pred Gospodom; i pomazaše Davida za cara nad Izrailjem.
4 Davide anali ndi zaka makumi atatu pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka makumi anayi.
Trideset godina bijaše Davidu kad se zacari, i carova èetrdeset godina.
5 Analamulira Yuda ali ku Hebroni kwa zaka zisanu ndi ziwiri ndi miyezi isanu ndi umodzi, ndipo ali ku Yerusalemu analamulira Israeli yense ndi Yuda kwa zaka 33.
U Hevronu carova nad Judom sedam godina i šest mjeseca; a u Jerusalimu carova trideset i tri godine nad svijem Izrailjem i Judom.
6 Mfumu ndi ankhondo ake anapita ku Yerusalemu kukathira nkhondo Ayebusi amene ankakhala kumeneko. Ayebusiwo anamuwuza Davide kuti, “Inu simulowa muno. Ngakhale osaona ndi olumala akhoza kukuthamangitsani.” Iwo ankaganiza kuti, “Davide sangathe kulowa momwemo.”
A car otide sa svojim ljudima u Jerusalim na Jevuseje, koji življahu u onoj zemlji. I oni rekoše Davidu govoreæi: neæeš uæi ovamo dok ne uzmeš slijepe i hrome, hoteæi kazati: neæe uæi ovamo David.
7 Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
Ali David uze kulu Sion, to je grad Davidov.
8 Pa tsiku limenelo Davide anati, “Aliyense wogonjetsa Ayebusi ayenera kudzera mʼngalande ya madzi kuti akafike kwa iwo amene ndi ‘olumala ndi osaona,’ amene ndi adani a Davide.” Nʼchifukwa chake amanena kuti, “Olumala ndi osaona sadzalowa mʼnyumba yaufumu.”
Jer reèe David u onaj dan: ko god pobije Jevuseje i doðe do jaza, i do slijepijeh i hromijeh, na koje mrzi duša Davidova, biæe vojvoda. Zato se kaže: slijepi i hromi da ne ulaze u ovu kuæu.
9 Tsono Davide anakhazikika mu lingamo ndipo mzindawu anawutcha, Mzinda wa Davide. Iye anamanga malo onse ozungulira kuyambira ku matsitso ozungulira khoma.
I sjede David u kuli, i nazva je gradom Davidovijem: i pogradi je David unaokolo od Milona i unutra.
10 Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
I David jednako napredovaše, jer Gospod Bog nad vojskama bješe s njim.
11 Tsono Hiramu mfumu ya Turo inatumiza amithenga ake kwa Davide, pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndi amisiri a matabwa ndi amisiri a miyala, ndipo anamumangira Davide nyumba yaufumu.
I Hiram car Tirski posla poslanike k Davidu, i kedrovijeh drva i drvodjelja i kamenara, i sagradiše kuæu Davidu.
12 Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
I razumje David da ga je Gospod utvrdio za cara nad Izrailjem, i da je uzvisio carstvo njegovo radi naroda svojega Izrailja.
13 Davide atafika ku Yerusalemu kuchokera ku Hebroni, anakwatira azikazi natenganso akazi ena kumeneko, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
I uze David još inoèa i žena iz Jerusalima, pošto doðe iz Hevrona; i rodi se Davidu još sinova i kæeri.
14 Mayina a ana amene anabereka ku Yerusalemu ndi awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
I ovo su imena onijeh koji mu se rodiše u Jerusalimu: Samuja i Sovav i Natan i Solomun,
15 Ibihari, Elisua, Nefegi, Yafiya,
I Jevar i Elisuja i Nafig i Jafija,
16 Elisama, Eliada ndi Elifeleti.
I Elisama i Elijada i Elifalet.
17 Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anakalowa mu linga.
A Filisteji èuvši da su pomazali Davida za cara nad Izrailjem, izidoše svi Filisteji da traže Davida; a David èuvši to, otide u kulu.
18 Ndipo Afilisti anabwera ndi kukhala momwazika mʼChigwa cha Refaimu.
I Filisteji došavši raširiše se po dolini Rafajskoj.
19 Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka ndithu mʼmanja mwako.”
Tada David upita Gospoda govoreæi: hoæu li izaæi na Filisteje? Hoæeš li ih dati u moje ruke? A Gospod reèe Davidu: izaði; doista æu dati Filisteje u tvoje ruke.
20 Choncho Davide anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Yehova waphwanya adani anga ine ndikuona.” Choncho anawatcha malowa Baala Perazimu.
Tada David doðe u Val-Ferasim, i pobi ih ondje, i reèe: prodrije Gospod neprijatelje moje preda mnom kao kad voda prodire. Otuda se prozva ono mjesto Val-Ferasim.
21 Afilisti anasiya mafano awo kumeneko ndipo Davide ndi ankhondo ake anawatenga.
I ostaviše ondje lažne bogove svoje; a David i ljudi njegovi odnesoše ih.
22 Nthawi inanso Afilisti anabweranso namwazikana mʼChigwa cha Refaimu;
I opet nanovo doðoše Filisteji, i raširiše se u dolini Rafajskoj.
23 Davide anafunsa Yehova ndipo Yehovayo anayankha kuti, “Usapite molunjika koma uzungulire kumbuyo kwawo ndipo ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
I David upita Gospoda, koji reèe: ne idi pred njih, nego im zaði za leða, pa udari na njih prema dudovima.
24 Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukayende mofulumira, chifukwa izi zikasonyeza kuti Yehova ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
Pa kad èuješ da zašušti po vrhovima od dudova, onda se kreni, jer æe onda poæi Gospod pred tobom da pobije vojsku Filistejsku.
25 Kotero Davide anachita zimene Yehova anamulamulira ndipo anakantha Afilisti njira yonse kuchokera ku Geba mpaka ku Gezeri.
I David uèini tako kako mu zapovjedi Gospod, i pobi Filisteje od Gavaje do Gezera.

< 2 Samueli 5 >