< 2 Samueli 23 >

1 Nawa mawu otsiriza a Davide: “Mawu a Davide mwana wa Yese, mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba, munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo, woyimba nyimbo za Israeli:
A ovo su pošljednje rijeèi Davidove: Reèe David sin Jesejev, reèe èovjek koji bi postavljen visoko, pomazanik Boga Jakovljeva, i ljubak u pjesmama Izrailjevim:
2 “Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine; mawu ake anali pakamwa panga.
Duh Gospodnji govori preko mene, i besjeda njegova bi na mojem jeziku.
3 Mulungu wa Israeli anayankhula, Thanthwe la Israeli linati kwa ine: ‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo, pamene alamulira moopa Mulungu,
Reèe Bog Izrailjev, kaza mi stijena Izrailjeva: koji vlada ljudima neka je pravedan, vladajuæi u strahu Božijem;
4 amakhala ngati kuwala kwa mmamawa, mmawa wopanda mitambo, monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa imene imameretsa udzu mʼnthaka.’
I biæe kao svjetlost jutrenja, kad sunce izlazi jutrom bez oblaka, i kao trava koja raste iz zemlje od svjetlosti iza dažda.
5 “Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu? Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine, lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse? Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa, ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
Ako i nije taki dom moj pred Bogom, ipak je uèinio zavjet vjeèan sa mnom, u svemu dobro ureðen i utvrðen. I to je sve spasenje moje i sva želja moja, ako i ne da da raste.
6 Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga, imene sitengedwa ndi manja.
A bezakonici æe svikoliki biti kao trnje poèupani, koje se ne hvata rukom.
7 Aliyense amene wayikhudza mingayo amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo; nayitentha pa moto.”
Nego ko hoæe da ga se dohvati, uzme gvožðe ili kopljaèu; i sažiže se ognjem na mjestu.
8 Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.
Ovo su imena junaka Davidovijeh: Josev-Vasevet Tahmonac prvi izmeðu trojice; njemu milina bi udariti s kopljem na osam stotina, i pobi ih ujedanput.
9 Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo.
Za njim Eleazar sin Dodona sina Ahohova, izmeðu tri junaka koji bijahu s Davidom, i osramotiše Filisteje skupljene na boj, kad Izrailjci otidoše;
10 Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.
On se podiže, i bi Filisteje dokle mu se ruka ne umori i ukoèi se pri maèu; i Gospod dade veliko spasenje onaj dan, te se narod vrati za njim samo da pokupi plijen.
11 Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo.
A za njim Sama sin Agejev Araranin; kad se Filisteji skupiše u gomilu, i ondje bješe njiva puna leæa, i narod pobježe od Filisteja,
12 Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
Stade usred njive, i odbrani je, i pobi Filisteje, i Bog dade veliko spasenje.
13 Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
I ta tri prva izmeðu trideset siðoše i doðoše o žetvi k Davidu u peæinu Odolamsku, kad vojska Filistejska stajaše u okolu u dolini Rafajskoj.
14 Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
A David bijaše onda u gradu, i bješe onda straža Filistejska u Vitlejemu.
15 Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
A David zaželje, i reèe: ko bi mi donio vode da pijem iz studenca Vitlejemskoga što je kod vrata!
16 Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
Tada ona tri junaka prodriješe kroz oko Filistejski, i zahvatiše vode iz studenca Vitlejemskoga što je kod vrata, i donesoše i dadoše Davidu; ali on je ne htje piti, nego je proli pred Gospodom;
17 Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
I reèe: ne daj Bože da bih to uèinio. Nije li to krv ovijeh ljudi, koji ne mareæi za život svoj idoše. I ne htje piti. To uèiniše ova tri junaka.
18 Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
I Avisaj brat Joavov sin Serujin bješe prvi izmeðu trojice; on mahnu kopljem svojim na tri stotine, i pobi ih, i proslavi se meðu trojicom.
19 Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
Izmeðu te trojice bješe najslavniji, i posta im poglavar; ali one trojice ne stiže.
20 Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
I Venaja sin Jodajev, sin èovjeka junaka, velik djelima, iz Kavseila; on pogubi dva junaka Moavska, i sišav ubi lava u jami kad bješe snijeg.
21 Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
On ubi i jednoga Misirca, znatna èovjeka; imaše Misirac koplje u ruci, a on izide na nj sa štapom, i istrže Misircu koplje iz ruke, i ubi ga njegovijem kopljem.
22 Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
To uèini Venaja sin Jodajev, i bi slavan meðu ova tri junaka.
23 Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
Bješe najslavniji izmeðu tridesetorice, ali one trojice ne stiže; i David ga postavi nad pratiocima svojim.
24 Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
Asailo brat Joavov bješe meðu tridesetoricom, a to bjehu: Elhanan sin Dodonov iz Vitlejema,
25 Sama Mharodi, Elika Mherodi,
Sama Aroðanin, Elika Aroðanin.
26 Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,
Helis Falæanin, Ira sin Ikisov Tekojanin,
27 Abiezeri wa ku Anatoti, Sibekai Mhusati,
Avijezer Anatoæanin, Mevunej Husaæanin,
28 Zalimoni Mwahohi, Maharai Mnetofa,
Salmon Ahošanin, Maraj Netofaæanin,
29 Heledi mwana wa Baana Mnetofa, Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,
Helev sin Vanin Netofaæanin, Itaj sin Rivejev iz Gavaje sinova Venijaminovih,
30 Benaya Mpiratoni, Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.
Venaja Piratonjanin, Idaj iz doline Gasa.
31 Abi-Aliboni Mwaribati, Azimaveti Mbarihumi,
Avi-Alvon Arvaæanin, Azmavet Varumljanin,
32 Eliyahiba Msaaliboni, ana a Yaseni, Yonatani,
Elijava Salvonjanin, Jonatan od sinova Jasinovih,
33 mwana wa Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,
Sama Araranin, Ahijam sin Sararov Araranin,
34 Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati, Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,
Elifelet, sin Asveja Mahaæanina, Elijam sin Ahitofela Gilonjanina,
35 Heziro wa ku Karimeli, Paarai Mwaribi,
Esraj Karmilac, Farej Arvljanin,
36 Igala mwana wa Natani wa ku Zoba, mwana wa Hagiri,
Igal sin Natanov iz Sove, Vanija od Gada,
37 Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,
Selek Amonac, Naraj Viroæanin, koji nošaše oružje Joavu sinu Serujinu,
38 Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
Ira Jetranin, Gariv Jetranin,
39 ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37.
Urija Hetejin; svega trideset i sedam.

< 2 Samueli 23 >