< 2 Samueli 22 >

1 Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
Locutus est autem David Domino verba carminis huius, in die qua liberavit eum Dominus de manu omnium inimicorum suorum, et de manu Saul,
2 Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
et ait: Dominus petra mea, et robur meum, et salvator meus.
3 Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Deus fortis meus sperabo in eum: scutum meum, et cornu salutis meæ: elevator meus, et refugium meum: salvator meus, de iniquitate liberabis me.
4 “Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
Laudabilem invocabo Dominum: et ab inimicis meis salvus ero.
5 “Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
Quia circumdederunt me contritiones mortis: torrentes Belial terruerunt me.
6 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
Funes inferni circumdederunt me: prævenerunt me laquei mortis. (Sheol h7585)
7 “Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
In tribulatione mea invocabo Dominum, et ad Deum meum clamabo: et exaudiet de templo suo vocem meam, et clamor meus venit ad aures eius.
8 “Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Commota est et contremuit terra: fundamenta montium concussa sunt, et conquassata, quoniam iratus est eis.
9 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
Ascendit fumus de naribus eius, et ignis de ore eius vorabit: carbones succensi sunt ab eo.
10 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
Inclinavit cælos, et descendit: et caligo sub pedibus eius.
11 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
Et ascendit super cherubim, et volavit: et lapsus est super pennas venti.
12 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
Posuit tenebras in circuitu suo latibulum: cribrans aquas de nubibus cælorum.
13 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
Præ fulgore in conspectu eius, succensi sunt carbones ignis.
14 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
Tonabit de cælo Dominus: et Excelsus dabit vocem suam.
15 Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
Misit sagittas et dissipavit eos: fulgur, et consumpsit eos.
16 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
Et apparuerunt effusiones maris, et revelata sunt fundamenta orbis ab increpatione Domini, ab inspiratione spiritus furoris eius.
17 “Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
Misit de excelso, et assumpsit me: et extraxit me de aquis multis.
18 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
Liberavit me ab inimico meo potentissimo, et ab his qui oderant me: quoniam robustiores me erant.
19 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
Prævenit me in die afflictionis meæ, et factus est Dominus firmamentum meum.
20 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
Et eduxit me in latitudinem: liberavit me, quia complacui ei.
21 “Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
Retribuet mihi Dominus secundum iustitiam meam: et secundum munditiam manuum mearum reddet mihi.
22 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
Quia custodivi vias Domini, et non egi impie, a Deo meo.
23 Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
Omnia enim iudicia eius in conspectu meo: et præcepta eius non amovi a me.
24 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
Et ero perfectus cum eo: et custodiam me ab iniquitate mea.
25 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
Et restituet mihi Dominus secundum iustitiam meam: et secundum munditiam manuum mearum, in conspectu oculorum suorum.
26 “Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
Cum sancto sanctus eris: et cum robusto perfectus.
27 Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
Cum electo electus eris: et cum perverso perverteris.
28 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
Et populum pauperem salvum facies: oculisque tuis excelsos humiliabis.
29 Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
Quia tu lucerna mea Domine: et tu Domine illuminabis tenebras meas.
30 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
In te enim curram accinctus: in Deo meo transiliam murum.
31 “Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
Deus, immaculata via eius, eloquium Domini igne examinatum: scutum est omnium sperantium in se.
32 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
Quis est Deus præter Dominum: et quis fortis præter Deum nostrum?
33 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
Deus qui accinxit me fortitudine: et complanavit perfectam viam meam.
34 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
Coæquans pedes meos cervis, et super excelsa mea statuens me.
35 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
Docens manus meas ad prælium, et componens quasi arcum æreum brachia mea.
36 Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
Dedisti mihi clypeum salutis tuæ: et mansuetudo tua multiplicavit me.
37 Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
Dilatabis gressus meos subtus me: et non deficient tali mei.
38 “Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
Persequar inimicos meos, et conteram: et non convertar donec consumam eos.
39 Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
Consumam eos et confringam, ut non consurgant: cadent sub pedibus meis.
40 Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
Accinxisti me fortitudine ad prælium: incurvasti resistentes mihi subtus me.
41 Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
Inimicos meos dedisti mihi dorsum: odientes me, et disperdam eos.
42 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
Clamabunt, et non erit qui salvet, ad Dominum, et non exaudiet eos.
43 Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Delebo eos ut pulverem terræ: quasi lutum platearum comminuam eos atque confringam.
44 “Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Salvabis me a contradictionibus populi mei: custodies me in caput Gentium: populus, quem ignoro, serviet mihi.
45 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
Filii alieni resistent mihi, auditu auris obedient mihi.
46 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
Filii alieni defluxerunt, et contrahentur in angustiis suis.
47 “Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
Vivit Dominus, et benedictus Deus meus: et exaltabitur Deus fortis salutis meæ.
48 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
Deus qui das vindictas mihi, et deiicis populos sub me.
49 amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Qui educis me ab inimicis meis, et a resistentibus mihi elevas me: a viro iniquo liberabis me:
50 Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Propterea confitebor tibi Domine in gentibus: et nomini tuo cantabo.
51 “Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”
Magnificans salutes regis sui, et faciens misericordiam Christo suo David, et semini eius in sempiternum.

< 2 Samueli 22 >