< 2 Samueli 22 >

1 Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
And David spoke to the Lord the words of this song, in the day in which the Lord rescued him out of the hand of all his enemies, and out of the hand of Saul.
2 Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
And the song was thus: O Lord, my rock, and my fortress, and my deliverer,
3 Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
my God; he shall be to me my guard, I will trust in him: [he is] my protector, and the horn of my salvation, my helper, and my sure refuge; you shall save me from the unjust man.
4 “Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
I will call upon the Lord who is worthy to be praised, and I shall be saved from my enemies.
5 “Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
For the troubles of death compassed me, the floods of iniquity amazed me:
6 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
the pangs of death surrounded me, the agonies of death prevented me. (Sheol h7585)
7 “Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
When I am afflicted I will call upon the Lord, and will cry to my God, and he shall hear my voice out of his temple, and my cry shall come into his ears.
8 “Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
And the earth was troubled and quaked, and the foundations of heaven were confounded and torn asunder, because the Lord was angry with them.
9 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
There went up a smoke in his wrath, and fire out of his mouth devours: coals were kindled at it.
10 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
And he bowed the heavens, and came down, and [there was] darkness under his feet.
11 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
And he rode upon the cherubs and did fly, and was seen upon the wings of the wind.
12 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
And he made darkness his hiding-place; his tabernacle round about him was the darkness of waters, he condensed it with the clouds of the air.
13 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
At the brightness before him coals of fire were kindled.
14 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
The Lord thundered out of heaven, and the Most High uttered his voice.
15 Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
And he sent forth arrows, and scattered them, and he flashed lightning, and dismayed them.
16 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
And the channels of the sea were seen, and the foundations of the world were discovered, at the rebuke of the Lord, at the blast of the breath of his anger.
17 “Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
He sent from above and took me; he drew me out of many waters.
18 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
He delivered me from my strong enemies, from them that hated me, for they were stronger than I.
19 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
The days of my affliction prevented me; but the Lord was my stay.
20 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
And he brought me into a wide place, and rescued me, because he delighted in me.
21 “Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
And the Lord recompensed me according to my righteousness; even according to the purity of my hands did he recompense me.
22 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
Because, I kept the ways of the Lord, and did not wickedly depart from my God.
23 Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
For all his judgements and his ordinances [were] before me: I departed not from them.
24 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
And I shall be blameless before him, and will keep myself from my iniquity.
25 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
And the Lord will recompense me according to my righteousness, and according to the purity of my hands in his eye-sight.
26 “Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
With the holy you will be holy, and with the perfect man you will be perfect,
27 Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
and with the excellent you will be excellent, and with the froward you will be froward.
28 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
And you will save the poor people, and will bring down the eyes of the haughty.
29 Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
For you, Lord, [are] my lamp, and the Lord shall shine forth to me in my darkness.
30 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
For by you shall I run [as] a girded man, and by my God shall I leap over a wall.
31 “Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
As for the Mighty One, his way [is] blameless: the word of the Lord [is] strong [and] tried in the fire: he is a protector to all that put their trust in him.
32 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
Who [is] strong, but the Lord? and who will be a Creator except our God?
33 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
[It is] the Mighty One who strengthens me with might, and has prepared my way without fault.
34 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
He makes my feet like hart's feet, and sets me upon the high places.
35 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
He teaches my hands to war, and has broken a brazen bow by my arm.
36 Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
And you have given me the shield of my salvation, and your propitious dealing has increased me,
37 Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
so as to make room under me for my going, and my legs did not totter.
38 “Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
I will pursue my enemies, and will utterly destroy them; and I will not turn again till I have consumed them.
39 Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
And I will crush them, and they shall not rise; and they shall fall under my feet.
40 Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
And you shall strengthen me with power for the war; you shall cause them that rise up against me to bow down under me.
41 Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
And you have caused mine enemies to flee before me, even them that hated me, and you have slain them.
42 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
They shall cry, and there shall be no helper; to the Lord, but he hearkens not to them.
43 Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
And I ground them as the dust of the earth, I beat them small as the mire of the streets.
44 “Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
And you shall deliver me from the striving of the peoples, you shall keep me [to be] the head of the Gentiles: a people which I knew not served me.
45 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
The strange children feigned [obedience] to me; they listened to me as soon as they heard.
46 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
The strange children shall be cast away, and shall be overthrown out of their hiding places.
47 “Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
The Lord lives, and blessed [be] my guardian, and my God, my strong keeper, shall be exalted.
48 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
The Lord who avenges me [is] strong, chastening the nations under me,
49 amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
and bringing me out from my enemies: and you shall set me on high from amongst those that rise up against me: you shall deliver me from the violent man.
50 Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Therefore will I confess to you, O Lord, amongst the Gentiles, and sing to your name.
51 “Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”
He magnifies the salvation of his king, and works mercy for his anointed, even for David and for his seed for ever.

< 2 Samueli 22 >