< 2 Samueli 20 >

1 Ndipo munthu wina wokonda kuyambitsa chisokonezo, dzina lake Seba, mwana wa Bikiri wa fuko la Benjamini, anali komweko. Iye analiza lipenga ndipo anafuwula kuti, “Ife tilibe chathu mu mfumu wa Davide, tilibe gawo mwa mwana wa Yese! Inu Aisraeli aliyense apite ku nyumba kwake!”
Also it bifelde, that a man of Belial was there, Siba bi name, the sone of Bothri, a man of the generacioun of Gemyny; and he sownede with a clarioun, and seide, No part is to vs in Dauid, nether eritage in the sone of Ysai; thou, Israel, turne ayen in to thi tabernaclis.
2 Kotero Aisraeli onse anamuthawa Davide ndipo anatsatira Seba mwana wa Bikiri. Koma anthu a ku Yuda anakhala ndi mfumu yawo njira yonse kuchokera ku Yorodani mpaka ku Yerusalemu.
And al Israel was departid fro Dauid, and suede Siba, the sone of Bothri; forsothe the men of Juda cleuyden to her kyng, fro Jordan `til to Jerusalem.
3 Davide atabwerera ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu, iye anatenga azikazi khumi aja amene anawasiya kuti aziyangʼanira nyumba yaufumu, ndipo anawayika mʼnyumba imene anayikapo mlonda. Iye ankawadyetsa koma sanagone nawonso. Anasungidwa kwa okha mpaka tsiku la kufa kwawo ndipo anakhala ngati akazi amasiye.
And whanne the kyng hadde come in to his hows in Jerusalem, he took ten wymmen, hise secundarie wyues, whiche he hadde left to kepe the hous, and he bitook hem in to keping, and yaf mete to hem; and he entride not to hem; but thei weren closid `til to the dai of her deeth, and lyueden in widewehed.
4 Kenaka mfumu inati kwa Amasa, “Itanitsa ankhondo a Yuda kuti abwere kwa ine pasanathe masiku atatu, ndipo iwe udzakhale nawo.”
Forsothe Dauid seide to Amasa, Clepe thou to gidere to me alle the men of Juda in to the thridde dai, and be thou present.
5 Motero Amasa anakayitana Ayuda, koma anachedwa, napitirira pa nthawi imene mfumu inamuyikira.
Therfor Amasa yede, that he clepe to gidere the puple of Juda; and he dwellide ouer the couenaunt, which the kyng hadde set to hym.
6 Davide anati kwa Abisai, “Tsono Seba mwana wa Bikiri adzatipweteka kuposa momwe Abisalomu anatichitira. Tenga asilikali a mbuye wako ndipo umuthamangitse, mwina adzapeza mizinda yotetezedwa ndi kutithawa ife.”
Sotheli Dauid seide to Abisai, Now Siba, the sone of Botri, schal turmente vs more than Absolon dide; therfor take the seruauntis of thi lord, and pursue hym, lest in hap he fynde strengthid citees, and ascape vs.
7 Kotero anthu a Yowabu, Akereti ndi Apeleti ndiponso asilikali onse amphamvu anapita motsogozedwa ndi Abisai. Iwo anayenda kuchokera ku Yerusalemu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
Therfor the men of Joab yeden out with Abisai, and Cerethi and Ferethi, and alle stronge men yeden out of Jerusalem to pursue Siba, the sone of Bochry.
8 Ali pa mwala waukulu wa ku Gibiyoni, Amasa anabwera kudzakumana nawo. Yowabu anali atavala chovala chausilikali ndipo pamwamba pa malayawo, mʼchiwuno mwake anavala lamba womangirirapo lupanga lili moyikamo mwakemo. Akuyenda linasololoka kuchoka moyikamo mwake.
And whanne thei weren bisidis the greet stoon, which is in Gabaon, Amasa cam, and ran to hem; forsothe Joab was clothid with a streit coote at the mesure of his abit, and was gird aboue with a swerd, `ether dagger, hangynge doun `til to the entrayls in a schethe, `which swerd maad `craftily myyte go out bi liyt touchyng, and smyte. Therfor Joab seide to Amasa,
9 Yowabu anati kwa Amasa, “Kodi uli bwanji mʼbale wanga?” Kenaka Yowabu anamugwira ndevu Amasa uja ndi dzanja lake lamanja ndi kupsompsona.
Heil, my brother! And he helde with the riyt hond the chyn of Amasa, as kissinge him.
10 Amasa sanayangʼanitsitse lupanga limene linali mʼdzanja la Yowabu, ndipo Yowabu anamubaya nalo mʼmimba ndipo matumbo ake anatuluka ndi kugwera pansi. Popanda kubayanso kachiwiri, Amasa anafa. Ndipo Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anathamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
Forsothe Amasa took not kepe of the swerd, `which swerd Joab hadde, and Joab smoot Amasa in the side, and schedde out his entrailis in to the erthe, and Amasa was deed; and Joab addide not `the secounde wounde. Forsothe Joab and Abisai, his brother, pursueden Siba, the sone of Bochri.
11 Mmodzi mwa ankhondo a Yowabu anakayimirira pafupi ndi mtembo wa Amasa ndipo anati, “Aliyense amene amakonda Yowabu ndi aliyense amene ali wa Davide, atsatire Yowabu!”
In the meene tyme whanne `sum men of the children of Dauid, of the felowis of Joab, hadden stonde bisidis the deed bodi of Amasa, thei seiden, Lo! he that wolde be the felowe of Dauid for Joab.
12 Amasa anagona pakati pa msewu atasamba magazi ake, ndipo munthuyo anaona kuti asilikali onse amayima pamenepo. Atazindikira kuti aliyense amene ankafika pamene panali Amasa amayima, iye anamuchotsa mu msewu ndi kumukokera mʼmunda ndipo anamuphimba ndi nsalu.
Forsothe Amasa was bispreynt with blood, and lay in the myddil of the weie. Sum man siy this, that al the puple abood to se Amasa, and he remouyde Amasa fro the weie in to the feeld, and he hilide Amasa with a cloth, lest men passynge schulden abide for hym.
13 Amasa atachotsedwa pa msewu anthu onse anapita ndi Yowabu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
Therfor whanne he was remouyd fro the weie, ech man passide suynge Joab to pursue Siba, the sone of Bochri.
14 Seba anadutsa mafuko onse a Israeli mpaka ku Abeli ndi Beti-Maaka ndiponso chigawo chonse cha Abeli, amene anasonkhana pamodzi ndi kumutsata iye.
Forsothe Siba hadde passide bi alle the lynagis of Israel til in to Habela, and in to Bethmacha; and alle chosun men weren gaderid to hym.
15 Ankhondo onse pamodzi ndi Yowabu anafika ndi kumuzungulira Seba mu Abeli-Beti-Maaka. Iwo anapanga mzere wa nkhondo mpaka ku mzinda, ndipo unayangʼanana ndi malo otetezera a kunja. Pamene amalimbana ndi khoma kuti aligwetse,
Therfor thei camen, and fouyten ayens hym in Habela, and in Bethmacha, and cumpassiden the citee with strengthingis; and the citee was bisegid. Sotheli al the cumpany, that was with Joab, enforside to distrie the wallis.
16 mayi wina wanzeru anafuwula kuchokera mu mzindawo, “Tamverani! Tamverani! Muwuzeni Yowabu abwere pano kuti ndiyankhule naye.”
And a wijs womman of the citee criede an hiy, Here ye! here ye! seie ye to Joab, Neiye thou hidur, and Y schal speke with thee.
17 Yowabu anayandikira kumene kunali mayiyo, ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndinu Yowabu?” Iye anayankha kuti, “Ndine.” Mayiyo anati, “Tamverani zimene mtumiki wanu akuti anene.” Yowabu anayankha kuti, “Ndikumvetsera.”
And whanne he hadde neiyed to hir, sche seide to hym, Art thou Joab? And he answeride, Y am. To whom sche spak thus, Here thou the wordis of thin handmayde. Which Joab answeride, Y here.
18 Iye anapitiriza kunena kuti, “Kalekale ankanena kuti, ‘Kapeze yankho lako ku Abeli,’ ndipo nkhani imathera pamenepo.
And eft sche seide, A word was seid in eld prouerbe, Thei that axen, axe in Habela; and so thei profitiden.
19 Ife ndife anthu a mtendere ndi okhulupirika mu Israeli. Inu mukufuna kuwononga mzinda umene ndi mayi mu Israeli. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kufafaniza cholowa cha Yehova?”
Whethir Y am not, that answere treuthe to Israel? and sekist thou to distrie a citee, and to distrie a modir citee in Israel? whi castidist thou doun the eritage of the Lord?
20 Yowabu anayankha kuti, “Ayi ndisatero. Ine sindikufuna kuwufafaniza kapena kuwuwononga.
And Joab answeride, and seide, Fer be, fer be this fro me; Y `caste not doun, nether Y distrye.
21 Nkhani simeneyo ayi. Koma munthu wina wa ku dziko lamapiri la Efereimu, dzina lake Seba mwana wa Bikiri, wawukira mfumu Davide. Muperekeni munthuyo ndipo ine ndidzachoka pa mzinda uno.” Mayiyo anati kwa Yowabu, “Mutu wake tikuponyerani pa khoma pano.”
The thing hath not so it silf; but a man of the hil of Effraym, Siba, sone of Bochri, bi surname, reiside his hond ayens kyng Dauid; bitake ye him aloone, and we schulen go awei fro the citee. And the womman seide to Joab, Lo! his heed schal be sent to thee bi the wal.
22 Ndipo mayiyo anapita kwa anthu onse ndi malangizo ake anzeru, ndipo anadula mutu wa Seba mwana wa Bikiri ndipo anawuponya kwa Yowabu. Kotero iye analiza lipenga ndipo anthu ake anachoka pa mzindawo, aliyense nʼkubwerera kwawo. Ndipo Yowabu anabwerera kwa mfumu ku Yerusalemu.
Therfor the womman entride to al the puple, and sche spak to hem wiseli; whiche `castiden forth to Joab the heed of Siba, sone of Bochri, gird of. And Joab sownede with a trumpe, and thei departiden fro the citee, ech man in to hise tabernaclis; forsothe Joab turnede ayen to Jerusalem to the kyng.
23 Yowabu ndiye amalamulira gulu lonse la ankhondo. Benaya mwana wa Yehoyada amalamulira Akereti ndi Apeleti.
Therfor Joab was on al the oost of Israel; forsothe Benanye, sone of Joiada, was on Cerethi and Ferethi;
24 Adoramu amayangʼanira anthu ogwira ntchito ya thangata, Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika,
forsothe Adhuram was on tributis; forsothe Josaphat, sone of Achilud, was chaunceler; forsothe Siba was scryueyn;
25 Seva anali mlembi wa mfumu. Zadoki ndi Abiatara anali ansembe
forsothe Sadoch and Abiathar weren preestis;
26 ndipo Ira wa ku Yairi anali wansembe wa Davide.
forsothe Hira of Hiarith was preest of Dauid.

< 2 Samueli 20 >