< 2 Samueli 15 >

1 Patapita nthawi, Abisalomu anadzipezera galeta ndi akavalo pamodzi ndi amuna makumi asanu amene amathamanga patsogolo pake.
Therfor aftir these thingis Absolon made a chaar to hym, and knyytis, and fifti men, that schulden go bifor hym.
2 Iye amadzuka mmamawa ndi kuyima pa njira yopita ku chipata cha mzinda. Munthu wina aliyense akakhala ndi zodandaula zopita nazo kwa mfumu kuti akaweruze, Abisalomu amamuyitana iye ndi kumufunsa kuti, “Kodi ukuchokera ku limodzi mwa mafuko a Israeli?”
And Absolon roos eerli, and stood bisidis the entryng of the yate in the weie; and Absolon clepide to hym ech man, that hadde a cause that he schulde come to the doom of the kyng, and Absolon seide, Of what citee art thou? Which answeride, and seide, Of o lynage of Israel Y am, thi seruaunt.
3 Kenaka Abisalomu amanena kwa iye kuti, “Taona, madandawulo ako ndi abwino ndi oyenera, koma palibe woyimira mfumu woti akumvere.”
And Absolon answeride to hym, Thi wordis semen to me good and iust, but noon is ordeyned of the kyng to here thee. And Absolon seide, Who schal ordeyne me iuge on the lond,
4 Ndipo Abisalomu amawonjezera kunena kuti, “Ine ndikanangosankhidwa kukhala woweruza mʼdziko muno bwenzi munthu aliyense amene ali ndi madandawulo kapena milandu akubwera kwa ine ndipo ndikanaonetsetsa kuti chilungamo chachitika.”
that alle men that han cause come to me, and Y deme iustly?
5 Ndipo nthawi zonse amati munthu akasendera pafupi ndi kumugwandira, Abisalomu amatambalitsa dzanja lake, kumuyimiritsa munthuyo ndi kupsompsona.
But whanne a man cam to Absolon to greete hym, he helde forth the hond, and took, and kisside that man;
6 Abisalomu amachitira izi Aisraeli onse amene amabwera kwa mfumu kuti adzaweruzidwe ndipo Abisalomuyo anagwira mtima anthu a mu Israeli.
and Absolon dide this to al Israel, that cam to doom to be herd of the kyng; and Absolon drow awei the hertis of men of Israel.
7 Patapita zaka zinayi Abisalomu anati kwa mfumu, “Loleni ndipite ku Hebroni kuti ndikakwaniritse lonjezo limene ndinachita kwa Yehova.
Forsothe aftir foure yeer Absolon seide to kyng Dauid, Y schal go, and Y schal yelde my vowis, whiche Y vowide to the Lord in Ebron;
8 Pamene mtumiki wanu amakhala ku Gesuri ku Aramu, anachita lonjezo ili: ‘Ngati Yehova adzandibweretsadi ku Yerusalemu, ndidzapembedza Yehovayo mu Hebroni.’”
for thi seruaunt vowynge vowide, whanne he was in Gessur of Sirie, and seide, If the Lord bryngith ayen me in to Jerusalem, Y schal make sacrifice to the Lord.
9 Mfumu inati kwa iye, “Pita mu mtendere” Kotero iye anapita ku Hebroni.
And the kyng seide to hym, Go thou in pees. And Absolon roos, and yede in to Ebron.
10 Ndipo Abisalomu anatuma amithenga ake mwamseri kwa mafuko onse a Israeli kukanena kuti, “Mukangomva kulira kwa malipenga pamenepo munene kuti, ‘Abisalomu ndiye mfumu mu Hebroni.’”
Forsothe Absolon sente aspieris in to al the lynage of Israel, and seide, Anoon as ye heren the sown of clarioun, seye ye, Absolon schal regne in Ebron.
11 Anthu 200 ochokera mu Yerusalemu anapita naye Abisalomu. Iwo anayitanidwa monga alendo ndipo anapita osadziwa chilichonse pa nkhaniyi.
Forsothe twei hundrid men clepid of Jerusalem yeden with Absolon, and yede with symple herte, and outirli thei knewen not the cause.
12 Pamene Abisalomu amapereka nsembe, iye anayitanitsanso Ahitofele Mgiloni, mlangizi wa Davide, wa ku Gilo, kotero kuwukiraku kunakula kwambiri, ndipo anthu otsatira Abisalomu anapitirira kuchuluka.
Also Absolon clepide Achitofel of Gilo, the councelour of Dauid, fro his citee Gilo. And whanne he offride sacrifices a strong swerynge togidere was maad, and the puple rennynge togidere was encreessid with Absolon.
13 Munthu wina anabweretsa uthenga ndi kudzamuwuza Davide kuti, “Mitima ya Aisraeli onse ili pa Abisalomu.”
Therfor a messanger cam to Dauid, and seide, With al herte al Israel sueth Absolon.
14 Ndipo Davide anati kwa akuluakulu ake amene anali mu Yerusalemu. “Bwerani! Tiyeni tithawe, mwina palibe adzapulumuke kwa Abisalomu. Tiyeni tichoke msanga, mwina iye adzabwera msanga ndi kutipitirira, nʼkuwononga ife ndi mzinda wathu ndi lupanga.”
And Dauid seide to hise seruauntis that weren with hym in Jerusalem, Rise ye, and flee we; for noon ascaping schal be to us fro the face of Absolon; therfor haste ye to go out, lest he come, and ocupie vs, and fille on vs fallynge, and smyte the citee bi the scharpnesse of swerd.
15 Akuluakulu a mfumu anamuyankha kuti, “Antchito anu ndi okonzeka kuchita chilichonse chimene mbuye wathu mfumu mukufuna kuchita.”
And the seruauntis of the kyng seiden to hym, We thi seruauntis schulen performe gladli alle thingis, what euer thingis oure lord the kyng schal comaunde.
16 Mfumu inanyamuka pamodzi ndi banja lake lonse. Koma iye anasiya azikazi khumi kuti azisamalira nyumba yaufumu.
Therfor the kyng yede out, and al his hous, on her feet; and the king lefte ten wymmen concubyns, `that is, secundarie wyues, to kepe the hous.
17 Kotero mfumu inanyamuka pamodzi ndi anthu onse oyitsatira, ndipo anayima pamalo pena chapatalipo.
And the king yede out, and al Israel, on her feet, and the kyng stood fer fro the hous.
18 Ankhondo ake onse anayamba kuyenda pamaso pa Davide, ndipo Akereti ndi Apeleti, pamodzinso ndi Agiti okwanira 600 amene anamutsata kuchokera ku Gati, nawonso anayenda pamaso pake.
And alle hise seruauntis yeden bisidis him, and the legiouns of Cerethi and of Ferethi, and alle men of Geth `strong fiyters, sixe hundrid men, that sueden him fro Geth, yeden on foote bifor the kyng.
19 Mfumu inati kwa Itai Mgiti, “Nʼchifukwa chiyani iwe ukupita ndi ife? Bwerera ndipo ukakhale ndi mfumu Abisalomu. Iwe ndiwe mlendo munthu wothawa kwawo.
Forsothe the kyng seide to Ethai of Geth, Whi comest thou with vs? Turne thou ayen, and dwelle with the kyng, for thou art a pilgrym, and thou yedist out fro thi place.
20 Wangobwera dzulo lomweli, lero ndikutenge kuti uziyendayenda ndi ife, pamene ine sindikudziwa kumene ndikupita? Bwerera, ndipo tenga abale ako. Chifundo ndi kukhulupirika zikhale nawe.”
Thou camest yistirdai, and to dai thou art compellid to go out with vs. Sotheli Y schal go, whidur Y schal go; turne ayen, and lede ayen thi britheren with thee, and the Lord do mercy and treuthe with thee, for thou schewidist grace and feith.
21 Koma Itai anayankha mfumu kuti, “Pali Yehova wamoyo, kulikonse kumene mbuye wanga mfumu mudzakhala, kaya ndi moyo kapena imfa, mtumiki wanu adzakhala komweko.”
And Ethai answeride to the kyng, and seide, The Lord lyueth, and my lord the kyng lyueth, for in what euer place thou schalt be, my lord the kyng, ether in deeth ethir in lijf, there thi seruaunt schal be.
22 Davide anati kwa Itai, “Tiye pita nafe” Kotero Itai Mgiti anayenda pamodzi ndi anthu ake ndi mabanja amene anali naye.
And Dauid seide to Ethay, Come thou, and passe. And Ethai of Geth passide, and the kyng, and alle men that weren with hym, and the tother multitude.
23 Anthu onse a madera ozungulira analira mofuwula pamene anthu onsewo amadutsa. Mfumunso inawoloka chigwa cha Kidroni, ndipo anthu onse anayenda kulowera ku chipululu.
And alle men wepten with greet vois, and al the puple passide; and the kyng yede ouer the strond of Cedron, and al the puple yede ayens the weie of the olyue tree, that biholdith to deseert.
24 Zadoki anali nawonso, ndipo Alevi onse amene anali naye ananyamula Bokosi la Chipangano la Mulungu. Iwo anayika pansi Bokosi la Mulungulo ndipo Abiatara ankapereka nsembe mpaka pamene anthu onse anamaliza kutuluka mu mzinda.
Forsothe and Sadoch the preest cam, and alle the dekenes with hym, and thei baren the arke of boond of pees of God, and thei diden doun the arke of God; and Abiathar stiede, til al the puple was passid that yede out of the citee.
25 Kenaka mfumu inati kwa Zadoki, “Tenga Bokosi la Mulungu ubwerere nalo mu mzinda. Ngati ndidzapeza chifundo pamaso pa Yehova, adzandibweretsa kuti ndilionenso ndi malo ake okhalamo.
And the kyng seide to Sadoch, Bere ayen the arke of God in to the citee; if Y schal fynde grace in the iyen of the Lord, he schal lede me ayen, and he schal schewe to me that arke and his tabernacle.
26 Koma iye anati, ‘Akapanda kukondwera nane,’ chabwino, andichite chimene chimukomere.”
Sotheli if the Lord seith, Thou plesist not me; Y am redi, do he that, that is good bifor hym silf.
27 Mfumu inatinso kwa wansembe Zadoki, “Kodi siwe mlosi? Bwerera mu mzinda mwamtendere pamodzi ndi mwana wako Ahimaazi ndi Yonatani mwana wa Abiatara. Iwe ndi Abiatara tengani ana anu awiri.
And the kyng seide to Sadoch, preest, A! thou seere, `that is, profete, turne ayen in to the citee, with pees; and Achymaas, thi sone, and Jonathas, the sone of Abiathar, youre twei sones, be with you.
28 Ine ndidzadikira powolokera Yorodani ku chipululu mpaka nditalandira mawu ochokera kwa iwe ondiwuza mmene zilili zinthu.”
Lo! Y schal be hid in the feeldi places of deseert, til word come fro you, and schewe to me.
29 Kotero Zadoki ndi Abiatara ananyamula Bokosi la Mulungu lija nabwerera nalo ku Yerusalemu, ndipo anakakhala kumeneko.
Therfor Sadoch and Abiathar baren ayen the arke of God in to Jerusalem, and dwelliden there.
30 Koma Davide anapitirira ndi kukakwera phiri la Olivi akupita nalira. Anafunda kumutu koma sanavale nsapato. Anthu onse amene anali naye anafundanso kumutu, ndipo nawonso amalira pamene amapita.
Forsothe Dauid stiede on the hil of olyue trees, stiynge and wepynge, with the heed hilyd, and `goynge with nakid feet; but also al the puple that was with hym, stiede with the heed hilid, and wepte.
31 Tsono Davide anamva kuti, “Ahitofele ali pakati pa anthu owukira pamodzi ndi Abisalomu.” Choncho Davide anapemphera, “Inu Yehova, musandutse uphungu wa Ahitofele ukhale uchitsiru.”
Forsothe it was teld to Dauid, that Achitofel was in the sweryng togidere with Absolon; and Dauid seide, Lord, Y byseche, make thou fonned the counsel of Achitofel.
32 Davide atafika pamwamba pa phiri pomwe anthu ankapembedzerapo Mulungu, Husai Mwariki anadzakumana naye atangʼamba mkanjo wake ndi kudzithira fumbi kumutu.
And whanne Dauid stiede in to the hiyenesse of the hil, in which he schulde worschipe the Lord, lo! Cusi of Arath, with the cloth to-rent, and with the heed ful of erthe, cam to hym.
33 Davide anati kwa iye, “Ngati iwe upite ndi ine, udzakhala chondilemetsa.
And Dauid seide to hym, If thou comest with me, thou schalt be to me to charge; sotheli if thou turnest ayen in to the citee,
34 Koma ngati ubwerera ku mzinda ndi kukanena kwa Abisalomu kuti, ‘Inu mfumu ine ndidzakhala wantchito wanu.’ Mʼmbuyomu ndinali wantchito wa abambo anu koma tsopano ndidzakhala wantchito wanu. Ukatero udzandithandiza kulepheretsa malangizo a Ahitofele.
and seist to Absolon, Y am thi seruaunt, kyng, suffre thou me to lyue; as Y was the seruaunt of thi fadir, so Y schal be thi seruaunt; thou schalt distrye the counsel of Achitofel.
35 Kodi ansembe, Zadoki ndi Abiatara, sakukhala nawe kumeneko? Ukawawuze zonse zimene umamva mʼnyumba yaufumu.
Forsothe thou hast with thee Sadoch and Abiathar, preestis; and `thou schalt schewe ech word, what euer word thou schalt here in the hows of the kyng, to Sadoch and Abiathar, preestis.
36 Ana awo awiri, Ahimaazi wa Zadoki, ndi Yonatani mwana wa Abiatara ali nawo pamodzi, uzikawatuma kwa ine ndi china chilichonse chimene ukamve.”
Sotheli twei sones `of hem ben with hem, Achymaas, sone of Sadoch, and Jonathan, sone of Abiathar; and ye schulen sende bi hem to me ech word which ye schulen here.
37 Ndipo Husai bwenzi la Davide anafika ku Yerusalemu pamene Abisalomu amalowa mu mzinda.
Therfor whanne Chusi, freend of Dauid, cam in to the citee, also Absolon entryde in to Jerusalem.

< 2 Samueli 15 >