< 2 Samueli 13 >

1 Patapita nthawi, Amnoni mwana wa Davide anakonda Tamara, mlongo wa Abisalomu, mwana wa Davide, amene anali wokongola.
A potom se dogodi: Avesalom sin Davidov imaše lijepu sestru po imenu Tamaru, i zamilova je Amnon sin Davidov.
2 Amnoni sankagona tulo mpaka anadwala chifukwa cha Tamara mlongo wakeyo, pakuti iye anali asanagonepo ndi mwamuna ndipo zimaoneka kuti zinali zosatheka kuti achite chilichonse kwa iye.
I tužaše Amnon tako da se razbolje radi Tamare sestre svoje; jer bješe djevojka, te se Amnonu èinjaše teško da joj uèini što.
3 Koma Amnoni anali ndi mnzake dzina lake Yehonadabu mwana wamwamuna wa Simea, mʼbale wake wa Davide. Yonadabu anali munthu wochenjera kwambiri.
A imaše Amnon prijatelja, kojemu ime bješe Jonadav sin Same brata Davidova; i Jonadav bješe vrlo domišljat.
4 Iye anafunsa Amnoni, “Nʼchifukwa chiyani iwe mwana wa mfumu, umaoneka wowonda mmawa uliwonse? Bwanji wosandiwuza?” Amnoni anamuyankha kuti, “Ine ndamukonda Tamara, mlongo wa mʼbale wanga Abisalomu.”
I reèe mu: što se tako sušiš, carev sine, od dana na dan? ne bi li mi kazao? A Amnon mu reèe: ljubim Tamaru sestru Avesaloma brata svojega.
5 Yehonadabu anati, “Pita ukagone ndipo unamizire kudwala. Abambo ako akabwera kudzakuona, udzati kwa iwo, Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara abwere kuti adzandikonzere chakudya kuti ndidye. Adzandikonzere chakudyacho ine ndikumuona ndi kudya chili mʼmanja mwake.”
Tada mu reèe Jonadav: lezi u postelju svoju, i uèini se bolestan; pa kad doðe otac tvoj da te vidi, ti mu reci: neka doðe Tamara sestra moja da me nahrani, i da zgotovi pred mojim oèima jelo da gledam, i iz njezine ruke da jedem.
6 Kotero Amnoni anagona nakhala ngati akudwala. Mfumu itabwera kudzamuona, Amnoni anati kwa iyo, “Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara kuti abwere adzandipangire buledi wapamwamba ineyo ndikuona, kuti ndidye ali mʼmanja mwake.”
I Amnon leže i uèini se bolestan; i kad doðe car da ga vidi, reèe Amnon caru: neka doðe Tamara sestra moja i zgotovi preda mnom dva jelca da jedem iz njezine ruke.
7 Davide anatumiza mawu kwa Tamara ku nyumba yaufumu kuti, “Pita ku nyumba ya mlongo wako Amnoni ndipo ukamukonzere chakudya.”
Tada David posla k Tamari kuæi, i poruèi joj: idi u kuæu brata svojega Amnona i zgotovi mu jelo.
8 Choncho Tamara anapitadi ku nyumba ya mlongo wake Amnoni kumalo kumene ankagona. Anakanda ufa, nawumba buledi Amunoniyo akuona ndipo anaphika bulediyo.
I Tamara otide u kuæu brata svojega Amnona, i on ležaše; i uze brašna i zamijesi i zgotovi jelo pred njim i skuha.
9 Kenaka iye anatenga chiwaya ndipo anamupatsa bulediyo, koma iyeyo anakana. Amnoni anati “Uza aliyense atuluke muno.” Ndipo aliyense anatuluka.
Potom uze tavicu i izruèi preda nj; ali Amnon ne htje jesti, nego reèe: kažite neka izidu svi koji su kod mene. I izidoše svi.
10 Kenaka Amnoni anati kwa Tamara, “Bweretsa chakudya kuno, ku chipinda changa chogona kuti ndidye chili mʼmanja mwako.” Ndipo Tamara anatenga buledi amene anapanga ndi kubwera naye kwa mlongo wake ku chipinda chake.
Tada reèe Amnon Tamari: donesi to jelo u klijet da jedem iz tvoje ruke. I Tamara uze jelo što bješe zgotovila, i donese Amnonu bratu svojemu u klijet.
11 Koma atabweretsa kwa iye kuti adye, anamugwira ndipo anati, “Bwera ugone nane, iwe mlongo wanga.”
A kad mu pruži da jede, on je uhvati i reèe joj: hodi, lezi sa mnom, sestro moja!
12 Tamara anati kwa iye, “Ayi mlongo wanga! Usandikakamize. Zotere siziyenera kuchitika mu Israeli! Usachite chinthu choyipa chotere.
A ona mu reèe: ne, brate, nemoj me osramotiti, jer se tako ne radi u Izrailju, ne èini toga bezumlja.
13 Kodi ukuganiza bwanji za ine? Kodi manyazi anga ndidzawachotsa bwanji? Ndipo nanga iweyo? Udzakhalatu monga mmodzi mwa zitsiru zoyipitsitsa muno mu Israeli. Chonde kapemphe kwa mfumu. Sadzakuletsa kuti undikwatire.”
Kuda bih ja sa sramotom svojom? a ti bi bio kao koji od najgorih ljudi u Izrailju. Nego govori caru; on me neæe tebi odreæi.
14 Koma sanamvere zimene amanena Tamara ndipo popeza anali wamphamvu kuposa Tamarayo, iye anamugwirira.
Ali je on ne htje poslušati, nego savladavši je osramoti je i obleža je.
15 Atatero Amnoni anadana naye kwambiri. Iyeyo anamuda kuposa momwe anamukondera. Amnoni anati, “Dzuka ndipo tuluka!”
A poslije omrze na nju Amnon veoma, te mržnja kojom mržaše na nju bješe veæa od ljubavi kojom je prije ljubljaše. I reèe joj Amnon: ustani, odlazi.
16 Iye anayankha, “Ayi! Kundithamangitsa kukhala kulakwa kwakukulu kuposa zimene wachita kale kwa ine.” Koma anakana kumumvera.
A ona mu reèe: to æe biti veæe zlo od onoga koje si mi uèinio što me tjeraš. Ali je on ne htje poslušati.
17 Amnoni anayitana wantchito wake ndipo anati, “Mutulutse mkazi uyu muno ndipo utseke chitseko akatuluka.”
Nego viknu momka koji ga služaše, i reèe mu: vodi ovu od mene napolje, i zakljuèaj vrata za njom.
18 Choncho wantchito wakeyo anamutulutsa ndipo anatseka chitseko atatuluka. Tamara anali atavala mkanjo wokongoletsedwa kwambiri, pakuti ichi chinali chovala chimene ana aakazi a mfumu amene sanagonepo ndi mwamuna amavala.
A ona imaše na sebi šarenu haljinu, jer take haljine nošahu carske kæeri dok su djevojke. I sluga njegov izvede je napolje, i zakljuèa za njom vrata.
19 Tamara anatsira phulusa pamutu pake ndipo anangʼamba mkanjo wokongoletsedwa umene anavalawo. Iye anagwira manja ake kumutu ndipo anachoka, akulira mokweza pamene amapita.
Tada Tamara posu se pepelom po glavi i razdrije šarenu haljinu koju imaše na sebi, i metnu ruku svoju na glavu, i otide vièuæi.
20 Mlongo wake Abisalomu anati, “Kodi Amnoni uja mlongo wako wagona nawe? Khala chete mlongo wanga. Iye uja ndi mlongo wako ndipo usazilabadire.” Choncho Tamara anakhala mʼnyumba ya Abisalomu mlongo wake ngati woferedwa.
A brat njezin Avesalom reèe joj: da nije Amnon brat tvoj bio s tobom? ali, sestro moja, æuti, brat ti je, ne misli o tom. I tako osta Tamara osamljena u kuæi brata svojega Avesaloma.
21 Mfumu Davide itamva zimenezi, inakwiya kwambiri.
I car David èuvši sve ovo razgnjevi se vrlo.
22 Abisalomu sananene mawu aliwonse kwa Amnoni; abwino kapena oyipa. Iye anamuda Amunoniyo chifukwa anachititsa manyazi mlongo wake Tamara.
Avesalom pak ne govoraše s Amnonom ni ružno ni lijepo; jer Avesalom mržaše na Amnona što mu osramoti sestru Tamaru.
23 Patapita zaka ziwiri, pamene wometa nkhosa za Abisalomu anali ku Baala-Hazori pafupi ndi malire a fuko la Efereimu, iye anayitana ana onse aamuna a mfumu kuti apite kumeneko.
A poslije dvije godine kad se strizijahu ovce Avesalomove u Val-Asoru, koji je kod Jefrema, on pozva sve sinove careve.
24 Abisalomu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Ometa nkhosa za mtumiki wanu anabwera. Chonde mfumu ndi akuluakulu anu mubwere kudzakhala nane?”
I doðe Avesalom k caru i reèe mu: evo, sad se strigu ovce sluzi tvojemu; neka poðe car i sluge njegove sa slugom svojim.
25 Mfumu inayankha kuti, “Ayi mwana wanga, tisapite tonsefe. Tidzakhala cholemetsa kwa iwe.” Ngakhale Abisalomu anayesetsa kuwumiriza mfumuyo, inakana kupita. Mʼmalo mwake inangomudalitsa Abisalomuyo.
Ali car reèe Avesalomu: nemoj, sine, nemoj da idemo svi, da ti ne budemo na tegotu. I premda navaljivaše, opet ne htje iæi, nego ga blagoslovi.
26 Kenaka Abisalomu anati, “Ngati sizitero, chonde mulole mʼbale wanga Amnoni apite nane.” Mfumu inamufunsa kuti, “Apite nawe chifukwa chiyani?”
A Avesalom reèe: kad ti neæeš, a ono neka ide s nama Amnon brat moj. A car mu reèe: što da ide s tobom?
27 Koma Abisalomu anamuwumiriza, kotero analola kuti Amnoni pamodzi ndi ana onse a mfumu apite naye.
Ali navali Avesalom na nj, te pusti s njim Amnona i sve sinove carske.
28 Abisalomu analamula antchito ake kuti, “Tamverani! Amnoni akakaledzera ndi vinyo ndipo ine ndikakanena kuti, ‘Mukantheni Amnoni,’ pamenepo mukamuphe. Musakachite mantha. Kodi ine sindinakulamuleni? Mukhale amphamvu ndipo mulimbe mtima.”
Tada Avesalom zapovjedi momcima svojim govoreæi: pazite, kad se srce Amnonu razveseli od vina, i ja vam reèem: ubijte Amnona; tada ga ubijte; ne bojte se, jer vam ja zapovijedam, budite slobodni i hrabri.
29 Kotero antchito a Abisalomu anachita kwa Amnoni zimene Abisalomu anawalamula. Kenaka ana onse a mfumu anayimirira ndipo anakwera pa abulu awo nathawa.
I uèiniše s Amnonom sluge Avesalomove kako im zapovjedi Avesalom. Tada ustaše svi sinovi carevi i pojahaše svak svoju mazgu i pobjegoše.
30 Ali mʼnjira, Davide anamva mphekesera yakuti, “Abisalomu wakantha ana onse a mfumu ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene watsala.”
A dokle još bijahu na putu, doðe glas Davidu da je Avesalom pobio sve sinove careve, da nije ostao od njih nijedan.
31 Mfumu inayimirira, ningʼamba zovala zake ndi kugona pa dothi. Antchito ake onse anayimirira pomwepo atangʼamba zovala zawo.
Tada ustavši car razdrije haljine svoje, i leže na zemlju, i sve sluge njegove koje stajahu oko njega razdriješe haljine svoje.
32 Koma Yehonadabu mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anati, “Mbuye wanga mfumu musaganize kuti wapha ana onse a mfumu; wafa ndi Amnoni yekha. Awa ndiwo akhala maganizo a Abisalomu kuyambira tsiku limene Amnoni anagwirira mlongo wake Tamara.
A Jonadav sin Same brata Davidova progovori i reèe: neka ne govori gospodar moj da su pobili svu djecu, careve sinove; poginuo je samo Amnon, jer Avesalom bješe tako naumio od onoga dana kad Amnon osramoti Tamaru sestru njegovu.
33 Mbuye wanga mfumu musavutike ndi maganizo ndi nkhani yoti ana onse a mfumu afa. Wafa ndi Amnoni yekha.”
Neka dakle car gospodar moj ne misli o tom u srcu svojem govoreæi: svi sinovi carevi pogiboše; jer je samo Amnon poginuo.
34 Nthawi imeneyi nʼkuti Abisalomu atathawa. Tsono munthu amene amalondera anayangʼana ndipo anaona anthu ambiri pa msewu wa kumadzulo kwake, akubwera kutsetsereka phiri. Mlondayo anapita kukawuza mfumu kuti, “Ndikuona anthu pa njira ya Horonaimu, mʼmbali mwa phiri.”
A Avesalom pobježe. A momak na straži podiže oèi svoje i ugleda, a to mnogi narod ide k njemu pokraj gore.
35 Yehonadabu anati kwa mfumu, “Taonani ana a mfumu afika. Zachitika monga momwe mtumiki wanu ananenera.”
I Jonadav reèe caru: evo idu sinovi carevi; kao što je kazao sluga tvoj, tako je bilo.
36 Pamene amatsiriza kuyankhula, ana a mfumu analowa, akulira mofuwula. Mfumunso ndi antchito ake onse analira mokhudzidwa.
I kad izreèe, a to sinovi carevi doðoše, i podigavši glas svoj plakaše; a i car i sve sluge njegove plakaše vrlo.
37 Abisalomu anathawa, napita kwa Talimai mwana wa Amihudi, mfumu ya ku Gesuri. Koma mfumu Davide inalira mwana wake tsiku ndi tsiku.
Avesalom pak pobježe i otide k Talmaju sinu Amijudovu caru Gesurskom. A David plakaše za sinom svojim svaki dan.
38 Abisalomu atathawa ndi kupita ku Gesuri, anakhala kumeneko zaka zitatu.
A kad Avesalom uteèe i doðe u Gesur, osta ondje tri godine.
39 Ndipo Davide anagwidwa ndi chifundo chofuna kumulondola Abisalomu pakuti anali atatonthozedwa pa imfa ya Amnoni.
Potom zaželje car David otiæi k Avesalomu, jer se utješi za Amnonom što pogibe.

< 2 Samueli 13 >