< 2 Samueli 11 >

1 Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Davide anatumiza Yowabu ndi ankhondo a mfumu pamodzi ndi gulu lonse lankhondo la Aisraeli. Iwo anawononga Aamoni ndi kuzungulira mzinda wa Raba. Koma Davide anatsala ku Yerusalemu.
A kad proðe godina, u vrijeme kad carevi idu na vojsku, posla David Joava i sluge svoje s njim, i svega Izrailja, te potirahu sinove Amonove, i opkoliše Ravu; a David osta u Jerusalimu.
2 Tsiku lina cha kumadzulo Davide anadzuka pa bedi lake ndipo ankayenda pamwamba pa nyumba yake. Ali pa dengapo anaona mkazi akusamba. Mkaziyo anali wokongola kwambiri.
I pred veèe usta David s postelje svoje, i hodajuæi po krovu carskoga dvora ugleda s krova ženu gdje se mije, a žena bijaše vrlo lijepa na oèi.
3 Ndipo Davide anatuma munthu wina kuti akafufuze za iye. Munthuyo anati, “Kodi uyu si Batiseba, mwana wa Eliamu, mkazi wa Uriya Mhiti?”
I David posla da propitaju za ženu i rekoše: nije li to Vitsaveja kæi Elijamova žena Urije Hetejina?
4 Ndipo Davide anatumiza amithenga kwa iye kukamuyitana. Batiseba anabwera kwa Davide ndipo anagona naye. (Nʼkuti mkaziyu atayeretsedwa ku masiku ake osamba). Kenaka anabwerera ku nyumba yake.
I David posla poslanike da je dovedu; i kad doðe k njemu, on leže s njom, a ona se bješe oèistila od neèistote svoje; poslije se vrati svojoj kuæi.
5 Mkaziyo anakhala woyembekezera ndipo anatumiza mawu kwa Davide kunena kuti, “Ine ndine woyembekezera.”
I zatrudnje žena, te posla i javi Davidu govoreæi: trudna sam.
6 Ndipo Davide anatumiza mawu awa kwa Yowabu: “Nditumizire Uriya Mhiti.” Ndipo Yowabu anamutumiza kwa Davide.
Tada David posla k Joavu i poruèi: pošlji mi Uriju Hetejina. I posla Joav Uriju k Davidu.
7 Uriya atafika kwa Davide, Davide anamufunsa za momwe analili Yowabu, za asilikali ndi momwe nkhondo inkayendera.
I kad Urija doðe k njemu, zapita ga David kako je Joav i kako je narod i kako ide rat.
8 Kenaka Davide anati kwa Uriya, “Pita ku nyumba yako ukapumule.” Choncho Uriya anachoka ku nyumba yaufumu, ndipo mfumuyo inatumiza mphatso kwa Uriya.
Potom reèe David Uriji: idi kuæi svojoj, i operi noge svoje. I Urija izide iz careva dvora, a za njim iznesoše jelo carsko.
9 Koma Uriya anagona pa chipata cha nyumba yaufumu pamodzi ndi antchito onse a mbuye wake ndipo sanapite ku nyumba yake.
Ali Urija leže na vratima dvora careva sa svijem slugama gospodara svojega, i ne otide kuæi svojoj.
10 Davide atawuzidwa kuti, “Uriya sanapite ku nyumba yake.” Iye anafunsa kuti, “Kodi iwe sunachokera kutali? Nʼchifukwa chiyani sunapite ku nyumba yako?”
I javiše Davidu govoreæi: Urija nije otišao kuæi svojoj. A David reèe Uriji: nijesi li došao s puta? zašto ne ideš kuæi svojoj?
11 Uriya anayankha Davide kuti, “Bokosi la Chipangano ndi Israeli ndiponso Yuda akukhala mʼmatenti, ndipo mbuye wanga Yowabu ndi ankhondo anu mbuye wanga amanga misasa pa mtetete. Ine ndingapite bwanji ku nyumba yanga kukadya ndi kumwa ndiponso kugona ndi mkazi wanga? Pali inu wamoyo, ine sindidzachita chinthu chimenechi.”
A Urija reèe Davidu: kovèeg i Izrailj i Juda stoje po šatorima, i Joav gospodar moj i sluge gospodara mojega stoje u polju, pa kako bih ja ušao u kuæu svoju da jedem i pijem i spavam sa ženom svojom? Tako ti bio živ i tako bila živa duša tvoja, neæu to uèiniti.
12 Ndipo Davide anati kwa iye, “Ukhale konkuno tsiku lina limodzi, ndipo mawa ndikulola kuti upite.” Kotero Uriya anakhala mu Yerusalemu tsiku limenelo ndi tsiku linalo.
Tada reèe David Uriji: ostani ovdje još danas, pa æu te sjutra otpustiti. Tako osta Urija u Jerusalimu onaj dan i sjutradan.
13 Davide anayitana Uriya nadya ndi kumwa naye, ndipo Davide anamuledzeretsa. Koma madzulo Uriya anapita kukagona pa mphasa pamodzi ndi antchito a mbuye wake. Iye sanapite ku nyumba yake.
I pozva ga David da jede i pije s njim, te ga opije. A uveèe otide, te leže na postelju svoju sa slugama gospodara svojega, a kuæi svojoj ne otide.
14 Mmawa Davide analemba kalata kwa Yowabu ndipo anayitumiza ndi Uriya.
A ujutru napisa David knjigu Joavu, i posla po Uriji.
15 Mʼkalatayo analembamo kuti, “Uriya mumuyike patsogolo penipeni, pamene pali nkhondo yoopsa. Ndipo mumusiye yekha kuti akanthidwe ndi kufa.”
A u knjizi pisa i reèe: namjestite Uriju gdje je najžešæi boj, pa se uzmaknite od njega da bi ga ubili da pogine.
16 Kotero Yowabu atawuzinga mzindawo, anamuyika Uriya pamalo pamene amadziwa kuti pali asilikali amphamvu.
I Joav opkolivši grad namjesti Uriju na mjesto gdje je znao da su najhrabriji ljudi.
17 Ankhondo a mu mzindawo atabwera kudzamenyana ndi Yowabu, anthu ena a gulu la ankhondo la Davide anaphedwa ndipo Uriya Mhiti uja anaphedwanso.
I izidoše ljudi iz grada i pobiše se s Judom. I pogibe iz naroda nekoliko sluga Davidovijeh; pogibe i Urija Hetejin.
18 Yowabu anatumiza wamthenga kwa Davide kukafotokoza mwatsatanetsatane za nkhondoyo.
Tada Joav posla k Davidu, i javi mu sve što bi u boju.
19 Iye anamulangiza wa mthengayo kuti, “Pamene ukatsiriza kufotokozera mfumu za ku nkhondozi,
I zapovjedi glasniku govoreæi: kad pripovjediš caru sve što je bilo u boju,
20 mfumu ikapsa mtima, ndipo akakakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani munapita pafupi ndi mzindawo kukamenya nkhondo? Inu simunadziwe kuti atha kukuponyerani mivi kuchokera pa khoma?
Ako se razgnjevi car i reèe ti: zašto ste išli tako blizu grada da se bijete? zar nijeste znali kako se strijelja s grada?
21 Kodi anapha Abimeleki mwana wa Yerubeseti ndani? Kodi mkazi sanamuponyere mphero kuchokera pa khoma? Kotero kuti anakafera ku Tebezi. Nʼchifukwa chiyani munafika pafupi ndi khoma?’ Ngati iye akafunsa zimenezi, iwe ukanene kwa iye kuti, ‘Mtumiki wanunso Uriya Mhiti wafa.’”
Ko je ubio Avimeleha sina Jeruvesetova? nije li žena bacila na nj komad žrvnja sa zida, te pogibe u Tevesu? zašto ste išli blizu zida? tada reci: poginuo je i sluga tvoj Urija Hetejin.
22 Mthengayo ananyamuka, ndipo atafika anamuwuza Davide zonse zimene Yowabu anamutuma kuti akanene.
I otide glasnik, i došavši javi Davidu sve za što ga je poslao Joav.
23 Mthengayo anati kwa Davide, “Anthuwo anatiposa mphamvu ndipo anabwera kudzalimbana nafe poyera, koma ife tinawabwezera ku chipata cha mzindawo.
I reèe glasnik Davidu: bijahu jaèi od nas, i izidoše u polje na nas, ali ih uzbismo do vrata gradskih.
24 Ndipo anthu oponya mivi anatiponyera kuchokera pa khoma, anthu ena a mfumu afa. Kuwonjezera apo, mtumiki wanu Uriya Mhiti wafanso.”
A strijelci stadoše strijeljati na sluge tvoje sa zida, i pogibe nekoliko sluga carevijeh, tako i sluga tvoj Urija Hetejin pogibe.
25 Davide anamuwuza mthengayo kuti, “Ukanene izi kwa Yowabu: ‘Zimenezi zisakukhumudwitse; lupanga limapha wina nthawi zinanso wina. Limbikitsa nkhondo pa mzindawo ndipo uwuwononge!’ Ukanene zimenezi pomulimbikitsa Yowabu.”
Tada reèe David glasniku: ovako reci Joavu: ne budi zlovoljan za to; jer maè proždire sad ovoga sad onoga; udri još jaèe na grad i raskopaj ga. Tako ga ohrabri.
26 Mkazi wa Uriya atamva kuti mwamuna wake wafa, analira maliro.
A žena Urijina èuvši da je poginuo muž njezin Urija, plaka za mužem svojim.
27 Nthawi yolira maliro itatha, Davide anamubweretsa ku nyumba yake, ndipo anakhala mkazi wake nabala mwana wamwamuna. Koma Yehova sanakondwe ndi zimene Davide anachitazo.
A kad proðe žalost, posla David i uze je u kuæu svoju, i ona mu posta žena, i rodi mu sina. Ali ne bješe po volji Gospodu što uèini David.

< 2 Samueli 11 >